NKHANI ZA PADZIKO LONSE

Zechariah Wa wakhala ali m’ndende ku Singapore kuyambira mu August 2025

A Mboni za Yehova Anamangidwa Chifukwa cha Zimene Amakhulupirira​—Potengera Dera

A Mboni za Yehova Anamangidwa Chifukwa cha Zimene Amakhulupirira​—Potengera Dera

Pofika mu December 2025, a Mboni za Yehova oposa 261 padziko lonse anamangidwa chifukwa cha zimene amakhulupirira.

Gawo 18 la malamulo a padziko lonse okhudza ufulu wa anthu limanena kuti anthu ali ndi ufulu wa maganizo, chikhulupiriro komanso chipembedzo. Ngakhale zili choncho, a Mboni za Yehova m’mayiko ena sakupatsidwa ufulu umenewu ndipo amamangidwa komanso kuzunzidwa chifukwa cha zimene amakhulupirira kapena chifukwa chokana kulowa usilikali.

“Muzikumbukira amene ali mʼndende ngati kuti mwamangidwa nawo limodzi.”​—Aheberi 13:3.