Yesaya 64:1-12

64  Zikanakhalatu bwino mukanang’amba kumwamba, mukanatsika pansi pano,+ komanso mapiri akanagwedezeka chifukwa cha inu,+  ngati momwe zimakhalira moto ukayatsa tchire la zitsamba ndiponso ukawiritsa madzi. Zikanakhala bwino mukanachita zimenezi kuti dzina lanu lidziwike kwa adani anu,+ ndiponso kuti mitundu ya anthu igwedezeke chifukwa cha inu.+  Inu munatsikira pansi pano pamene munachita zinthu zochititsa mantha+ zimene sitinali kuyembekezera. Mapiri anagwedezeka chifukwa cha inu.+  Kuyambira kalekale palibe amene anamvapo+ kapena kuganizira za Mulungu wina kupatula inu,+ ndipo palibe amene anamuonapo. Inu mumathandiza munthu amene akukuyembekezerani.+  Mwabwera kudzathandiza anthu amene akukondwera ndiponso amene akuchita zolungama,+ anthu amene amakukumbukirani potsatira njira zanu.+ Koma inuyo munakwiya+ chifukwa chakuti ifeyo tinkangopitirizabe kuchimwa+ kwanthawi yaitali. Choncho kodi ndife oyenera kupulumutsidwa?+  Tonsefe takhala ngati munthu wodetsedwa, ndipo zochita zathu zonse zolungama zili ngati kansalu kamene mkazi amavala pa nthawi yosamba.+ Tonsefe tidzayoyoka ngati masamba+ ndipo zolakwa zathu zidzatiuluzira kutali ngati mphepo.+  Palibe amene akutamanda dzina lanu.+ Palibe amene akutekeseka kuti akufunefuneni ndi kukugwirani mwamphamvu, pakuti mwatibisira nkhope yanu+ ndipo mwatichititsa kuti tisungunuke+ ndi mphamvu ya zolakwa zathu.  Komatu inu Yehova, inu ndinu Atate wathu.+ Ife ndife dongo+ ndipo inu ndinu Wotiumba.+ Tonsefe ndife ntchito ya manja anu.+  Inu Yehova musatikwiyire kwambiri,+ ndipo musakumbukire zolakwa zathu kwamuyaya.+ Chonde, kumbukirani kuti tonsefe ndife anthu anu.+ 10  Mizinda yanu yoyera+ yasanduka chipululu. Ziyoni+ wangosanduka chipululu basi, ndipo Yerusalemu wasanduka bwinja.+ 11  Nyumba yathu yoyera ndiponso yokongola+ imene makolo athu anali kukutamandiranimo,+ yasanduka chinthu chofunika kuchitentha pamoto,+ ndipo zinthu zathu zonse zabwinozabwino+ zasakazidwa. 12  Poona zinthu zonsezi, kodi mupitiriza kumangokhala osachitapo kanthu,+ inu Yehova? Kodi muzingoonerera pamene ife tikusautsidwa koopsa?+

Mawu a M'munsi