Miyambo 5:1-23

5  Mwana wanga, mvetsera nzeru zanga.+ Tchera makutu ako ku zimene ndikukuphunzitsa zokhudza kuzindikira,+  kuti uteteze kuganiza bwino,+ ndiponso kuti milomo yako iteteze kudziwa zinthu.+  Pakuti milomo ya mkazi wachilendo imakha uchi ngati chisa cha njuchi+ ndipo m’kamwa mwake ndi mosalala kuposa mafuta.+  Koma zotsatirapo zochokera kwa iye n’zowawa kwambiri ngati chitsamba chowawa.+ N’zakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.+  Mapazi ake amatsikira ku imfa.+ Miyendo yake imalowera ku Manda.+  Iye saganizira njira ya moyo.+ Amangoyendayenda panjira zake osadziwa kumene akupita.+  Tsopano ananu ndimvereni,+ ndipo musapatuke pa mawu otuluka m’kamwa mwanga.+  Njira yako ikhale kutali ndi iye. Usayandikire pakhomo la nyumba yake,+  kuti usapereke ulemu wako kwa anthu ena+ kapena kupereka zaka zako ku zinthu zankhanza.+ 10  Ndiponso kuti alendo asakhute mphamvu zako,+ kuti zinthu zimene unazipeza movutikira* zisakhale m’nyumba ya mlendo,+ 11  komanso kuti usadzabuule m’tsogolo+ mnofu ndi thupi lako zikadzafika ku mapeto kwake.+ 12  Pa nthawiyo udzanena kuti: “Ndinkadana ndi malangizo* ine,+ ndipo mtima wanga sunkavomereza kudzudzula.+ 13  Sindinamvere mawu a alangizi anga,+ ndipo sindinatchere khutu kwa aphunzitsi anga.+ 14  N’chifukwa chake mosayembekezeka ndinagwera m’zinthu zoipa zamtundu uliwonse,+ ndipo ndinachita manyazi pamaso pa mpingo wonse.”+ 15  Imwa madzi ochokera m’chitsime chako, komanso madzi oyenderera kuchokera pakati pa chitsime chako.+ 16  Kodi akasupe ako amwazike panja,+ ndipo mitsinje yako yamadzi imwazike m’mabwalo a mumzinda? 17  Zimenezi zikhale zako zokha osatinso za alendo amene ali nawe.+ 18  Kasupe wa madzi ako akhale wodalitsidwa,+ ndipo usangalale ndi mkazi wapaunyamata wako.+ 19  Iye akhale ngati mbawala yaikazi yokondedwa ndiponso ngati mbuzi yokongola ya m’mapiri.+ Mabere ake akukhutiritse nthawi zonse.+ Nthawi zonse uzikhala wokondwa kwambiri ndi chikondi chake.+ 20  Chotero pali chifukwa chanji choti usangalalire ndi mkazi wachilendo mwana wanga, kapena choti ukumbatirire chifuwa cha mkazi wina?+ 21  Pakuti njira za munthu zili pamaso pa Yehova,+ ndipo iye amaonetsetsa njira zake zonse.+ 22  Woipa adzagwidwa ndi zolakwa zake zomwe,+ ndipo adzamangidwa m’zingwe za tchimo lake lomwe.+ 23  Iye adzafa chifukwa chosamvera malangizo,+ ndiponso chifukwa chakuti amasocheretsedwa ndi zopusa zake zochuluka.+

Mawu a M'munsi

Mawu ake enieni, “zimene unazipeza ukumva kupweteka.”
Onani mawu a m’munsi pa Miy 1:2.