Miyambo 28:1-28

28  Anthu oipa amathawa popanda wowathamangitsa,+ koma olungama ali ngati mkango wamphamvu umene umakhala wolimba mtima.+  Anthu okhala m’dziko akamachimwa pamakhala akalonga ambiri otsatizanatsatizana,+ koma chifukwa cha munthu wozindikira, wodziwa zinthu zoyenera kuchita, kalonga amakhala kwa nthawi yaitali.+  Mwamuna wamphamvu wosauka amene amabera mwachinyengo anthu onyozeka,+ ali ngati mvula imene imakokolola zinthu moti sipakhalanso chakudya.  Anthu osiya chilamulo akamatamanda munthu woipa,+ anthu amene amasunga chilamulo amawaukira.+  Anthu okonda kuchita zoipa sangamvetse chilungamo, koma amene akufunafuna Yehova amamvetsa chilichonse.+  Munthu wosauka amene akuyenda ndi mtima wosagawanika, ali bwino kuposa munthu aliyense woyenda m’njira zokhota, ngakhale ali wolemera.+  Mwana womvetsa zinthu amasunga malamulo,+ koma wochita ubwenzi ndi anthu osusuka amachititsa manyazi bambo ake.+  Munthu amene amachulukitsa zinthu zamtengo wapatali kuchokera ku chiwongoladzanja ndi katapira,*+ amangosungira zinthuzo munthu amene amakomera mtima anthu onyozeka.+  Munthu amene amathawitsa khutu lake kuti asamve chilamulo,+ ngakhale pemphero lake limakhala lonyansa.+ 10  Munthu amene amasocheretsa anthu owongoka mtima+ kuti ayende m’njira yoipa, adzagwera m’dzenje lake lomwe.+ Koma anthu osalakwa adzapeza zabwino.+ 11  Munthu wolemera amadziona ngati wanzeru m’maso mwake,+ koma munthu wonyozeka amene ali wozindikira zinthu amam’fufuza n’kudziwa zoona zake.+ 12  Anthu olungama akamasangalala+ zimakhala bwino kwambiri, koma anthu oipa akamalamulira, munthu amadzisintha maonekedwe.+ 13  Wobisa machimo ake zinthu sizidzamuyendera bwino,+ koma woulula n’kuwasiya adzachitiridwa chifundo.+ 14  Wodala ndi munthu amene amaopa Mulungu nthawi zonse,+ koma woumitsa mtima wake adzagwera m’tsoka.+ 15  Mtsogoleri woipa wolamulira anthu onyozeka ali ngati mkango wobangula ndiponso chimbalangondo chimene chikubwera kudzakuluma.+ 16  Mtsogoleri amene ali wosazindikira kwenikweni amakhalanso wakatangale kwambiri,+ koma munthu wodana ndi phindu lachinyengo+ adzachulukitsa masiku ake. 17  Munthu wolemedwa ndi mlandu wokhetsa magazi a munthu adzakhala wothawathawa mpaka kumanda.+ Anthu asamugwire n’cholinga choti amuletse. 18  Woyenda mosalakwa adzapulumutsidwa,+ koma woyenda m’njira zokhota adzagwa mwadzidzidzi.+ 19  Munthu amene amalima munda wake adzakhala ndi chakudya chokwanira,+ ndipo amene amafunafuna zinthu zopanda phindu adzakhala ndi umphawi waukulu.+ 20  Munthu wochita zinthu mokhulupirika adzapeza madalitso ambiri,+ koma woyesetsa kuti apeze chuma mofulumira, sadzapitiriza kukhala wosalakwa.+ 21  Si bwino kukondera.+ Si bwinonso kuti mwamuna wamphamvu achimwe chifukwa cha kachidutswa ka mkate. 22  Munthu wanjiru amayesetsa kuti apeze zinthu zamtengo wapatali,+ koma sadziwa kuti umphawi udzamugwera. 23  Wodzudzula munthu,+ patsogolo pake adzakondedwa kwambiri kuposa amene amakokomeza ndi lilime lake ponena zinthu zabwino za wina. 24  Wobera bambo ake ndi mayi ake+ n’kumanena kuti: “Si kulakwa,”+ amakhala mnzake wa munthu wobweretsa chiwonongeko. 25  Munthu wonyada amayambitsa mikangano,+ koma wodalira Yehova adzanenepa.+ 26  Munthu wodalira mtima wake ndi wopusa,+ koma woyenda mwanzeru ndi amene adzapulumuke.+ 27  Wopatsa zinthu munthu wosauka sadzasowa kanthu,+ koma wophimba maso ake adzapeza matemberero ambiri.+ 28  Oipa akamalamulira, munthu amadzibisa.+ Koma oipawo akatha anthu olungama amachuluka.+

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa Eks 22:25.