Mlaliki 3:1-22

3  Chilichonse chili ndi nthawi yake,+ ndipo chilichonse chochitika padziko lapansi chilidi ndi nthawi yake:  Pali nthawi yobadwa+ ndi nthawi ya kufa.+ Nthawi yobzala ndi nthawi yozula chimene chinabzalidwa.+  Nthawi yakupha+ ndi nthawi yochiritsa.+ Nthawi yogumula ndi nthawi yomanga.+  Nthawi yolira+ ndi nthawi yoseka.+ Nthawi yolira mofuula+ ndi nthawi yodumphadumpha mosangalala.+  Nthawi yotaya miyala+ ndi nthawi younjika miyala pamodzi.+ Nthawi yokumbatirana+ ndi nthawi yosakumbatirana.+  Nthawi yofunafuna+ ndi nthawi yovomereza kuti chinthu chatayika. Nthawi yosunga ndi nthawi yotaya.+  Nthawi yong’amba+ ndi nthawi yosoka.+ Nthawi yokhala chete+ ndi nthawi yolankhula.+  Nthawi ya chikondi ndi nthawi ya chidani ndi munthu.+ Nthawi yankhondo+ ndi nthawi yamtendere.+  Kodi munthu wogwira ntchito mwakhama adzapeza phindu lanji pa ntchito yakeyo?+ 10  Ndaona ntchito imene Mulungu wapatsa ana a anthu kuti azigwira.+ 11  Chilichonse iye anachipanga chokongola ndiponso pa nthawi yake.+ Komanso anapatsa anthu mtima wofuna kukhala ndi moyo mpaka kalekale+ kuti ntchito imene Mulungu woona wagwira, iwo asaidziwe kuyambira pa chiyambi mpaka pa mapeto.+ 12  Ndazindikira kuti palibe chabwino kuposa kuti iwo asangalale ndiponso azichita zabwino pamene ali ndi moyo,+ 13  komanso kuti munthu aliyense adye ndi kumwa ndi kusangalala ndi zinthu zabwino, chifukwa choti wagwira ntchito mwakhama.+ Imeneyi ndi mphatso yochokera kwa Mulungu.+ 14  Ndazindikira kuti zonse zimene Mulungu woona amapanga zimakhala mpaka kalekale.+ Palibe choti n’kuwonjezerapo kapena choti n’kuchotsapo.+ Mulungu woona ndi amene wapanga zimenezi,+ kuti anthu azimuopa.+ 15  Zimene zilipo zinalipo kale, ndipo zimene zidzachitike zinachitikapo kale.+ Mulungu woona+ amafunafuna kuchitira zabwino anthu amene akuzunzidwa.+ 16  Ine ndaonanso padziko lapansi pano kuti pamene panayenera kukhala chilungamo panali zoipa, ndipo pamene panayenera kuchitika zachilungamo panachitika zoipa.+ 17  Ine ndinanena mumtima mwanga+ kuti: “Mulungu woona adzaweruza munthu wolungama ndi munthu woipa,+ pakuti iye ali ndi nthawi yochitira chinthu chilichonse ndiponso yokhudza ntchito iliyonse.”+ 18  Ineyo ndinanena mumtima mwanga kuti Mulungu woona adzasankhula ana a anthu. Zimenezi zidzawasonyeza kuti iwo ndi ofanana ndi zinyama.+ 19  Pakuti ana a anthu ali ndi mapeto, ndipo zinyamanso zili ndi mapeto. Mapeto a zonsezi ndi ofanana.+ Nyama imafa ndipo munthunso amafa.+ Mzimu wa zonsezi ndi umodzi,+ moti munthu saposa nyama, pakuti zonse n’zachabechabe. 20  Zonse zimapita kumalo amodzi.+ Zonse zinachokera kufumbi+ ndipo zonse zimabwerera kufumbi.+ 21  Ndani akudziwa ngati mzimu* wa ana a anthu umakwera m’mwamba, ndiponso ngati mzimu wa zinyama umatsika pansi?+ 22  Ine ndaona kuti palibe chabwino kuposa kuti munthu asangalale ndi ntchito yake,+ pakuti imeneyo ndi mphoto yake, popeza palibe amene adzam’bweretse kuti adzaone zimene zizidzachitika iye atafa.+

Mawu a M'munsi

Onani Zakumapeto 4.