Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

NYIMBO 13

Khristu ni Citsanzo Cathu

Khristu ni Citsanzo Cathu

(1 Petulo 2:21)

  1. 1. Timayamikila,

    Cikondi ca M’lungu—

    Anapeleka Yesu Mwana wake.

    Khristu’a naonetsa,

    Citsanzo cabwino—

    Anayeletsa dzina Ia M’lungu.

  2. 2. Mau a Yehova,

    Anamuthandiza,

    Kuti akhale wokhulupilika.

    Anatumikila

    M’lungu mokondwela,

    Tidzatengela citsanzo cake.

  3. 3. Khristu’a natipatsa

    Citsanzo cabwino—

    Anatamanda Yehova Atate.

    Ise tilengeze

    Ufumu wa M’lungu.

    Tidzalandila moyo wosatha.

(Onaninso Yoh. 8:29; Aef. 5:2; Afil. 2:5-7)