Yesaya 11:1-16

11  Nthambi+ idzatuluka pachitsa cha Jese,+ ndipo mphukira+ yotuluka pamizu yake idzakhala yobereka zipatso.+  Mzimu wa Yehova udzakhazikika pa iye,+ mzimu wanzeru,+ womvetsa zinthu,+ wolangiza, wamphamvu,+ wodziwa zinthu+ ndi woopa Yehova.+  Iye adzasangalala ndi kuopa Yehova.+ Sadzaweruza potengera zimene wangoona ndi maso ake, kapena kudzudzula potengera zimene wangomva ndi makutu ake.+  Adzaweruza mwachilungamo anthu onyozeka+ ndipo adzadzudzula anthu mowongoka mtima, pothandiza ofatsa a padziko lapansi. Adzakwapula dziko lapansi ndi ndodo ya pakamwa pake,+ ndipo adzagwiritsa ntchito mzimu wa pakamwa pake kupha munthu woipa.+  Chilungamo ndi kukhulupirika zidzakhala lamba wa m’chiuno mwake.+  Mmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wa nkhosa wamphongo kwa kanthawi,+ ndipo kambuku* adzagona pansi ndi mwana wa mbuzi. Mwana wa ng’ombe, mkango wamphamvu+ ndi nyama yodyetsedwa bwino zidzakhala pamodzi,+ ndipo kamnyamata kakang’ono kadzakhala mtsogoleri wawo.  Ng’ombe ndi chimbalangondo zidzadyera pamodzi. Ana awo adzagona pansi pamodzi. Ngakhale mkango udzadya udzu ngati ng’ombe yamphongo.+  Mwana woyamwa adzasewera pa una wa mamba,+ ndipo mwana woleka kuyamwa adzapisa dzanja lake kudzenje la njoka yapoizoni.  Sizidzavulazana+ kapena kuwonongana m’phiri langa lonse loyera,+ chifukwa dziko lapansi lidzadzaza ndi anthu odziwa Yehova ngati mmene madzi amadzazira nyanja.+ 10  M’tsiku limenelo,+ padzakhala muzu wa Jese+ womwe udzaimirire ngati chizindikiro kwa anthu.+ Ngakhale anthu a mitundu ina adzatembenukira kwa iye kuti awatsogolere,+ ndipo malo ake okhalapo adzakhala aulemerero.+ 11  M’tsiku limenelo, Yehova adzaperekanso dzanja lake kachiwiri+ kuti atenge anthu ake otsala kuchokera ku Asuri,+ ku Iguputo,+ ku Patirosi,+ ku Kusi,+ ku Elamu,+ ku Sinara,+ ku Hamati ndi m’zilumba za m’nyanja.+ 12  Iye adzakwezera chizindikiro mitundu ya anthu n’kusonkhanitsa Aisiraeli omwe anamwazikana.+ Ndipo adzasonkhanitsa pamodzi Ayuda omwe anabalalika, kuchokera kumalekezero anayi a dziko lapansi.+ 13  Nsanje ya Efuraimu idzatha,+ ndipo ngakhale anthu odana ndi Yuda adzaphedwa. Efuraimu sadzachitira nsanje Yuda ndiponso Yuda sadzadana ndi Efuraimu.+ 14  Iwo adzauluka paphewa la Afilisiti kumadzulo,+ ndipo onsewa pamodzi, adzalanda katundu wa ana aamuna a Kum’mawa.+ Adzatambasulira dzanja lawo pa Edomu ndi Mowabu,+ ndipo ana a Amoni adzawagonjera.+ 15  Yehova adzaphwetsa chigawo cha nyanja ya Iguputo,+ ndipo adzayendetsa dzanja lake moopseza Mtsinje*+ pogwiritsa ntchito mpweya wake wotentha. Adzamenya mtsinjewo pokwapula timitsinje take 7, ndipo adzachititsa anthu kuwolokapo nsapato zili kuphazi.+ 16  Padzakhala msewu waukulu+ wochokera kudziko la Asuri woti mudzadutse anthu ake amene adzatsale,+ monga mmene panalili msewu umodzi umene Aisiraeli anayendamo m’tsiku limene anatuluka m’dziko la Iguputo.

Mawu a M'munsi

Ena amati “nyalugwe.”
Umenewu ndi mtsinje wa Firate.