Yeremiya 3:1-25

3  Pali mawu akuti: “Mwamuna akathetsa ukwati ndi mkazi wake, ndipo mkaziyo n’kuchokadi ndi kukakwatiwa ndi mwamuna wina, sangabwererenso kwa mwamuna woyamba uja.”+ Kodi dzikoli silinaipitsidwe kale?+ Yehova wanena kuti: “Iwe wachita uhule ndi amuna ambirimbiri.+ Kodi m’poyenera kuti ubwererenso kwa ine?+  Kweza maso ako ndi kuona njira zodutsidwadutsidwa.+ Ndi pamalo ati pamene amuna sanakugonerepo?+ Unali kukhala m’mbali mwa njira kudikirira okondedwa ako, ngati mmene Mluya amakhalira m’chipululu.+ Ukuipitsa dzikoli ndi zochita zako zauhule komanso kuipa kwako.+  Choncho mvula yamvumbi yasiya kugwa,+ ndipo mvula yomalizira siinagwe.+ Ukuchita zinthu mopanda manyazi ngati mkazi amene akuchita uhule.* Palibe chimene chikukuchititsa manyazi.+  Tsopano wayamba kundiitana kuti, ‘Atate wanga,+ ndinu bwenzi langa lapamtima kuyambira pa unyamata wanga.+  Kodi mukhala wokwiya mpaka kalekale?* Kapena kodi muzingoyang’anira machimo athu mpaka muyaya?’+ Taona! Iwe wanena ndi kuchita zinthu zoipa ndipo wapambana.”+  Yehova anapitiriza kulankhula nane m’masiku a Mfumu Yosiya kuti:+ “‘Kodi waona zimene Isiraeli wosakhulupirikayu akuchita?+ Akupita kuphiri lililonse lalitali+ ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu wa masamba ambiri obiriwira+ kuti akachite uhule kumeneko.+  Pambuyo poti wachita zinthu zonsezi, ine ndinamupempha mobwerezabwereza kuti abwerere kwa ine, koma iye sanabwerere.+ Ndipo Yuda anali kungoyang’anitsitsa zimene m’bale wake wachinyengoyo anali kuchita.+  Nditaona zimenezo, ndinam’pitikitsa+ ndipo ndinamupatsa kalata yotsimikizira kuti ukwati watha+ chifukwa chakuti Isiraeli wosakhulupirikayu anachita chigololo. Koma Yuda amene ndi m’bale wake wochita zachinyengo sanachite mantha ndipo nayenso anayamba kuchita uhule.+  Iye anayamba kuchita uhule chifukwa choona nkhani imeneyi mopepuka. Anali kuipitsa dzikolo+ ndi kuchita chigololo ndi miyala komanso mitengo.+ 10  Ngakhale kuti m’bale wake Yuda amene anali wochita zachinyengoyo anaona zonsezi, iye sanabwerere kwa ine ndi mtima wake wonse+ koma anangobwerera mwachiphamaso,’+ watero Yehova.” 11  Yehova anapitiriza kundiuza kuti: “Isiraeli wosakhulupirikayo wakhala wolungama kuposa Yuda wochita zachinyengoyo.+ 12  Pita, ndipo ukalengeze mawu awa kumpoto+ kuti: “‘Yehova wanena kuti: “Bwerera Isiraeli wopanduka iwe. Sindidzakuyang’anani mokwiya anthu inu+ pakuti ndine wokhulupirika,”+ watero Yehova.+ “Sindidzakhala wokwiya mpaka kalekale.+ 13  Koma ganizirani zolakwa zanu chifukwa mwaphwanya malamulo a Yehova Mulungu wanu.+ Anthu inu simunamvere mawu anga, koma munapitiriza kupanga njira zambirimbiri zopita kwa anthu achilendo+ pansi pa mtengo uliwonse waukulu wa masamba ambiri obiriwira,”+ watero Yehova.’” 14  “Bwererani inu ana opanduka,”+ watero Yehova. “Ine ndakhala mwamuna wanu anthu inu.+ Ine ndidzakutengani, mmodzi kuchokera mumzinda uliwonse, awiri kuchokera mu fuko lililonse ndipo ndidzakupititsani ku Ziyoni.+ 15  Ndidzakupatsani abusa amene mtima wanga wakonda+ ndipo iwo adzakuthandizani kudziwa zinthu zambiri ndiponso kumvetsa bwino zinthu.+ 16  Pamenepo mudzabalana ndi kuchuluka m’dzikoli masiku amenewo,” watero Yehova.+ “Iwo sadzafuulanso kuti, ‘Likasa la pangano la Yehova!’+ Sadzaliganiziranso m’mitima yawo, kulikumbukira,+ kapena kulilakalaka ndipo sadzapanganso likasa lina. 17  Pa nthawiyo mzinda wa Yerusalemu adzautcha kuti mpando wachifumu wa Yehova.+ Ndipo mitundu yonse adzaisonkhanitsira+ ku Yerusalemu kuti ikatamande dzina la Yehova+ kumeneko. Iwo sadzaumitsanso mitima yawo yoipayo.”+ 18  “M’masiku amenewo nyumba ya Yuda idzayenda pamodzi ndi nyumba ya Isiraeli,+ ndipo onse+ adzatuluka m’dziko la kumpoto ndi kulowa m’dziko limene ndinapereka kwa makolo anu monga cholowa chawo.+ 19  Ine ndanena kuti, ‘Mokondwera ndinakuikani pakati pa ana anga ndi kukupatsani dziko labwino,+ cholowa chimene mitundu yambiri ya anthu imachisirira!’ Ndipo ndinanenanso kuti, ‘Anthu inu mudzandiitana kuti, “Atate wanga!”+ ndipo mudzandilondola osabwerera.’ 20  ‘Ndithudi, monga mmene mkazi amasiyira mwamuna wake+ mwachinyengo, inunso a m’nyumba ya Isiraeli mwandichitira zachinyengo,’+ watero Yehova.” 21  Panjira zodutsidwadutsidwa pamveka mawu a ana a Isiraeli, kulira ndi kuchonderera kwawo. Pakuti iwo akhotetsa njira zawo+ ndipo aiwala Yehova Mulungu wawo.+ 22  “Bwererani, inu ana opanduka.+ Ndidzachiritsa kusakhulupirika kwanu.”+ “Ife tabwerera! Tabwera kwa inu, pakuti inu Yehova ndinu Mulungu wathu.+ 23  Ndithudi, zitunda ndi chipwirikiti chimene chimachitika m’mapiri+ ndiko kupembedza kwachinyengo.+ Kunena zoona chipulumutso cha Isiraeli chili mwa Yehova Mulungu wathu.+ 24  Chinthu chochititsa manyazi+ chadya ntchito yolemetsa ya manja a makolo athu kuyambira tili anyamata. Chadya nkhosa zawo, ng’ombe zawo, ana awo aamuna ndi ana awo aakazi. 25  Tagona pansi mwamanyazi+ ndipo manyazi athuwo akupitiriza kutiphimba.+ Zimenezi zakhala choncho chifukwa chakuti ifeyo ndi makolo athu, tachimwira Yehova Mulungu wathu+ ndipo sitinamvere mawu a Yehova Mulungu wathu+ kuyambira tili anyamata mpaka lero.”+

Mawu a M'munsi

Mawu ake enieni, “uli ndi nkhope ya mkazi wochita uhule.”
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.