Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Kodi Nthawi Ili Bwanji?

Kodi Nthawi Ili Bwanji?

MUKAFUNA kudziŵa nthawi, kodi mumacita ciani? Mosakayikila mumayang’ana pa nkholoko yanu. Ngati mnzanu wakufunsani nthawi, kodi mungamuyankhe bwanji? Pali njila zosiyana-siyana zochulila nthawi. Kodi njila zimenezo n’ziti?

Cabwino, tikambe kuti papita ola limodzi na maminetsi 30 kucokela pa 12:00hrs masana. Mnzanuyo mungamuuze kuti nthawi ili 1:30. Koma potengela dela limene mumakhala komanso zimene anthu anazoloŵela kwanuko, mwina mungakambe kuti nthawi ili 13:30. Kachulidwe kameneka ka nthawi n’kotengela nkholoko yoonetsa maola 24 pa tsiku. Komanso kuli madela ena kumene anthu amachula nthawi imeneyi kuti “hafu 1,” kutanthauza kuti papita maminetsi 30 kucokela pamene 1 koloko yakwana.

Monga munthu amene amaŵelenga Baibo, mwina mumafuna kudziŵa kuti anthu m’nthawi yakale anali kuchula bwanji nthawi. Panali njila zosiyana-siyana zochulila nthawi. Malemba Aciheberi amachula nthawi monga “m’maŵa kwambili,” “m’maŵa,” “masana,” na ‘madzulo.’ (Gen. 8:11; 19:27; 1 Maf. 18:26) Komabe, nthawi zina iwo anali kuchula nthawi mwacindunji kwambili kuposa pamenepa.

M’nthawi yakale, kaŵili-kaŵili kunali kukhala alonda, maka-maka usiku. Zaka mahadiledi ambili Yesu asanabadwe, Aisiraeli anali kugaŵa usiku m’zigawo zitatu, zimene anali kuzicha maulonda. (Sal. 63:6, ftn.) Oweruza 7:19 imakamba za “ulonda wapakati pa usiku.” Pofika m’nthawi ya Yesu, Ayuda anali atatengela kaŵelengedwe ka Agiriki na Aroma, kokhala na zigawo zinayi za maulonda a usiku.

Kangapo konse, mabuku a Uthenga Wabwino amachulako za maulonda amenewa. Mwacitsanzo, Mateyu anakamba kuti inali nthawi ya “ulonda wacinayi” pamene Yesu anali kuyenda pamwamba pa madzi, kuyandikila ngalawa imene munali ophunzila ake. (Mat. 14:25) Komanso m’fanizo lina, Yesu anati: “Odala ndi akapolo amene mbuye wawo pofika adzawapeza akudikila! . . . Iwo ndi odala ndithu ngati atawapeza akudikilabe ngakhale atafika pa ulonda waciwili kapenanso wacitatu!”—Luka 12:37, 38.

Yesu anachula maulonda onse anayi pamene anauza ophunzila ake kuti: “Conco khalani maso, pakuti simukudziŵa nthawi yobwela mwininyumba. Simukudziŵa ngati adzabwele madzulo, pakati pa usiku, atambala akulila, kapena m’mawa.” (Maliko 13:35) Ulonda woyamba pa maulonda amenewo, wa “madzulo,” unali kuyamba dzuŵa likaloŵa, mpaka ca m’ma 21:00hrs madzulo. Ulonda waciŵili, wa “pakati pa usiku,” unali kuyamba ca m’ma 21:00hrs mpaka pakati pa usiku. Ulonda wacitatu, wa pa nthawi imene “atambala akulila,” unali kuyamba pakati pa usiku, mpaka ca m’ma 03:00hrs usiku. Zioneka kuti ni nthawi ya ulonda umenewu pamene tambala analila, pa usiku umene Yesu anagwidwa na adani ake. (Maliko 14:72) Ulonda wacinayi, wa “m’maŵa,” unali kuyamba ca m’ma 03:00hrs, mpaka m’maŵa pa nthawi ya kutuluka dzuŵa.

Conco, olo kuti m’nthawi yakale anthu analibe nkholoko, anali na njila yodziŵila nthawi, ya masana komanso ya usiku.