NYIMBO 69
Pitirizani Kulalikira za Ufumu
-
1. Pitani patsogolo ndithu
Polalikira konse.
Muthandize anthu ofatsa,
Akonde choonadi.
Ndi mwayidi kutumikira;
Tikonde kulalikira.
Chitirani umboni M’lungu;
Ndi dzina lake loyera.
(KOLASI)
Pitirizani kulalikira
padziko lonse.
Pitirizani kukhala
okhulupirikabe.
-
2. Tipite patsogolo tonse,
Amuna ndi akazi.
Odzozedwa ndi nkhosa zina
Tisasiye cho’nadi.
Ndi kofunika kuti anthu
Amve uthenga wabwino.
Yehova atipatsa mphamvu;
Ndipo sitiopa kanthu!
(KOLASI)
Pitirizani kulalikira
padziko lonse.
Pitirizani kukhala
okhulupirikabe.
(Onaninso Sal. 23:4; Mac. 4:29, 31; 1 Pet. 2:21.)