Yeremiya 7:1-34

7  Mawu amene Yehova anauza Yeremiya ndi awa:  “Imirira pachipata cha nyumba ya Yehova, ndi kulengeza kuti,+ ‘Tamverani mawu a Yehova nonsenu okhala mu Yuda, amene mumalowa pazipata izi kuti mukagwadire Yehova.  Yehova wa makamu, Mulungu wa Isiraeli wanena kuti: “Konzani njira zanu ndiponso zochita zanu kuti zikhale zabwino, ndipo ndidzachititsa anthu inu kukhalabe m’dziko lino.+  Musamakhulupirire mawu achinyengo+ ndi kunena kuti, ‘Nyumba izi ndizo kachisi wa Yehova, inde ndi kachisi wa Yehova, ndithudi ndi kachisi wa Yehova!’  Ngati mungakonze njira zanu ndi zochita zanu kuti zikhale zabwino, mukamaweruza molungama pakati pa munthu ndi mnzake,+  ngati simudzapondereza mlendo wokhala pakati panu, mwana wamasiye* ndi mkazi wamasiye,+ komanso ngati simudzakhetsa magazi a munthu wopanda mlandu m’dziko lino,+ ndiponso ngati simudzatsatira milungu ina, zimene zingakubweretsereni tsoka,+  inenso ndidzachititsa kuti mukhalebe m’dziko lino, dziko limene ndinapatsa makolo anu, ndipo mudzakhalamo mpaka kalekale.”’”+  “Inu mukukhulupirira mawu achinyengo, koma simudzapezapo phindu lililonse.+  Kodi mungamabe,+ kupha,+ kuchita chigololo,+ kulumbira monama,+ kufukiza nsembe zautsi kwa Baala+ ndi kutsatira milungu ina imene simunali kuidziwa,+ 10  kenako n’kubwera kudzaima pamaso panga m’nyumba iyi, imene yatchedwa ndi dzina langa+ n’kumanena kuti, ‘Ndithudi tidzapulumutsidwa,’ ngakhale mukuchita zinthu zonyansa zonsezi? 11  Kodi nyumba iyi, imene yatchedwa ndi dzina langa,+ mwayamba kuiona ngati phanga la achifwamba?+ Inetu ndaona zimene mukuchita,” watero Yehova.+ 12  “‘Pitani ku Silo,+ kumalo kumene poyamba kunali dzina langa,+ ndipo mukaone zimene ndinachitira malowo chifukwa cha kuipa kwa anthu anga Aisiraeli.+ 13  Tsopano chifukwa chakuti mwapitiriza kuchita ntchito zimenezi,’ watero Yehova, ‘ndipo ndinali kukulankhulani nthawi zonse, kudzuka m’mamawa ndi kukulankhulani,+ koma inu osamva,+ kukuitanani koma inu osandiyankha,+ 14  ndidzachita zofanana ndi zimene ndinachita ku Silo.+ Ndidzachita zimenezi panyumba imene ikutchedwa ndi dzina langa,+ imene inu mukuidalira,+ ndiponso malo amene ndinapatsa inu ndi makolo anu. 15  Ine ndidzakuthamangitsani, kukuchotsani pamaso panga,+ ngati mmene ndinathamangitsira abale anu onse, mbadwa zonse za Efuraimu.’+ 16  “Tsopano iwe usawapempherere anthu awa, kapena kuwalirira kwa ine mochonderera. Usawaperekere pemphero, kapena kuwapemphera mochonderera,+ chifukwa ine sindidzakumvetsera.+ 17  Kodi sukuona zimene akuchita m’mizinda ya Yuda ndi m’misewu ya Yerusalemu?+ 18  Ana aamuna akutola nkhuni, abambo akuyatsa moto ndipo akazi akukanda ufa kuti apange makeke okapereka nsembe kwa ‘mfumukazi yakumwamba.’+ Ndipo akuthira pansi nsembe zachakumwa+ kwa milungu ina kuti andikhumudwitse.+ 19  ‘Kodi iwo akukhumudwitsa ine?’ watero Yehova.+ ‘Kodi iwo sakudzikhumudwitsa okha kuti achite manyazi pankhope zawo?’+ 20  Choncho Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti, ‘Taonani! Mkwiyo wanga ndi ukali wanga zikutsanulidwa pamalo awa,+ pamunthu, pachiweto, pamtengo wakuthengo,+ ndi pachipatso chilichonse chochokera m’nthaka yawo, ndipo udzayaka moti sudzazimitsidwa.’+ 21  “Yehova wa makamu, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti, ‘Wonjezerani nsembe zanu zopsereza zathunthuzo pansembe zanu zinazo ndipo muzidye nokha.+ 22  Chifukwatu makolo anu, pamene ndinali kuwatulutsa m’dziko la Iguputo, sindinawauze kapena kuwalamula kuti azipereka nsembe zopsereza zathunthu ndi nsembe zina.+ 23  Koma ndinawalamula kuti: “Muzimvera mawu anga,+ ndipo ndidzakhala Mulungu wanu,+ inuyo mudzakhala anthu anga. Muziyenda m’njira+ imene ndidzakulamulani, kuti zinthu zikuyendereni bwino.”’+ 24  Koma iwo sanamvere kapena kutchera khutu,+ ndipo anapitiriza kuyenda mwa zofuna zawo, mwa kuuma kwa mtima wawo woipawo,+ mwakuti anali kuyenda mobwerera m’mbuyo osati mopita patsogolo,+ 25  kuchokera tsiku limene makolo anu anatuluka m’dziko la Iguputo kufikira lero.+ Ndinapitiriza kukutumizirani atumiki anga onse aneneri, tsiku ndi tsiku ndinali kudzuka m’mawa kwambiri ndi kuwatumiza.+ 26  Koma iwo sanandimvere kapena kutchera khutu lawo.+ M’malomwake anapitiriza kuumitsa khosi lawo,+ ndipo anachita zinthu zoipa kuposa makolo awo.+ 27  “Ukawauze mawu onsewa,+ ngakhale kuti sadzakumvera. Ukawaitane ngakhale kuti sadzakuyankha.+ 28  Ukawauze kuti, ‘Uwu ndiwo mtundu umene anthu ake sanamvere mawu a Yehova Mulungu wawo,+ ndipo sanamvere chilango.*+ Palibe munthu wokhulupirika pakati pawo, ndipo satchulanso n’komwe za kukhulupirika.’+ 29  “Meta tsitsi lako lalitalilo ndi kulitaya.+ Ukwere pamapiri opanda mitengo ndi kuimba nyimbo yoimba polira pamenepo,+ pakuti Yehova wakana+ ndi kusiya mbadwo wa anthu amene wawakwiyira.+ 30  ‘Pakuti ana a Yuda achita zinthu zoipa m’maso mwanga,’ watero Yehova. ‘Aika zinthu zawo zonyansa m’nyumba yotchedwa ndi dzina langa kuti aiipitse.+ 31  Iwo amanga malo okwezeka ku Tofeti,+ m’chigwa cha mwana wa Hinomu,+ kuti azitentha ana awo aamuna ndi ana awo aakazi pamoto,+ chinthu chimene sindinawalamule kuchita ndiponso chimene sindinachiganizirepo mumtima mwanga.’+ 32  “‘Chotero taonani! Masiku akubwera,’ watero Yehova, ‘pamene sadzatchulanso malowo kuti Tofeti ndiponso chigwa cha mwana wa Hinomu, koma adzawatchula kuti chigwa chopherako anthu.+ Iwo adzaika anthu m’manda ku Tofeti mpaka sikudzakhala malo okwanira.+ 33  Mitembo ya anthu awa idzakhala chakudya cha zolengedwa zouluka zam’mlengalenga ndi cha zilombo zakutchire, ndipo sipadzakhala woziopsa.+ 34  Pamenepo ndidzathetsa phokoso lachikondwerero, phokoso lachisangalalo, mawu a mkwati ndi mawu a mkwatibwi+ m’mizinda ya Yuda ndi m’misewu ya Yerusalemu pakuti dzikoli lidzakhala litawonongedwa.’”+

Mawu a M'munsi

Mawu ake enieni, “mwana wamwamuna wopanda bambo.”
Onani mawu a m’munsi pa Miy 1:2.