Yeremiya 13:1-27

13  Yehova wandiuza kuti: “Pita ukatenge lamba wansalu ndipo ukamumange m’chiuno mwako, koma asakakhudze madzi.”  Choncho ndinapita kukatenga lambayo mogwirizana ndi mawu a Yehova ndipo ndinamumanga m’chiuno mwanga.  Ndiyeno Yehova analankhulanso nane kachiwiri kuti:  “Tenga lamba wabweretsayo amene wamumanga m’chiuno ndipo upite kumtsinje wa Firate.+ Kumeneko ukabise lambayo mumng’alu wa m’phanga.”  Pamenepo ndinanyamuka ndi kukabisa lambayo pafupi ndi mtsinje wa Firate monga mmene Yehova anandilamulira.  Ndiyeno patapita masiku ambiri Yehova anandiuza kuti: “Nyamuka, pita kumtsinje wa Firate ndipo ukatenge lamba amene ndinakulamula kuti ukabise kumeneko.”  Choncho ndinapita kumtsinje wa Firate ndipo ndinakumba pamalo amene ndinabisapo lambayo ndi kumutenga. Koma nditamuona, anali atawonongeka moti sakanagwiranso ntchito iliyonse.  Pamenepo Yehova anandiuzanso kuti:  “Yehova wanena kuti, ‘Mofanana ndi lamba ameneyu, ndidzawononga kunyada kwa Yuda+ ndiponso kunyada kwakukulu kwa Yerusalemu. 10  Anthu oipa amenewa akukana kumvera mawu anga.+ Iwo akupitirizabe kuumitsa mitima yawo+ ndipo akutsatira milungu ina kuti aitumikire ndi kuigwadira.+ Anthu amenewa adzakhala ngati lamba ameneyu amene sangagwirenso ntchito iliyonse.’ 11  ‘Ine ndinachititsa nyumba yonse ya Isiraeli ndi nyumba yonse ya Yuda kundimamatira+ mofanana ndi mmene lamba amagwirira m’chiuno mwa munthu,’ watero Yehova. ‘Ndinachita zimenezi kuti iwo akhale anthu anga,+ akhale dzina langa lotchuka,+ anditamande ndi kukhala chinthu changa chokongola. Koma iwo sanandimvere.’+ 12  “Tsopano uwauze kuti, ‘Yehova Mulungu wa Isiraeli wanena kuti: “Mtsuko uliwonse waukulu amadzazamo vinyo.”’+ Ukakawauza zimenezi, iwo adzakufunsa kuti, ‘Kodi ife sitikudziwa kuti mtsuko uliwonse waukulu amadzazamo vinyo?’ 13  Pamenepo ukawauze kuti, ‘Yehova wanena kuti: “Inetu ndikuledzeretsa+ anthu onse a m’dzikoli, mafumu amene akukhala pampando wa Davide,+ ansembe, aneneri ndi onse okhala mu Yerusalemu. 14  Ndipo ndidzawombanitsa munthu ndi mnzake, abambo ndi ana awo pa nthawi imodzi,”+ watero Yehova. “Sindidzawachitira chifundo kapena kuwamvera chisoni. Ndithu sindidzakhala ndi chifundo choti ndisawawononge.”’+ 15  “Tamverani anthu inu. Tcherani khutu. Musadzikweze+ pakuti Yehova ndi amene wanena zimenezi.+ 16  Patsani Yehova Mulungu wanu ulemerero+ asanachititse mdima,+ komanso mapazi anu asanapunthwe pamapiri madzulo dzuwa litalowa.+ Mudzayembekeza kuwala+ koma iye adzabweretsa mdima,+ ndipo adzachititsa mdima wandiweyani.+ 17  Ndipo ngati simudzamvera mawu ake+ ndidzalira ndi kugwetsa misozi m’malo obisika chifukwa cha kunyada kwanu. Maso anga adzatulutsa misozi+ chifukwa chakuti nkhosa+ za Yehova zidzakhala zitagwidwa ndi kutengedwa kupita kudziko lina. 18  “Uza mfumu ndi mayi a mfumu+ kuti, ‘Khalani pamalo apansi,+ pakuti chisoti chanu chaulemerero chidzachotsedwa pamutu panu ndi kuikidwa pansi.’+ 19  Mizinda ya kum’mwera yatsekedwa moti palibe amene akuitsegula. Yuda yense watengedwa kupita ku ukapolo. Watengedwa wathunthu kupita ku ukapolo.+ 20  “Kweza maso ako kuti uone anthu amene akubwera kuchokera kumpoto.+ Kodi nkhosa zimene anakupatsa, nkhosa zako zokongolazo zili kuti?+ 21  Kodi udzanenanji wina akadzatembenukira kwa iwe+ ngakhale kuti iweyo unamuchititsa kukhala bwenzi lako lapamtima, limene unali kukondana nalo kwambiri kuyambira pa chiyambi?+ Kodi zowawa za pobereka ngati za mkazi amene akubereka mwana sizidzakugwira?+ 22  Ukadzanena mumtima mwako kuti,+ ‘N’chifukwa chiyani zinthu zimenezi zandigwera?’+ pamenepo udzadziwe kuti wavulidwa siketi yako+ ndipo zidendene zako zazunzidwa chifukwa zolakwa zako zachuluka. 23  “Kodi Mkusi*+ angasinthe khungu lake, kapena kodi kambuku angasinthe mawanga ake?+ Ngati angathe kuchita zimenezi, ndiye kuti inunso amene munaphunzitsidwa kuchita zinthu zoipa mungathe kuchita zinthu zabwino.+ 24  Choncho ndidzakumwazani+ ngati mapesi amene akuuluka ndi mphepo kuchokera m’chipululu.+ 25  Limeneli ndilo gawo lako, malo ako amene ndakuyezera,”+ watero Yehova, “chifukwa chakuti wandiiwala+ ndipo ukupitirizabe kukhulupirira zinthu zachinyengo.+ 26  Ndidzakuvula siketi yako ndi kukuphimba nayo kumaso, moti udzachita manyazi.+ 27  Chigololo chako,+ kumemesa* kwako,+ khalidwe lako lotayirira la uhule, zonsezi zidzaonekera. Ndaona zinthu zako zonyansa pamapiri kuthengo.+ Tsoka kwa iwe Yerusalemu! Sungakhale woyera.+ Kodi udzakhalabe wosayera kufikira liti?”+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti “Mwitiyopiya.”
Mawu akuti “kumemesa” amatanthauza zimene nyama yamphongo imachita ikafuna kukwera.