Yeremiya 35:1-19

35  M’masiku a Yehoyakimu+ mwana wa Yosiya, mfumu ya Yuda, Yehova anauza Yeremiya kuti:  “Pita kunyumba ya Arekabu,+ ndipo ukalankhule nawo ndi kubwera nawo kunyumba ya Yehova. Ukalowe nawo m’chimodzi mwa zipinda zodyera ndipo ukawapatse vinyo kuti amwe.”  Pamenepo ndinatenga Yaazaniya, mwana wa Yeremiya mwana wa Habaziniya, pamodzi ndi abale ake. Ndinatenganso ana ake onse aamuna ndi mabanja onse a Arekabu.  Onsewa ndinawabweretsa m’nyumba ya Yehova. Ndinalowa nawo m’chipinda chodyera+ cha ana a Hanani mwana wa Igadaliya, munthu wa Mulungu woona. Chipinda chimenechi chinali pafupi ndi chipinda chodyera cha akalonga chimene chinali pamwamba pa chipinda chodyera cha Maaseya mwana wa Salumu,+ amene anali mlonda wa pakhomo.  Kenako ndinaika makapu odzaza vinyo ndi zipanda pamaso pa ana a Rekabu ndi kuwauza kuti: “Imwani vinyoyu.”  Koma iwo anati: “Sitingamwe vinyo, chifukwa Yonadabu mwana wa Rekabu,+ kholo lathu, anatilamula kuti, ‘Inuyo kapena ana anu musamamwe vinyo mpaka kalekale.+  Musamamange nyumba, musamafese mbewu, musamabzale mpesa kuti ukhale wanu. Muzikhala m’mahema masiku onse a moyo wanu kuti mukhale ndi moyo wautali padziko lapansi limene mukukhala monga alendo.’+  Choncho ife timamvera mawu a Yehonadabu mwana wa Rekabu kholo lathu, pa chilichonse chimene anatilamula.+ Timachita zimenezi mwa kupewa kumwa vinyo masiku onse a moyo wathu, ifeyo, akazi athu, ana athu aamuna ndi ana athu aakazi.+  Sitimanga nyumba zoti tikhalemo ndipo sitibzala mpesa, kulima minda kapena kubzala mbewu kuti zikhale zathu. 10  Timakhala m’mahema ndipo timamvera ndi kutsatira zonse zimene Yonadabu,+ kholo lathu linatilamula.+ 11  Koma pamene Nebukadirezara mfumu ya Babulo anabwera kudzaukira dzikoli+ tinati, ‘Tiyeni tilowe mu Yerusalemu chifukwa kukubwera magulu ankhondo a Akasidi ndi magulu ankhondo a ku Siriya. Tiyeni tikakhale mu Yerusalemu.’”+ 12  Yehova anapitiriza kulankhula ndi Yeremiya kuti: 13  “Yehova wa makamu, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti, ‘Pita ukalankhule ndi anthu a ku Yuda ndi anthu okhala mu Yerusalemu kuti: “Kodi inu simunali kulimbikitsidwa nthawi zonse kuti muzimvera mawu anga?”+ watero Yehova. 14  “Anthu a m’nyumba ya Rekabu akhala akutsatira mawu a Yehonadabu mwana wa Rekabu,+ amene analamula ana ake kuti asamwe vinyo, ndipo sanamwe vinyo kufikira lerolino. Iwo achita zimenezi chifukwa chomvera lamulo la kholo lawo.+ Koma ine ndinali kulankhula nanu anthu inu, kudzuka m’mawa kwambiri ndi kulankhula nanu,+ koma simunandimvere.+ 15  Ndinali kukutumizirani atumiki anga onse aneneri,+ kudzuka m’mawa kwambiri ndi kuwatumiza. Ndinali kuwatuma uthenga wakuti, ‘Bwererani chonde, aliyense asiye njira zake zoipa+ ndipo sinthani zochita zanu kuti zikhale zabwino.+ Musatsatire milungu ina ndi kuitumikira.+ Mupitirize kukhala m’dziko limene ndinakupatsani, inuyo ndi makolo anu.’+ Koma inu simunatchere khutu kapena kundimvera.+ 16  Ana a Yehonadabu mwana wa Rekabu+ atsatira lamulo limene kholo lawo linawalamula,+ koma anthu awa sanandimvere.”’”+ 17  “Choncho Yehova, Mulungu wa makamu, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti, ‘Tsopano Yuda ndi anthu onse okhala mu Yerusalemu ndiwagwetsera masoka onse amene ndanena.+ Ndichita zimenezi chifukwa ndalankhula nawo koma sanandimvere ndipo ndinali kuwaitana koma sanandiyankhe.’”+ 18  Ndiyeno Yeremiya anauza anthu a m’nyumba ya Rekabu kuti: “Yehova wa makamu, Mulungu wa Isiraeli wanena kuti, ‘Chifukwa chakuti mwamvera lamulo la kholo lanu Yehonadabu,+ ndipo mukupitiriza kusunga malamulo ake onse ndi kuchita zonse zimene anakulamulani,+ 19  Yehova wa makamu, Mulungu wa Isiraeli wanena kuti: “Sipadzasowa munthu wa m’banja la Yonadabu mwana wa Rekabu woima+ pamaso panga kuti azinditumikira nthawi zonse.”’”+

Mawu a M'munsi