Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso

M’Baibulo muli mfundo zothandiza ndipo zikhoza kugwiritsidwa ntchito kulikonse. Ana ayenera kuphunzira zimene Atate wawo wakumwamba amanena osati zimene anthu ena amanena.

Zimene Ana Amafuna Kwa Makolo Awo

Cholinga cha bukuli ndi chofuna kuthandiza ana komanso amene akuwawerengera bukuli kuti azikambirana momasuka nkhani zofunika.

MUTU 1

Chifukwa Chake Yesu Anali Mphunzitsi Waluso

Kodi Yesu ankaphunzitsa zinthu zotani? Nanga zomwe ankaphunzitsazo anazitenga kuti?

MUTU 2

Kalata Yochokera kwa Mulungu

Kalatayi imapezeka m’buku lofunika kwambiri kuposa mabuku ena onse.

MUTU 3

Amene Anapanga Zinthu Zonse

Ndani analenga mbalame ndi kuziphunzitsa kuimba? Ndani analenga udzu? Ndani anakulenga?

MUTU 4

Mulungu Ali ndi Dzina Lake

Tonsefe tili ndi mayina. Kodi dzina la Mulungu umalidziwa? N’chifukwa chiyani dzina lake ndi lofunika?

MUTU 5

“Uyu Ndiye Mwana Wanga”

N’chiyani chinapangitsa Yesu kukhala munthu wapadera kwambiri?

MUTU 6

Mphunzitsi Waluso Anatumikira Anthu Ena

Kodi umasangalala munthu wina akakupangira chinthu chabwino? Tonse timasangalala, ndipo Mphunzitsi Waluso ankadziwa zimenezi.

MUTU 7

Kumvera Kudzakuteteza

Ana amaphunzira zinthu kuchokera kwa akuluakulu. Ndipo Mulungu akatiuza kuti tichite zinazake sitiyenera kukaikira ngati zilidi zofunika.

MUTU 8

Mulungu Ndi Wamkulu Kuposa Aliyense

Pali angelo ena abwino komanso pali ena oipa.

MUTU 9

Tifunika Kukana Ziyeso

Kodi ungachite chiyani ngati munthu wina atakuuza kuti uchite zinthu zoipa?

MUTU 10

Yesu Ali ndi Mphamvu Kuposa Ziwanda

Sitiyenera kuopa ziwanda komabe tiyenera kukhala osamala kuti zisatipusitse.

MUTU 11

Angelo a Mulungu Amatithandiza

Angelo a Mulungu amathandiza anthu omwe amakonda Yehova ndi kumutumikira.

MUTU 12

Yesu Atiphunzitsa Kupemphera

Mungathe kupemphera kwa Mulungu nthawi iliyonse ndipo iye adzamva mapemphero anu.

MUTU 13

Amene Anakhala Ophunzira a Yesu

Kodi ophunzira a Yesu anali anthu otani?

MUTU 14

Chifukwa Chake Tiyenera Kukhululukira Ena

Yesu anafotokoza nkhani pofuna kutiphunzitsa kufunika kokhululukira ena.

MUTU 15

Phunziro la Kukhala Wokoma Mtima

Mungaphunzire zambiri mu nkhani ya Msamariya wabwino.

MUTU 16

Kodi Chofunika Kwambiri Ndi Chiyani?

Kodi tingakhale bwanji olemera kwa Mulungu?

MUTU 17

Mmene Tingakhalire Osangalala

Mphunzitsi Waluso anatchula chinsinsi cha zimene zimapangitsa munthu kukhala wosangalala.

MUTU 19

Kodi Ndi Bwino Kuchita Ndewu?

Kodi mungatani ngati ndewu itayamba?

MUTU 20

Kodi Nthawi Zonse Umafuna Kukhala Woyamba?

Kodi Yesu anawauza chiyani ophunzira ake atakangana pofuna kudziwa amene anali woyamba?

MUTU 21

Kodi Tiyenera Kudzitama Tikachita Zabwino?

Yesu ananena nkhani ya Mfarisi ndi wokhometsa msonkho.

MUTU 22

Chifukwa Chake Tiyenera Kupewa Bodza

Werengani nkhaniyi kuti mudziwe zimene Yehova anachita ndi Hananiya komanso Safira.

MUTU 23

Chifukwa Chake Anthufe Timadwala

Kodi zidzatheka kuti nthawi ina anthu azingokhala bwinobwino osadwala?

MUTU 24

Usakhale Wakuba

Werengani nkhaniyi yomwe ikufotokoza za anthu 4 omwe anatenga zinthu za eniake.

MUTU 25

Kodi Amene Amachita Zinthu Zoipa Angasinthe?

Tikaona zimene Saulo komanso mzimayi amene anali hule anachita, zimasonyeza kuti anthu oipa akhoza kusintha n’kukhala anthu abwino.

MUTU 26

Chifukwa Chake Kuchita Zinthu Zabwino Kumavuta

Kodi ukuganiza kuti anthu ochita zoipa angamve bwanji ngati utakana kuchita zimene iwowo akufuna?

MUTU 27

Kodi Mulungu Wako Ndani?

Anthu amalambira milungu yambiri. Kodi inuyo mungalambire mulungu uti? Zimene achinyamata atatu achiheberi anachita zingatithandize kudziwa zimene tingachite.

MUTU 28

Kudziwa Amene Uyenera Kumumvera

“Perekani zinthu za Kaisara kwa Kaisara, koma zinthu za Mulungu muzizipereka kwa Mulungu.”

MUTU 29

Kodi Mapwando Onse Amakondweretsa Mulungu?

Kodi mukudziwa kuti Baibulo limanena za mapwando angapo omwe anthu anachita? Tikhoza kudziwa maganizo a Mulungu Tikawerenga nkhani zokhudza mapwandowa.

MUTU 30

Zimene Zingatithandize Kuthetsa Mantha

Mphunzitsi Waluso sananene kuti kutumikira Yehova n’kosavuta, koma kuti pali njira imene ingatithandize kukhala olimba mtima.

MUTU 31

Amene Angatitonthoze

Kodi ungatani ngati wakhumudwa kapena ngati ukuona kuti uli wekhawekha?

MUTU 32

Mmene Yesu Anatetezedwera

Phunzirani mmene Yehova anatetezera Yesu kwa anthu amene ankafuna kumupha ali mwana.

MUTU 33

Yesu Angatiteteze

Yesu ali padziko lapansi anasonyeza kuti anali ndi mphamvu zoteteza anthu amene ankamukonda.

MUTU 34

Kodi Chimachitika ndi Chiyani Tikamwalira?

Kodi muyenera kuopa kufa kapena kuopa anthu omwe anamwalira?

MUTU 35

Tingauke kwa Akufa

Mulungu anapatsa Yesu mphamvu zoukitsa anthu omwe anamwalira kuphatikizaponso ana.

MUTU 36

Kodi Ndani Adzauka kwa Akufa? Nanga Adzakhala Kuti?

Kodi Yesu ananena zotani pa nkhani imeneyi?

MUTU 37

Kukumbukira Yehova ndi Mwana Wake

Yesu anasonyeza otsatira ake njira yapadera yokumbukira zimene Yehova komanso iyeyo anatichitira.

MUTU 38

Chifukwa Chake Tiyenera Kukonda Yesu

Yesu anapereka moyo wake wangwiro kuti tidzapeze moyo wosatha.

MUTU 39

Mulungu Anakumbukira Mwana Wake

Yesu waukitsidwa.

MUTU 40

Kukondweretsa Mulungu

Mwambi wa m’Baibulo umati: ‘Mwananga, khala wanzeru, ukondweretse mtima wanga.’

MUTU 41

Ana Amene Amakondweretsa Mulungu

Kodi ndi zinthu ziti zimene mungapange kuti musangalatse Mulungu?

MUTU 42

Chifukwa Chake Tifunikira Kugwira Ntchito

Ntchito imatithandiza kuti tiziganiza bwino komanso kuti matupi athu akhale amphamvu. Mukhoza kuphunzira kuti muzisangalala pogwira ntchito.

MUTU 43

Kodi Abale Athu ndi Alongo Athu Ndani?

Kodi anthu omwe si a m’banja lanu angakhalenso abale anu?

MUTU 44

Mabwenzi Athu Azikhala Okonda Mulungu

“Musasocheretsedwe. Kugwirizana ndi anthu oipa kumawononga makhalidwe abwino.”

MUTU 45

Kodi Ufumu wa Mulungu Ndi Chiyani? Zimene Tingachite Posonyeza Kuti Tikuufuna

Yesu akadzayamba kulamulira dziko lonse lapansi, adzasintha zinthu zambiri padzikoli.

MUTU 46

Madzi Anawononga Dziko—Kodi Zidzachitikanso?

Anthu olungama adzakhala padzikoli mpaka kalekale.

MUTU 47

Zimene Zikutidziwitsa Kuti Aramagedo Ili Pafupi

Zizindikiro zikuonekera kulikonse

MUTU 48

Ungathe Kukhala M’dziko Latsopano la Mulungu

N’chifukwa chiyani ukufuna kudzala ndi moyo wosatha m’Paradaiso?