Yeremiya 8:1-22

8  “Pa nthawi imeneyo,” watero Yehova, “anthu adzatulutsa m’manda mafupa a mafumu a Yuda, a akalonga awo, a ansembe, a aneneri ndi a anthu amene anali mu Yerusalemu.+  Mafupawo adzawamwaza poyera ndipo dzuwa, mwezi, ndi makamu onse akumwamba zidzawala pa iwo. Zinthu zimenezi ndi zimene iwo anali kuzikonda, kuzitumikira, kuzitsatira,+ kuzipembedza, ndi kuziweramira.+ Mafupawo sadzasonkhanitsidwa pamodzi kapena kuikidwa m’manda. Iwo adzakhala ngati manyowa panthaka.”+  “Onse otsala a banja loipali, kulikonse kumene ndidzawabalalitsira,+ adzaona kuti ndi bwino kufa kusiyana ndi kukhala moyo,”+ watero Yehova wa makamu.  “Ukawauze kuti, ‘Yehova wanena kuti: “Kodi iwo adzagwa osadzukanso?+ Kodi mmodzi akabwerera, winanso sangabwerere?+  N’chifukwa chiyani anthu a mu Yerusalemu ali osakhulupirika ndipo akhalabe osakhulupirika kwa nthawi yaitali chonchi? Iwo akupitiriza kuchita zachinyengo+ ndipo akana kubwerera.+  Ine ndinali tcheru+ ndipo ndinali kuwamvetsera.+ Zimene iwo anali kunena sizinali zoona. Panalibe munthu wolapa zoipa zimene anachita,+ amene ananena kuti, ‘Kodi ndachitiranji zimenezi?’ Aliyense akubwerera kunjira imene anthu ambiri akuitsatira,+ ngati hatchi imene ikuthamangira kunkhondo.  Ngakhale dokowe, mbalame youluka m’mlengalenga, imadziwa bwino nthawi yake yoikidwiratu.+ Ndipo njiwa,+ namzeze* ndi pumbwa,* iliyonse mwa mbalame zimenezi imadziwa nyengo yobwerera kumene yachokera. Koma anthu anga sakudziwa chiweruzo cha Yehova.”’+  “‘Anthu inu munganene bwanji kuti: “Ndife anzeru, ndipo tili ndi chilamulo cha Yehova”?+ Ndithudi, zolembera zachinyengo+ za alembi zagwiritsidwa ntchito mwachinyengo.  Anthu anzeru achita manyazi.+ Achita mantha ndipo adzagwidwa. Taonani! Iwo akana mawu a Yehova. Kodi ali ndi nzeru yotani tsopano?+ 10  Choncho akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena, ndipo minda yawo ndidzaipereka kwa anthu ena.+ Pakuti kuyambira wamng’ono mpaka wamkulu aliyense wa iwo akupeza phindu lachinyengo.+ Kuyambira mneneri mpaka wansembe, aliyense wa iwo akuchita zachinyengo.+ 11  Iwo akuyesa kuchiritsa mwachinyengo+ kuwonongeka kwa mwana wamkazi wa anthu anga ponena kuti: “Kuli mtendere! Kuli mtendere!” pamene kulibe mtendere.+ 12  Kodi iwo anachita manyazi chifukwa anachita zinthu zonyansa?+ Iwo sanachite manyazi ngakhale pang’ono, komanso sanali kudziwa n’komwe kuchita manyazi.+ “‘Choncho iwo adzagwa pamodzi ndi anthu amene akugwa. Pa nthawi yowalanga+ adzapunthwa,’ watero Yehova.+ 13  “‘Pokolola ndidzawafafaniza,’ watero Yehova.+ ‘Mumtengo wa mpesa simudzapezeka mphesa,+ mumtengo wa mkuyu simudzapezeka nkhuyu, ndipo masamba adzafota. Zinthu zimene ndimawapatsa zidzawadutsa.’” 14  “N’chifukwa chiyani tikungokhala? Sonkhanani pamodzi, ndipo tiyeni tilowe m’mizinda yokhala ndi mipanda yolimba kwambiri+ kuti tikafere kumeneko. Pakuti Yehova Mulungu wathu watiweruza kuti tife,+ ndipo akutipatsa madzi apoizoni kuti timwe+ chifukwa tachimwira Yehova. 15  Tinali kuyembekezera mtendere, koma panalibe chabwino chilichonse.+ Tinali kuyembekezera kuchiritsidwa, koma m’malomwake tinali kuona zinthu zochititsa mantha.+ 16  Mahatchi ake akumveka kupuma mwawefuwefu ali ku Dani.+ Dziko lonse layamba kugwedezeka chifukwa cha phokoso la kulira kwa mahatchi ake amphongo.+ Adani akubwera kudzawononga dziko ndi zonse zokhala mmenemo, mzinda ndi onse okhala mmenemo.” 17  “Inetu ndikutumiza njoka pakati panu, njoka zapoizoni,+ zimene simungaziimbire nyimbo kuti muziseweretse,+ ndipo zidzakulumani ndithu,” watero Yehova. 18  Ndagwidwa ndi chisoni chosatha.+ Mtima wanga wadwala. 19  Pakumveka mawu olirira thandizo a mwana wamkazi wa anthu anga ali kudziko lakutali.+ Iye akuti: “Kodi Yehova sali mu Ziyoni?+ Kapena kodi mfumu ya Yerusalemu mulibe mmenemo?”+ “N’chifukwa chiyani andikhumudwitsa ndi mafano awo ogoba, ndiponso milungu yawo yachilendo yopanda pake?”+ 20  “Nthawi yokolola yadutsa, ndipo nyengo ya chilimwe yatha. Koma ife sitinapulumutsidwe!”+ 21  Ndasweka mtima+ chifukwa cha kuwonongeka+ kwa mwana wamkazi wa anthu anga. Ndine wachisoni. Ndadabwa kwambiri.+ 22  Kodi mu Giliyadi+ mulibe mafuta a basamu? Kapena kodi mulibe wochiritsa mmenemo?+ N’chifukwa chiyani nanga mwana wamkazi wa anthu anga sakuchira?+

Mawu a M'munsi

Mbalame imeneyi ena amati “nyapwere.”
Mbalame imeneyi ena amati “kaluweluwe” kapena “kamembe.”