Yeremiya 30:1-24

30  Mawu amene Yehova anauza Yeremiya ndi awa:  “Yehova Mulungu wa Isiraeli wanena kuti, ‘Lemba m’buku mawu onse amene ndidzalankhula nawe.+  Pakuti, “taona! masiku adzafika,” watero Yehova, “pamene ndidzasonkhanitsa Isiraeli ndi Yuda,+ anthu anga amene anagwidwa ndi kutengedwa kupita kudziko lina,” watero Yehova. “Iwo ndidzawabwezeretsa kudziko limene ndinapatsa makolo awo ndipo adzalitenga kukhalanso lawo.”’”+  Awa ndi mawu amene Yehova wauza Isiraeli ndi Yuda.  Yehova wanena kuti: “Ife tamva phokoso la anthu amene akunjenjemera. Iwo agwidwa ndi mantha+ ndipo palibe mtendere.  Anthu inu, funsani kuti mudziwe ngati mwamuna angabale mwana.+ N’chifukwa chiyani mwamuna aliyense wamphamvu akuoneka atagwira manja m’chiuno ngati mkazi amene akubala mwana? N’chifukwa chiyani nkhope zawo zonse zafooka?+  Kalanga ine! Tsiku limeneli ndi lalikulu+ moti palibe lofanana nalo.+ Limeneli ndi tsiku la masautso kwa Yakobo.+ Koma adzapulumuka m’masautso amenewa.”  “Pa tsikuli ndidzathyola goli ndi kulichotsa m’khosi lanu. Ndidzadula zingwe zimene akumangani nazo,+ moti alendowo sadzagwiritsanso ntchito Yakobo monga wantchito wawo,” watero Yehova wa makamu.  “Inu mudzatumikira Yehova Mulungu wanu ndi Davide mfumu yanu+ imene ndidzakuutsirani.”+ 10  “Koma iwe Yakobo mtumiki wanga usachite mantha, iwe Isiraeli usagwidwe ndi mantha,”+ watero Yehova. “Pakuti ine ndikukupulumutsa kuchokera kutali ndipo ndikupulumutsanso ana ako kuchokera kudziko limene anatengedwa kukakhala akapolo.+ Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala mosatekeseka komanso mopanda zosokoneza. Sipadzakhala womuopsa.”+ 11  “Pakuti ine ndili ndi iwe kuti ndikupulumutse,”+ watero Yehova. “Ndidzawononga anthu a mitundu yonse ya kumene ndinakubalalitsirani,+ koma iwe sindidzakuwononga.+ Ndidzakuwongolera pa mlingo woyenera chifukwa sindidzakusiya osakulanga.”+ 12  Yehova wanena kuti: “Sudzachira kuvulala kwako.+ Chilonda chako cha mkwapulo ndi chosachiritsika.+ 13  Palibe amene akuchonderera kuti chilonda chako chipole.+ Palibe njira iliyonse yokuchiritsira ndipo palibe mankhwala amene angakuthandize.+ 14  Achigololo onse amene anali kukukonda kwambiri akuiwala.+ Iwo sakukufunafunanso. Ndakumenya ndi mkwapulo+ ngati mdani ndipo ndakulanga ngati munthu wankhanza+ chifukwa cha kuchuluka kwa zolakwa zako.+ Machimo ako achuluka kwambiri.+ 15  N’chifukwa chiyani ukulira pamene wadzivulaza mwadala?+ Ululu wako ndi wosachiritsika chifukwa zolakwa zako zachuluka ndipo machimo ako ndi ochuluka kwambiri.+ Ine ndakuchitira zimenezi. 16  Choncho, onse okuwononga adzawonongedwa,+ ndipo adani ako onse adzatengedwa kupita ku ukapolo.+ Amene akulanda katundu wako nawonso adzalandidwa katundu wawo. Onse ofunkha zinthu zako nawonso zinthu zawo zidzafunkhidwa.”+ 17  “Ndidzakubwezeretsa mwakale ndipo ndidzachiritsa zilonda zako za mkwapulo,”+ watero Yehova. “Iwo anakutcha kuti mkazi wothamangitsidwa ndipo anali kunena kuti:+ ‘Ameneyu ndi Ziyoni ndipo palibe amene akumufunafuna.’”+ 18  Yehova wanena kuti: “Ndikusonkhanitsa anthu a m’mahema a Yakobo+ amene anagwidwa ndi kutengedwa kupita kudziko lina ndipo ndidzamvera chisoni malo okhala a Yakobo. Mzinda udzamangidwanso pachiunda chake+ ndipo nsanja yokhalamo idzakhala pamalo ake oyenera.+ 19  Kwa iwo kudzamveka mawu oyamikira ndi phokoso la kuseka kwa anthu.+ Ndidzawachulukitsa moti sadzakhala ochepa.+ Ndidzachulukitsa chiwerengero chawo moti sadzakhala kagulu kakang’ono ka anthu.+ 20  Ana ake aamuna adzabwerera mwakale ndipo khamu la anthu ake lidzakhazikika pamaso panga.+ Ndidzalanga onse omupondereza.+ 21  Munthu wotchuka adzachokera mwa iye+ ndipo pakati pa anthu ake padzatuluka wolamulira.+ Ndidzamulola kundiyandikira ndipo adzabwera kwa ine.”+ “Tsopano uyu ndani amene wapereka mtima wake ngati chikole kuti ayandikire kwa ine?”+ watero Yehova. 22  “Inu mudzakhaladi anthu anga+ ndipo ine ndidzakhala Mulungu wanu.”+ 23  Taonani! Mphepo yamkuntho yochokera kwa Yehova yawomba. Mkwiyo wake wawomba ngati kamvulumvulu wosakaza.+ Wawomba pamitu ya anthu oipa.+ 24  Mkwiyo woyaka moto wa Yehova sudzatha kufikira atachita zofuna za mtima wake ndi kuzikwaniritsa.+ M’masiku otsiriza, anthu inu mudzalingalira zimenezi.+

Mawu a M'munsi