Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Moyo wa Kusukulu

Moyo wa Kusukulu

Chigawo 4

Moyo wa Kusukulu

Kodi pali maphunziro ena amene amakuvutani kwambiri?

□ Inde

□ Ayi

Kodi munayamba mwavutitsidwapo kapena kuchitiridwa zachipongwe ndi anzanu a kusukulu?

□ Inde

□ Ayi

Kodi nthawi zina mumatengeka ndi makhalidwe a anzanu a kusukulu?

□ Inde

□ Ayi

Mwina mungaganize kuti: ‘Ngati nditakwanitsa kumaliza sukulu bwinobwino ndiye kuti palibenso china chilichonse chimene chingandivute.’ Zimenezi zikhoza kukhala zoona chifukwa kusukulu n’kumene kumavuta kwambiri kuti munthu asonyeze kuti ndi wanzeru, wosakwiya msanga ndiponso wokonda Mulungu. Kodi mungatani kuti muphunzire bwinobwino popanda kutengera makhalidwe oipa a anzanu a kusukulu? Mitu 13 mpaka 17 ikuthandizani kwambiri pankhani zimenezi.

[Chithunzi chachikulu pamasamba 112, 113]