1 Mbiri 16:1-43

  • Likasa linaikidwa mutenti (1-6)

  • Nyimbo ya Davide yothokoza (7-36)

    • “Yehova wakhala Mfumu!” (31)

  • Utumiki wa kumene kunali Likasa (37-43)

16  Choncho anabweretsa Likasa la Mulungu woona pamalo amene Davide anakonza nʼkuliika mutenti imene iye anamanga kuti lizikhalamo.+ Kenako iwo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zamgwirizano kwa Mulungu woona.+ 2  Davide atamaliza kupereka nsembe zopsereza+ ndi nsembe zamgwirizano,+ anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova. 3  Komanso anapatsa Aisiraeli onse mikate yozungulira, makeke a zipatso za kanjedza ndi makeke a mphesa. Anapereka zimenezi kwa aliyense, mwamuna ndiponso mkazi. 4  Kenako Davide anaika Alevi ena kuti azitumikira kumene Likasa la Yehova+ linkakhala ndiponso kuti azilemekeza,* kuyamika komanso kutamanda Yehova Mulungu wa Isiraeli. 5  Mtsogoleri wawo anali Asafu,+ wachiwiri wake anali Zekariya. Ndipo Yeyeli, Semiramoti, Yehiela, Matitiya, Eliyabu, Benaya, Obedi-edomu ndi Yeyeli+ ankaimba ndi zoimbira za zingwe ndiponso azeze.+ Asafu ankaimba zinganga.+ 6  Benaya ndi Yahazieli, omwe anali ansembe, ankaimba malipenga nthawi zonse patsogolo pa likasa la pangano la Mulungu woona. 7  Pa tsiku limeneli mʼpamene Davide kwa nthawi yoyamba anathandiza nawo kuimba nyimbo yothokoza Yehova kudzera mwa Asafu+ ndi abale ake yakuti: 8  “Yamikani Yehova,+ itanani pa dzina lake,Dziwitsani mitundu ya anthu ntchito zake!+ 9  Muimbireni, muimbireni nyimbo* zomutamanda,+Ganizirani mozama* ntchito zake zonse zodabwitsa.+ 10  Nyadirani dzina lake loyera.+ Mitima ya anthu ofunafuna Yehova isangalale.+ 11  Funafunani Yehova+ ndipo muzidalira mphamvu zake. Nthawi zonse muzimupempha kuti akuthandizeni.*+ 12  Kumbukirani ntchito zodabwitsa zimene wachita,+Kumbukirani zozizwitsa zake ndi ziweruzo zimene wanena, 13  Inu mbadwa* za Isiraeli mtumiki wake,+Inu ana a Yakobo, osankhidwa ake.+ 14  Iye ndi Yehova Mulungu wathu.+ Ziweruzo zake zili padziko lonse lapansi.+ 15  Kumbukirani pangano lake mpaka kalekale,Lonjezo limene anapereka ku mibadwo 1,000,+ 16  Kumbukirani pangano limene anapangana ndi Abulahamu,+Komanso lumbiro limene analumbira kwa Isaki.+ 17  Pangano limene analikhazikitsa monga lamulo kwa Yakobo,+Komanso monga pangano lokhalapo mpaka kalekale kwa Isiraeli, 18  Pamene anati: ‘Ndidzakupatsa dziko la Kanani,+Kuti likhale cholowa chako.’+ 19  Pamene ankanena zimenezi nʼkuti inu mulipo ochepa,Nʼkuti mulipo ochepa kwambiri komanso muli alendo mʼdzikolo.+ 20  Iwo ankayendayenda kuchokera ku mtundu wina kupita ku mtundu wina,Komanso kuchokera mu ufumu wina kupita kwa anthu a mtundu wina.+ 21  Mulungu sanalole kuti munthu aliyense awapondereze,+Koma anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo.+ 22  Iye anati: ‘Musakhudze odzozedwa anga,Ndipo aneneri anga musawachitire choipa chilichonse.’+ 23  Dziko lonse lapansi liimbire Yehova! Tsiku ndi tsiku muzilengeza za chipulumutso chake!+ 24  Lengezani ulemerero wake pakati pa anthu a mitundu ina,Lengezani ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu. 25  Chifukwa Yehova ndi wamkulu komanso woyenera kutamandidwa, Iye ndi wochititsa mantha kwambiri kuposa milungu ina yonse.+ 26  Milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi milungu yopanda pake.+Koma Yehova ndi amene anapanga kumwamba.+ 27  Pamene amakhala pali ulemu ndi ulemerero,+Pokhala pake pali mphamvu ndi chimwemwe.+ 28  Mʼpatseni Yehova zimene akuyenera kulandira, inu mabanja a mitundu ya anthu,Mʼpatseni Yehova zimene akuyenera kulandira chifukwa cha ulemerero ndi mphamvu zake.+ 29  Mʼpatseni Yehova ulemerero woyenera dzina lake,+Bweretsani mphatso pamaso pake.+ Weramirani* Yehova mutavala zovala zokongola ndi zopatulika.+ 30  Dziko lonse lapansi linjenjemere pamaso pake! Dziko lapansi lakhazikika moti silingasunthidwe.*+ 31  Kumwamba kukondwere ndipo dziko lapansi lisangalale,+Lengezani kwa anthu a mitundu ina kuti: ‘Yehova wakhala Mfumu!’+ 32  Nyanja ichite mkokomo ndi zonse zimene zili mmenemo,Mtunda, ndi zonse zili mmenemo, zikondwere. 33  Pa nthawi imodzimodziyo mitengo yamʼnkhalango ifuule mosangalala pamaso pa Yehova,Chifukwa iye akubwera* kudzaweruza dziko lapansi. 34  Yamikani Yehova chifukwa iye ndi wabwino,+Chikondi chake chokhulupirika chidzakhalapo mpaka kalekale.+ 35  Nenani kuti: ‘Tipulumutseni, inu Mulungu wachipulumutso chathu,+Tisonkhanitseni ndi kutipulumutsa kwa anthu a mitundu ina,Kuti titamande dzina lanu loyera,+Ndiponso kuti tikutamandeni mosangalala.+ 36  Atamandidwe Yehova Mulungu wa Isiraeli,Atamandidwe mpaka kalekale.’” Ndiyeno anthu onse ananena kuti, “Ame!”* ndipo anatamanda Yehova. 37  Kenako Davide anasiya Asafu+ ndi abale ake kumeneko pamaso pa likasa la pangano la Yehova, kuti azitumikira nthawi zonse kumene Likasalo linkakhala,+ mogwirizana ndi zofunika kuchita pa tsikulo.+ 38  Anasiyanso Obedi-edomu ndi abale ake okwana 68. Ndipo Obedi-edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa anali alonda apageti. 39  Zadoki+ wansembe ndi ansembe anzake anawasiya kuchihema cha Yehova chimene chinali pamalo okwezeka a ku Gibiyoni,+ 40  Anawasiya kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova nthawi zonse paguwa lansembe zopsereza, mʼmawa ndi madzulo, mogwirizana ndi zonse zolembedwa mʼChilamulo cha Yehova chimene analamula Aisiraeli.+ 41  Iwowa anali limodzi ndi Hemani ndi Yedutuni+ ndiponso amuna onse amene anawasankha mochita kuwatchula mayina kuti azithokoza Yehova,+ chifukwa “chikondi chake chokhulupirika chidzakhalapo mpaka kalekale.”+ 42  Hemani+ ndi Yedutuni anawasiya kuti aziimba malipenga, zinganga ndi zipangizo zina zimene ankagwiritsa ntchito potamanda Mulungu woona* ndipo ana a Yedutuni+ anali alonda apageti. 43  Kenako anthu onse anapita kunyumba kwawo. Nayenso Davide anapita kunyumba kwake kukadalitsa banja lake.

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “azikumbukira.”
Kapena kuti, “mupekereni nyimbo.”
Mabaibulo ena amati, “Nenani zokhudza.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “muzifunafuna nkhope yake.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mbewu.”
Kapena kuti, “Lambirani.”
Kapena kuti, “silingagwedezeke.”
Kapena kuti, “wabwera.”
Kapena kuti, “Zikhale momwemo!”
Kapena kuti, “zipangizo zina zoimbira nyimbo ya Mulungu woona.”