Mphindi Iliyonse
Citani daunilodi:
1. Moyo wathu uli ngati mame
Amene samakhalitsa.
Tiyeni tisonyeze cikondi
Kwa ena pamene tili ndi nthawi.
(KOLASI)
Ngati ndingazengeleze, ndingataye nthawi
Yofunika kuonetsa cikondi
Okondedwa anga onse. Sin’dziwa za mawa
Sindifuna kukadziimba mlandu.
Ndidzagwilitsila nchito bwino mphindi iliyonse.
2. Poona cikondi komanso
Kukongola kwa cilengedwe
Ca M’lungu, zimandilimbikitsa
Kuti ndizimutumikila mwakhama.
(KOLASI)
Ngati ndingazengeleze, ndingataye nthawi
Yofunika kuonetsa cikondi
Okondedwa anga onse. Sin’dziwa za mawa
Sindifuna kukadziimba mlandu.
Ndidzagwilitsila nchito bwino mphindi iliyonse.
(BILIJI)
M’tsogolo M’lungu adzatipatsa
Dziko labwino zedi.
Pamene tikuyembekezela
Tim’patse nthawi yathu.
(KOLASI)
Ngati ndingazengeleze, ndingataye nthawi
Yofunika kuonetsa cikondi
Okondedwa anga onse. Sindidziwa za mawa
Sindifuna kukadziimba mlandu.
Conco ndidzagwilitsa nchito bwino mphindi iliyonse.

