Yeremiya 6:1-30

6  Bisalani, inu ana a Benjamini, thawani pakati pa Yerusalemu. Ku Tekowa+ imbani lipenga la nyanga ya nkhosa.+ Ku Beti-hakeremu+ kwezani moto wa chizindikiro, chifukwa chiwonongeko chachikulu, tsoka, lasuzumira kuchokera kumpoto.+  Ndithudi mwana wamkazi wa Ziyoni wafanana ndi mkazi wachisasati* wooneka bwino.+  Abusa ndi magulu awo a ziweto anali kubwera kwa iye. Anamanga mahema awo momuzungulira kuti amuukire.+ Aliyense wa iwo anali kudyetsa ziweto zake pamalo ake.+  Anakonzekera kumuthira nkhondo ndipo anati:+ “Nyamukani, tiyeni tipite dzuwa lili paliwombo!”+ “Tsoka ife chifukwa nthawi yatithera ndipo zithunzithunzi zikupitiriza kutalika!”  “Nyamukani, ndipo tiyeni tipite usiku kuti tikawononge nsanja zake zokhalamo anthu.”+  Pakuti Yehova wa makamu wanena kuti: “Dulani mitengo+ kuti tipangire Yerusalemu chiunda chomenyerapo nkhondo.*+ Yerusalemu ndi mzinda woyenera kuimbidwa mlandu.+ Mkati mwake muli kuponderezana kokhakokha.+  Monga mmene chitsime chimasungira madzi ake ali ozizira, Yerusalemu wasunga zoipa zake ngati zinthu zabwino. Mkati mwake mumamveka zachiwawa ndi kufunkha.+ Nthawi zonse ndimaona matenda ndi miliri mumzindawo.  Iwe Yerusalemu, mvera chilango+ kuti ndisatembenuke ndi kukufulatira chifukwa chonyansidwa nawe,+ kuti ndisakusandutse bwinja, dziko lopanda munthu aliyense wokhalamo.”+  Yehova wa makamu wanena kuti: “Mosalephera adani adzakunkha otsalira a Isiraeli ngati mmene amakunkhira mphesa.+ Kweza dzanja lako ngati munthu amene akuthyola mphesa panthambi za mtengo wa mpesa.” 10  “Kodi ndilankhule ndi ndani ndipo ndichenjeze ndani kuti amve? Taonani! Makutu awo sanawachite mdulidwe, moti sangamve.+ Taonani! Mawu a Yehova akhala onyozeka kwa iwo,+ ndipo sakukondwera nawo.+ 11  Ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova. Ndatopa ndi kukhala chete.”+ “Tsanulira mkwiyowo pa mwana amene ali mumsewu+ ndipo nthawi yomweyo uutsanulirenso pa kagulu ka anyamata okondana. Mwamuna pamodzi ndi mkazi wake, munthu wachikulire pamodzi ndi munthu wokalamba, onsewo adzagwidwa.+ 12  Nyumba zawo, minda yawo ndi akazi awo, zonse pamodzi zidzaperekedwa kwa anthu ena.+ Pakuti ine ndidzatambasula dzanja langa ndi kuwononga anthu okhala m’dzikoli,” watero Yehova.+ 13  “Pakuti aliyense wa iwo, kuyambira wamng’ono mpaka wamkulu akupeza phindu lachinyengo.+ Kuyambira mneneri mpaka wansembe, aliyense wa iwo akuchita zachinyengo.+ 14  Iwo akuyesa kuchiritsa mwachinyengo+ kuwonongeka kwa anthu anga ponena kuti, ‘Kuli mtendere! Kuli mtendere!’ pamene kulibe mtendere.+ 15  Kodi iwo anachita manyazi chifukwa chochita zinthu zonyansazi?+ Iwo sanachite manyazi ngakhale pang’ono, komanso sadziwa n’komwe kuchita manyazi.+ Choncho iwo adzagwa pamodzi ndi anthu amene akugwa.+ Pamene ndidzakhala ndikuwaimba mlandu adzapunthwa,” watero Yehova. 16  Yehova wauza anthuwo kuti: “Imani chilili panjira anthu inu, kuti muone ndi kufunsa za njira zakale, kuti mudziwe kumene kuli njira yabwino.+ Mukaipeza muyende mmenemo+ kuti mupeze mpumulo wa miyoyo yanu.”+ Koma iwo anapitiriza kunena kuti: “Ife sitiyendamo.”+ 17  “Koma anthu inu ndinakuutsirani alonda+ ndipo ndinati, ‘Mverani kulira kwa lipenga la nyanga ya nkhosa!’”+ Koma iwo anapitiriza kunena kuti: “Ife sitidzamvera.”+ 18  “Choncho tamverani, inu mitundu ya anthu, kuti mudziwe anthu inu, zimene zidzawachitikira. 19  Tamverani, inu okhala padziko lapansi! Ine ndikubweretsa tsoka pa anthu awa+ chifukwa cha maganizo awo,+ pakuti sanamvere mawu anga ndipo anapitirizabe kukana chilamulo changa.”+ 20  “N’chifukwa chiyani mukundibweretsera lubani* wochokera ku Sheba+ ndi mabango onunkhira ochokera kudziko lakutali? Zimenezi zili ndi ntchito yanji kwa ine? Nsembe zanu zopsereza zathunthu sizikundisangalatsa,+ ndipo nsembe zina zonse zimene mukupereka sizikundikondweretsa.”+ 21  Choncho Yehova wanena kuti: “Tsopano ndikuikira anthu awa zinthu zopunthwitsa,+ ndipo onse pamodzi, abambo ndi ana, adzapunthwa pa zinthu zimenezi, munthu aliyense limodzi ndi mnzake adzatheratu.”+ 22  Yehova wanena kuti: “Taonani! Anthu akubwera kuchokera kudziko la kumpoto. Pali mtundu wamphamvu umene udzadzutsidwa kuchokera kumalekezero a dziko lapansi.+ 23  Iwo adzagwira uta ndi nthungo.*+ Umenewu ndi mtundu wankhanza ndipo sudzachita chisoni. Mawu awo adzamveka ngati mkokomo wa nyanja+ ndipo adzabwera pamahatchi.+ Mtunduwo wafola pokonzekera kumenya nawe nkhondo ngati mmene mwamuna wankhondo amachitira, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni.”+ 24  Ife tamva uthenga wa zimenezi. Manja athu angoti lendee!+ Tagwidwa ndi nkhawa ndipo tikumva ululu ngati wa mkazi amene akubereka.+ 25  Musatuluke kupita kunja ndipo musayende m’njira pakuti kumeneko kuli lupanga la mdani. Zochititsa mantha zili paliponse.+ 26  Iwe mwana wamkazi wa anthu anga, vala chiguduli*+ ndi kuvimvinizika m’phulusa.+ Lira ngati kuti ukulira maliro a mwana wamwamuna mmodzi yekhayo. Lira mowawidwa mtima+ chifukwa wofunkha adzatiukira modzidzimutsa.+ 27  “Ndakusandutsa woyesa zitsulo pakati pa anthu anga. Ndakusandutsa wofufuza mosamala ndipo udzaonetsetsa ndi kufufuza njira zawo.+ 28  Onse ndi anthu ouma khosi kwambiri,+ oyenda uku ndi uku ngati anthu amiseche.+ Iwo ali ngati mkuwa ndi chitsulo. Onsewo ndi anthu owononga.+ 29  Zipangizo zopemerera moto+ zatenthedwa ndi moto ndipo pamoto wawo pakutuluka mtovu.+ Munthu wakhala akuyenga chitsulo mobwerezabwereza koma osaphula kanthu, ndipo zoipa sizinachotsedwemo.+ 30  Anthu adzawatcha, ‘siliva wokanidwa,’+ pakuti Yehova wawakana.”+

Mawu a M'munsi

Munthu “wachisasati” ndi munthu wopusa chifukwa chakuti anamulera momulekerera ndipo sanaphunzire ntchito kapena zinthu zina zomuthandiza pamoyo wake.
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Tikati nthungo tikutanthauza mkondo waung’ono, wopepukirako.
Ena amati “saka.”