Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

NYIMBO 137

Azimayi Okhulupilika, Alongo Athu

Azimayi Okhulupilika, Alongo Athu

(Aroma 16:2)

  1. 1. Sara, Estere, Mariya na Rute—

    Iwo anali akazi abwino.

    Anali odzipeleka kwa M’lungu,

    Timaŵadziŵa na maina awo.

    Panali ena osachulidwa,

    Naonso anali okhulupilika.

  2. 2. Onsewa ni zitsanzo za bwinodi.

    Anali akazi olimba mtima.

    Anali acikondi na ubwino.

    Zocita zawo ise titengele.

    Tiyamikile alongo athu,

    Amatumikila mokhulupilika.

  3. 3. Atsikana, akazi amasiye,

    Mumagwila nchito yanu mwakhama;

    Mumadzipeleka mofunitsitsa.

    Musaope Yehova ali namwe,

    Limbikilani mpaka mapeto;

    Mudzasangalala, mudzadalitsidwa.

(Onaninso Afil. 4:3; 1 Tim. 2:9, 10; 1 Pet. 3:4, 5.)