NSANJA YA OLONDA (YOPHUNZIRA) February 2020

M’magaziniyi muli nkhani zophunzira kuyambira April 6–May 3, 2020.

Atate Wathu Yehova Amatikonda Kwambiri

Tisamakayikire kuti Atate wathu Yehova amatikonda komanso kutisamalira ndipo sangatisiye.

Timakonda Kwambiri Atate Wathu Yehova

Onani zinthu zimene tingachite posonyeza kuti timakonda kwambiri Atate wathu Yehova.

Muzipewa Nsanje Kuti Muzikhala Mwamtendere

Nthawi zina tikhoza kumavutika ndi mtima wa nsanje. Onani zimene tingachite kuti tipewe nsanje n’kumakhala mwamtendere ndi anzathu.

Muzilola Kuti Yehova Azikutonthozani

Hana, mtumwi Paulo ndi Mfumu Davide ankavutika ndi nkhawa. Kodi tingaphunzire chiyani tikaganizira mmene Yehova anawatonthozera?

MBIRI YA MOYO WANGA

Ndadalitsidwa Chifukwa Chotsatira Zimene Ndinaphunzira kwa Anthu Ena

Léonce Crépeault akufotokoza mmene chitsanzo cha anthu okhulupirika chinamuthandizira kuthetsa mantha ake komanso kusangalala ndi madalitso ambiri pa zaka pafupifupi 58 zimene wachita utumiki wa nthawi zonse.

Kodi Mukudziwa?

Kodi zimene asayansi apeza zikutsimikizira bwanji kuti Belisazara anali mfumu ku Babulo?