Miyambo 29:1-27

29  Munthu wodzudzulidwa kawirikawiri+ koma amene amaumitsa khosi lake,+ adzathyoledwa mwadzidzidzi ndipo akadzatero sadzachira.+  Olungama akachuluka, anthu amasangalala,+ koma aliyense woipa akayamba kulamulira, anthu amabuula.+  Munthu wokonda nzeru amasangalatsa bambo ake,+ koma woyenda ndi mahule amawononga zinthu zamtengo wapatali.+  Pochita zinthu zachilungamo, mfumu imachititsa dziko kulimba,+ koma munthu wokonda ziphuphu amaligwetsa.+  Mwamuna wamphamvu amene amanena zabwino za mnzake mokokomeza,+ akuyalira ukonde mapazi ake.+  Tchimo la munthu woipa limamutchera msampha,+ koma munthu wolungama amafuula mokondwera ndipo amasangalala.+  Wolungama amaganizira za mlandu wa anthu onyozeka.+ Woipa saganizira zimenezo.+  Anthu olankhula modzitama amabutsa mkwiyo wa mzinda,+ koma anthu anzeru amaletsa mkwiyo.+  Munthu wanzeru akakhala pa mlandu ndi chitsiru, chitsirucho chimangochita phokoso n’kumaseka, ndipo munthu wanzeruyo sapeza mpumulo.+ 10  Anthu okonda kukhetsa magazi amadana ndi aliyense wopanda cholakwa,+ koma anthu owongoka mtima amasamalira moyo wa anthu opanda cholakwawo.+ 11  Wopusa amatulutsa mkwiyo* wake wonse, koma wanzeru amakhala wodekha mpaka pamapeto.+ 12  Mtsogoleri akamamvera mabodza, onse omutumikira adzakhala oipa.+ 13  Munthu wosauka ndiponso munthu wozunza ena n’chimodzimodzi,+ koma Yehova amawalitsa maso a onsewa.+ 14  Mfumu ikamaweruza anthu onyozeka mwachilungamo,+ mpando wake wachifumu udzakhazikika mpaka kalekale.+ 15  Chikwapu ndi chidzudzulo n’zimene zimapereka nzeru,+ koma mwana womulekerera adzachititsa manyazi mayi ake.+ 16  Oipa akachuluka, machimo amachuluka, koma olungama adzawaona oipawo akugwa.+ 17  Langa mwana wako ndipo adzakupatsa mpumulo ndiponso adzasangalatsa kwambiri moyo wako.+ 18  Popanda kutsogozedwa ndi Mulungu, anthu amatayirira,+ koma odala ndi amene amasunga malamulo.+ 19  Wantchito salola kusintha ndi mawu okha,+ chifukwa amamvetsa koma satsatira.+ 20  Kodi waona munthu wopupuluma m’mawu ake?+ Munthu wopusa ali ndi chiyembekezo chachikulu kuposa iyeyo.+ 21  Ngati munthu akusasatitsa* wantchito wake kuyambira ali mwana, akadzakula adzakhala wosayamika. 22  Munthu wokonda kukwiya amayambitsa mkangano,+ ndipo aliyense wokonda kupsa mtima amakhala ndi machimo ambiri.+ 23  Kudzikuza kwa munthu wochokera kufumbi kudzamutsitsa,+ koma wa mtima wodzichepetsa adzapeza ulemerero.+ 24  Wochita ubwenzi ndi mbala akudana ndi moyo wake.+ Iye angamve lumbiro lokhudza temberero, koma osakanena chilichonse.+ 25  Kuopa anthu n’kumene kumatchera msampha,+ koma wokhulupirira Yehova adzatetezedwa.+ 26  Anthu ambiri amafuna kuonana ndi mtsogoleri,+ koma chiweruzo cha munthu chimachokera kwa Yehova.+ 27  Munthu wopanda chilungamo amakhala wonyansa kwa anthu olungama,+ ndipo munthu wowongoka m’njira yake amakhala wonyansa kwa munthu woipa.+

Mawu a M'munsi

Mawu ake enieni, “mzimu.”
Munthu wosasatitsidwa ndi munthu wopusa chifukwa chakuti anamulera momulekerera ndipo sanaphunzire ntchito kapena zinthu zina zomuthandiza pamoyo wake.