KUONJEZELA LUSO LANU MU ULALIKI

Mmene Tingatsogozele Phunzilo m’Kabuku ka Uthenga Wabwino

Mmene Tingatsogozele Phunzilo m’Kabuku ka Uthenga Wabwino
  1. Ŵelengani funso lili m’zilembo zakuda lokhala ndi nambala kuti muthandize mwininyumba kumvetsa mfundo yaikulu.

  2. Ŵelengani ndime ili munsi mwa funsolo.

  3. Ŵelengani malemba olembedwa mopendeketsa, ndipo funsani mafunso mwaluso kuti muthandize mwininyumba kuzindikila mmene malembawo akuyankhila funsolo.

  4. Ngati pali ndime ina munsi mwa funso limenelo, tsatilaninso malangizo amene alembedwa pa 2 ndi 3 pamwambapa. Ngati pa jw.org pali vidiyo yogwilizana ndi funsolo, mungaonetse mwininyumba vidiyoyo mkati mwa phunzilo lanu.

  5. Pofuna kutsimikizila kuti mwininyumba wamvetsetsa mfundo imene mwakambilana, mufunseninso funso lili m’zilembo zakuda.