Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Nyimbo 137

Tithandizeni Kukhala Olimba Mtima

Tithandizeni Kukhala Olimba Mtima

(Machitidwe 4:29)

  1. Polalikira Ufumu,

    Kukweza dzina lanu.

    Anthu ena amatsutsa,

    Ndiponso kutinyoza.

    Koma sitiwaopa

    Timamvera inu nokha.

    Choncho Yehova, tikupempha

    Mutipatse mzimu wanu.

    (KOLASI)

    Polalikira uthenga,

    Mutichotsere mantha.

    Tikhale olimba mtima

    Anthu amve uthenga.

    Amagedo ikufika,

    Tikhale olimba mtima,

    Tithandizeni Yehova.

    Tikupempha.

  2. Pamene tichita mantha,

    Mudziwa ndife fumbi.

    Mudzatithandiza ndithu

    Paja munalonjeza.

    Imvani kuopseza,

    Kwa anthu odana nafe.

    Tithandizeni, tisaope.

    Tikhale olimba mtima.

    (KOLASI)

    Polalikira uthenga,

    Mutichotsere mantha.

    Tikhale olimba mtima

    Anthu amve uthenga.

    Amagedo ikufika,

    Tikhale olimba mtima,

    Tithandizeni Yehova.

    Tikupempha.