Yesaya 38:1-22

38  M’masiku amenewo, Hezekiya anadwala mpaka kutsala pang’ono kufa.+ Choncho mneneri Yesaya+ mwana wa Amozi anabwera kwa iye n’kumuuza kuti: “Yehova wanena kuti, ‘Uza banja lako zochita,+ chifukwa iweyo ufa ndithu. Sukhala ndi moyo.’”+  Atamva mawu amenewa, Hezekiya anatembenukira kukhoma+ n’kuyamba kupemphera kwa Yehova.+  Iye anapemphera kuti: “Ndikukupemphani inu Yehova, chonde kumbukirani+ kuti ndinayenda+ pamaso panu mokhulupirika+ ndiponso ndi mtima wathunthu,+ komanso ndinachita zabwino pamaso panu.” Kenako Hezekiya anayamba kulira kwambiri.+  Tsopano Yehova analankhula+ ndi Yesaya kuti:  “Pita, kauze Hezekiya kuti, ‘Yehova Mulungu wa Davide kholo lako+ wanena kuti: “Ndamva pemphero lako,+ ndipo ndaona misozi yako.+ Tsopano ndiwonjezera zaka 15 pa masiku ako.+  Ndidzalanditsa iweyo ndi mzindawu m’manja mwa mfumu ya Asuri, ndipo ndidzateteza mzinda uno.+  Chizindikiro chochokera kwa Yehova, chakuti Yehova adzakwaniritsadi mawu amene walankhula, ndi ichi:+  Ndichititsa mthunzi wa dzuwa+ umene wapita kale kutsogolo pamasitepe a Ahazi, kuti ubwerere m’mbuyo masitepe 10.”’”+ Choncho dzuwa linabwerera m’mbuyo pang’onopang’ono masitepe 10 pa masitepe pomwe linali litapita kale kutsogolo.+  Hezekiya mfumu ya Yuda atadwala+ n’kuchira, analemba zotsatirazi.+ 10  Ine ndinati: “Pakatikati pa masiku anga ndidzalowa pazipata+ za Manda.Ndidzamanidwa zaka zanga zotsala.”+ 11  Ndanena kuti: “Sindidzamuona Ya.* Ndithu Ya sindidzam’penya m’dziko la amoyo.+Anthu sindidzawaonanso. Ndidzakhala ndi anthu okhala kudziko limene kulibe moyo. 12  Malo anga okhala ali ngati hema wa abusa. Mitengo yake yazulidwa ndipo hemayo wachotsedwapo.+Ndakulunga moyo wanga ngati munthu wowomba nsalu.Winawake wandidula+ ngati mmene amadulira nsalu kuchowombera nsalu akamaliza kuiwomba.Kuyambira m’mawa mpaka usiku mumandipereka ku zowawa.+ 13  Ndadzitonthoza mpaka m’mawa.+Mafupa anga onse, iye akungokhalira kuwaphwanya ngati mkango.+Kuyambira m’mawa mpaka usiku mukungokhalira kundipereka ku zowawa.+ 14  Ndikungokhalira kulira ngati namzeze* kapena pumbwa.*+Ndikungokhalira kubuula ngati njiwa.+ Maso anga akupenyetsetsa kumwamba motopa. Choncho ndinati:+‘Inu Yehova ine ndapanikizika. Chonde ndithandizeni.’+ 15  Kodi ndinene kuti chiyani? Kodi iyeyo andiuza kuti chiyani?+Iyeyonso wachitapo kanthu.+Zaka zanga zonse, ndikungokhalira kuyenda ndili khuma chifukwa cha chisoni cha mtima wanga.+ 16  ‘Ndi mawu anu, anthu amakhalabe ndi moyo inu Yehova, ndipo mofanana ndi wina aliyense, mzimu wanga umapeza moyo kudzera mu zochita zanu.+Inu mudzandibwezera thanzi langa n’kundisiya ndi moyo.+ 17  M’malo mopeza mtendere ndinapeza zowawa, zowawatu zedi!+Inuyo mwamamatira moyo wanga ndipo mwauteteza kuti usapite kudzenje la chiwonongeko.+Pakuti machimo anga onse mwawaponyera kumbuyo kwanu.+ 18  Pakuti Manda sangakutamandeni.+ Imfa singakulemekezeni.+Anthu amene akutsikira kudzenje sangayembekezere kukhulupirika kwanu.+ 19  Munthu wamoyo, amene akupuma, ndi amene angakutamandeni,+Ngati mmene ineyo ndikuchitira lero.+Bambo akhoza kuphunzitsa+ ana ake za kukhulupirika kwanu. 20  Inu Yehova bwerani mudzandipulumutse,+ ndipo tidzaimba nyimbo zimene ine ndinapeka. Ndidzaimba ndi zoimbira za zingwe+Kunyumba ya Yehova masiku onse a moyo wathu.’”+ 21  Kenako Yesaya anati: “Anthu atenge nkhuyu zouma zoumba pamodzi ndipo azikhukhutize pachithupsa+ chimene ali nacho kuti achire.”+ 22  Pa nthawiyi, Hezekiya anati: “Kodi chizindikiro chakuti ndidzapita kunyumba ya Yehova n’chiyani?”+

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa Eks 15:2.
Mbalame imeneyi ena amati “kaluweluwe” kapena “kamembe.”
Mbalame imeneyi ena amati “nyapwere.”