Yeremiya 33:1-26

33  Yeremiya atamutsekera m’Bwalo la Alonda,+ Yehova analankhula naye kachiwiri kuti:  “Yehova Wopanga+ dziko lapansi, Yehova Woumba+ dzikoli ndi kulikhazikitsa.+ Mulungu amene dzina lake ndi Yehova,+ wanena kuti,  ‘Mundiitane ndipo ndidzakuyankhani.+ Nthawi yomweyo ndidzakuuzani zinthu zazikulu ndi zovuta kuzimvetsa zimene simukuzidziwa.’”+  “Pakuti Yehova Mulungu wa Isiraeli wanena mawu okhudza nyumba za mumzinda uwu ndiponso okhudza nyumba za mafumu a Yuda zimene zagwetsedwa podziteteza ku ziunda zomenyerapo nkhondo ndiponso ku lupanga la adani.+  Wanenanso mawu okhudza amuna amene akubwera kudzamenyana ndi Akasidi, ndiponso okhudza malo amene adzaza ndi mitembo ya amuna amene wawapha chifukwa cha mkwiyo wake waukulu,+ amenenso ali oipa kwambiri moti iye wausiya mzindawu chifukwa cha kuipa kwa anthu amenewo.+  Iye wanena kuti: ‘Ine ndichiritsa anthu a mumzindawu ndi kuwapatsa thanzi labwino.+ Ndiwachiritsa ndi kuwapatsa mtendere wochuluka ndi choonadi.+  Ndibwezeretsa anthu a mu Yuda ndi a mu Isiraeli amene anagwidwa ndi kutengedwa kupita kudziko lina,+ ndipo ndiwalimbitsa kuti akhale ngati mmene analili poyamba.+  Ndiwayeretsa ku zolakwa zawo zonse zimene anachimwa nazo pamaso panga,+ ndipo ndiwakhululukira zolakwa zawo zonse zimene anandichimwira nazo ndi kuphwanya nazo malamulo anga.+  Mzindawu udzakhala ndi dzina limene lidzandikondweretsa,+ dzina lochititsa kuti nditamandidwe ndi kulandira ulemerero pakati pa mitundu yonse ya padziko lapansi imene idzamva za zinthu zabwino zimene ndikuwachitira.+ Anthu a mitundu inawo adzachita mantha+ ndi kunjenjemera+ chifukwa cha zinthu zabwino ndi mtendere wonse umene ndikubweretsa pamzindawu.’”+ 10  “Yehova wanena kuti, ‘Anthu inu mudzanena za dziko lino kuti ndi lopanda pake chifukwa mulibe anthu ndi ziweto. Mudzanena zimenezi za mizinda ya Yuda ndi misewu ya Yerusalemu imene yawonongeka,+ moti mulibe anthu ndipo simukukhala munthu aliyense ngakhale ziweto.+ 11  M’malo amenewa mudzamveka mawu achikondwerero ndi achisangalalo.+ Mudzamveka mawu a mkwati ndi mawu a mkwatibwi, ndi mawu a anthu onena kuti: “Tamandani Yehova wa makamu, pakuti Yehova ndi wabwino.+ Kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale!”’+ “‘Anthuwo azidzabweretsa nsembe yoyamikira kunyumba ya Yehova,+ pakuti ndidzabwezeretsa anthu a m’dzikoli amene anagwidwa ndi kutengedwa kupita kudziko lina kuti akhalenso ngati mmene analili poyamba,’+ watero Yehova.” 12  “Yehova wa makamu wanena kuti, ‘M’dziko lino lopanda pake, lopanda anthu ndi lopanda ziweto+ ndi mizinda yake yonse, mudzakhala malo odyetserako ziweto kumene abusa adzalola ziweto zawo kugona pansi.’+ 13  “Yehova wanena kuti, ‘Ziweto zidzadutsa pansi pa dzanja la munthu woziwerenga+ m’mizinda ya m’madera amapiri, m’mizinda ya m’chigwa,+ m’mizinda ya kum’mwera,+ m’dziko la Benjamini,+ m’madera ozungulira Yerusalemu+ ndi m’mizinda ya Yuda.’”+ 14  “‘Taonani! Masiku adzafika+ pamene ndidzakwaniritsa lonjezo langa+ lokhudza nyumba ya Isiraeli+ ndi nyumba ya Yuda,’ watero Yehova. 15  M’masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo ndidzameretsera Davide mphukira yolungama+ ndipo mphukirayo idzaweruza mwachilungamo m’dzikoli.+ 16  M’masiku amenewo, Yuda adzapulumutsidwa+ ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere.+ Yerusalemu adzatchedwa kuti, Yehova Ndiye Chilungamo Chathu.’”+ 17  “Yehova wanena kuti, ‘M’nyumba ya Davide simudzasowa munthu wokhala pampando wachifumu wa nyumba ya Isiraeli.+ 18  Ndipo ponena za ansembe achilevi, pakati pawo sindidzasowa mwamuna wopereka nsembe zopsereza zathunthu, nsembe yambewu yofukiza komanso nsembe zina nthawi zonse.’”+ 19  Yehova analankhulanso ndi Yeremiya kuti: 20  “Yehova wanena kuti, ‘Ngati anthu inu mungathe kuphwanya pangano langa loti kukhale usana ndi pangano langa loti kukhale usiku, kuti usana ndi usiku zisafike pa nthawi yake,+ 21  ndiye kuti inenso ndingathe kuphwanya pangano langa ndi Davide mtumiki wanga+ kuti asakhale ndi mwana woti adzalamulire monga mfumu pampando wachifumu wa Davide.+ Ndingachitenso chimodzimodzi ndi atumiki anga, ansembe achilevi.+ 22  Ine ndidzachulukitsa mbewu ya Davide mtumiki wanga ndi Alevi amene akunditumikira.+ Ndidzawachulukitsa mofanana ndi makamu akumwamba amene sangathe kuwerengedwa ndiponso mofanana ndi mchenga umene munthu sangathe kuuyeza.’”+ 23  Yehova anapitiriza kulankhula ndi Yeremiya kuti: 24  “Kodi sunamve zimene ena mwa anthu awa akunena kuti, ‘Mabanja awiri amene Yehova wasankha,+ adzawakananso’? Adani akuchitira anthu anga zachipongwe+ ndipo sakuwaonanso ngati mtundu wa anthu. 25  “Yehova wanena kuti, ‘Monga momwedi ndinakhazikitsira pangano langa loti kukhale usana ndi usiku,+ malamulo anga akumwamba ndi dziko lapansi,+ 26  momwemonso sindidzakana mbewu ya Yakobo ndi mbewu ya Davide mtumiki wanga,+ kuti pakati pa mbewu yake nditengepo olamulira mbewu ya Abulahamu, Isaki ndi Yakobo. Pakuti ndidzasonkhanitsa onse amene anagwidwa ndi kutengedwa kupita kudziko lina+ ndipo ndidzawamvera chisoni.’”+

Mawu a M'munsi