Yesaya 25:1-12
25 Inu Yehova, ndinu Mulungu wanga.+ Ndikukukwezani+ ndi kutamanda dzina lanu+ chifukwa mwachita zinthu zabwino kwambiri.+ Mwakwaniritsa zolinga zanu+ zakalekale ndipo mwachita zinthu mokhulupirika+ ndi modalirika.+
2 Mwasandutsa mzinda kukhala mulu wamiyala ndipo mudzi wokhala ndi mpanda wolimba kwambiri mwausandutsa bwinja logumukagumuka. Mzinda wa chitetezo champhamvu wa anthu achilendo mwauthetsa ndipo sudzamangidwanso mpaka kalekale.+
3 N’chifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani. Mudzi wa mitundu yankhanza udzakuopani.+
4 Pakuti inu mwakhala malo achitetezo kwa munthu wonyozeka ndiponso malo achitetezo kwa munthu wosauka m’masautso ake.+ Mwakhala malo ousapo mvula yamkuntho ndi mthunzi+ wobisalirapo kutentha kwa dzuwa. Mwakhala wotero pamene anthu ankhanza akuwomba anzawo ngati mvula yamkuntho yowomba khoma.
5 Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsera kutentha m’dziko lopanda madzi, inu mumachepetsa phokoso la alendo.+ Nayonso nyimbo ya anthu ankhanza yaletsedwa.+
6 Yehova wa makamu adzakonzera anthu a mitundu yonse+ m’phiri ili,+ phwando la zakudya zabwinozabwino,+ phwando la vinyo wokoma kwambiri,* phwando la zakudya zabwinozabwino zokhala ndi mafuta a m’mafupa,+ ndiponso la vinyo+ wokoma kwambiri, wosefedwa bwino.+
7 M’phiri limeneli iye adzameza chophimba chimene chikuphimba anthu onse,+ ndi nsalu imene yakuta mitundu yonse.
8 Iye adzameza imfa kwamuyaya+ ndipo Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, adzapukuta misozi pankhope zonse za anthu.+ Adzachotsa kunyozeka kwa anthu ake padziko lonse lapansi,+ pakuti Yehova ndiye wanena zimenezi.
9 M’tsiku limenelo munthu adzati: “Taonani! Uyu ndiye Mulungu wathu.+ Chiyembekezo chathu chinali mwa iye+ ndipo iye watipulumutsa.+ Uyu ndi Yehova.+ Chiyembekezo chathu chinali mwa iye. Tiyeni tisangalale ndi kukondwera ndi chipulumutso chochokera kwa iye.”+
10 Pakuti dzanja la Yehova lidzakhazikika paphiri limeneli,+ ndipo Mowabu adzapondedwapondedwa+ pamalo pake ngati mulu wa udzu umene umapondedwapondedwa pamalo opangira manyowa.+
11 Iye adzatambasula manja ake n’kuwamenyetsa pakati pa mzindawo ngati mmene munthu wosambira amatambasulira manja ake n’kuwamenyetsa pamadzi akamasambira. Adzathetsa kunyada+ kwa mzindawo poumenya mwaluso ndi manja ake.
12 Iye adzagwetsa mzinda wokhala ndi mipanda yachitetezo italiitali yolimba kwambiri. Adzautsitsa n’kuugwetsera pansi, pafumbi.+
Mawu a M'munsi
^ Kapena, “vinyo yemwe nsenga zake zadikha pansi chifukwa chokhalitsa.”