Miyambo 24:1-34

24  Usamasirire anthu oipa,+ ndipo usamasonyeze kuti ukusirira kukhala pagulu lawo,+  chifukwa mtima wawo umangokhalira kuganizira zolanda zinthu za ena, ndipo milomo yawo imangokhalira kunena zobweretsera ena mavuto.+  Nzeru zimamanga banja la munthu,+ ndipo kuzindikira kumachititsa kuti lilimbe kwambiri.+  Kudziwa zinthu kumachititsa kuti zipinda zamkati mwa nyumba zidzaze ndi zinthu zonse zamtengo wapatali ndiponso zosangalatsa.+  Munthu amene amagwiritsa ntchito mphamvu zake mwanzeru ndiye mwamuna wamphamvu,+ ndipo munthu wodziwa zinthu amachulukitsa mphamvu zake.+  Iweyo udzatha kumenya nkhondo yako potsatira malangizo anzeru,+ ndipo pakakhala aphungu ochuluka anthu amapulumuka.+  Kwa munthu wopusa, nzeru zenizeni n’chinthu chapatali.+ Iye satsegula pakamwa pake pachipata cha mzinda.  Aliyense wokonzera anzake ziwembu adzatchedwa katswiri wa maganizo oipa.+  Khalidwe lotayirira lobwera chifukwa cha kupusa limakhala tchimo,+ ndipo munthu wonyoza, anthu amanyansidwa naye.+ 10  Ukafooka pa tsiku la masautso,+ mphamvu zako zidzakhala zochepa. 11  Pulumutsa anthu amene atengedwa kuti akaphedwe, ndipo amene akudzandira popita ku imfa, chonde uwabweze.+ 12  Ukanena kuti: “Ifetu izi sitinali kuzidziwa,”+ kodi amene amafufuza mitima sazindikira zimenezo?+ Ndipo kodi amene amayang’anitsitsa moyo wako sadziwa zimenezo+ n’kubwezera munthu wochokera kufumbi mogwirizana ndi ntchito yake?+ 13  Mwana wanga, idya uchi chifukwa ndi wabwino, ndipo uchi wotsekemera wochokera pazisa za njuchi uuike m’kamwa mwako.+ 14  M’njira yomweyo, dziwa nzeru kuti upindule.+ Ukazipeza, udzakhala ndi tsogolo labwino ndipo chiyembekezo chako sichidzawonongedwa.+ 15  Mofanana ndi munthu woipa, usamabisalire munthu wolungama pamalo ake okhala.+ Usamasakaze malo ake okhala,+ 16  pakuti wolungama akhoza kugwa ngakhale nthawi 7 ndipo ndithu adzadzukanso.+ Koma anthu oipa, tsoka lidzawapunthwitsa.+ 17  Mdani wako akagwa usamasangalale ndipo akapunthwa, mtima wako usamakondwere,+ 18  kuti Yehova angaone ndipo zingamuipire m’maso mwake n’kuchotsa mkwiyo wake pamdani wakoyo.+ 19  Usamapse mtima chifukwa cha anthu ochita zoipa. Usamasirire anthu oipa,+ 20  pakuti aliyense woipa alibe tsogolo,+ ndipo nyale ya anthu oipa idzazimitsidwa.+ 21  Mwana wanga uziopa Yehova ndiponso mfumu.+ Usamakhale pagulu la anthu ofuna kuti zinthu zisinthe,+ 22  pakuti tsoka lawo lidzagwa mwadzidzidzi,+ ndipo ndani angadziwe za kufafanizika kwa anthu ofuna kuti zinthu zisinthe?+ 23  Mawu awanso akupita kwa anthu anzeru:+ Si bwino kukondera poweruza.+ 24  Munthu amene amauza woipa kuti: “Ndiwe wolungama,”+ anthu adzamutemberera, ndipo mitundu ya anthu idzamutsutsa. 25  Koma anthu omudzudzula zinthu zidzawayendera bwino,+ ndipo adzalandira madalitso a zinthu zabwino.+ 26  Woyankha mosapita m’mbali adzapsompsona milomo ya anthu.+ 27  Konzekera ntchito yako yapanja, ndipo konza munda wako.+ Ukatero ukamange banja lako. 28  Usakhale mboni yotsutsana ndi mnzako popanda umboni,+ chifukwa ukhoza kukhala wopusa ndi milomo yako.+ 29  Usanene kuti: “Ndim’chitira zimene iye anandichitira.+ Aliyense ndizim’bwezera mogwirizana ndi zimene anachita.”+ 30  Ndinadutsa pamunda pa munthu waulesi+ ndiponso pamunda wa mpesa wa munthu wopanda nzeru mumtima mwake.+ 31  Ndipo ndinaona kuti munali tchire lokhalokha.+ Zitsamba zoyabwa zinali paliponse m’mundamo komanso mpanda wake wamiyala unali utagumuka.+ 32  Choncho ine nditaona zimenezi, ndinayamba kuziganizira mumtima mwanga,+ ndipo ndinaphunzirapo* kuti:+ 33  Ukati, “Ndigoneko pang’ono, ndibeko katulo pang’ono, ndipindeko manja pang’ono pogona,”+ 34  umphawi wako ndithu udzabwera ngati wachifwamba ndipo kusauka kwako kudzabwera ngati munthu wokhala ndi zida.+

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa Miy 1:2.