Miyambo 19:1-29

19  Wosauka amene akuyenda ndi mtima wosagawanika ali bwino kuposa munthu wa milomo yopotoka,+ komanso munthu wopusa.+  Ndiponso, si bwino kuti munthu akhale wosadziwa zinthu,+ ndipo woyenda mofulumira ndi mapazi ake akuchimwa.+  Kupusa kwa munthu wochokera kufumbi n’kumene kumapotoza njira yake,+ choncho mtima wake umakwiyira Yehova.+  Chuma chimachulukitsa mabwenzi,+ koma munthu wonyozeka amalekanitsidwa ngakhale kwa bwenzi lake.+  Mboni yonama sidzalephera kulangidwa,+ ndipo wolankhula mabodza sadzapulumuka.+  Anthu amene amakhazika pansi mtima wa munthu wolemekezeka ndi ambiri,+ ndipo aliyense amakhala bwenzi la munthu wopereka mphatso.+  Abale ake onse a munthu wosauka amadana naye,+ komanso anzake amatalikirana naye kwambiri.+ Iye amafuna kuwachonderera, koma iwo amamuthawa.+  Munthu amene wapeza mtima wanzeru+ akukonda moyo wake. Wopitiriza kusonyeza kuzindikira amapeza zabwino.+  Mboni yonama sidzalephera kulangidwa,+ ndipo wolankhula mabodza adzawonongedwa.+ 10  Aliyense wopusa sayenera moyo wawofuwofu.+ Ndiye kuli bwanji kuti wantchito alamulire akalonga!+ 11  Kuzindikira kumachititsa munthu kubweza mkwiyo wake,+ ndipo kunyalanyaza cholakwa kumam’chititsa kukhala wokongola.+ 12  Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango wamphamvu,+ koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pazomera.+ 13  Mwana wopusa amabweretsa mavuto kwa bambo ake,+ ndipo mkazi wolongolola ali ngati denga* lodontha limene limathawitsa munthu.+ 14  Cholowa chochokera kwa makolo ndicho nyumba ndi chuma,+ koma mkazi wanzeru amachokera kwa Yehova.+ 15  Ulesi umachititsa tulo tofa nato,+ ndipo munthu waulesi amakhala ndi njala.+ 16  Wosunga lamulo akusunga moyo wake.+ Wosasamala za njira zake adzaphedwa.+ 17  Wokomera mtima munthu wonyozeka akukongoza Yehova,+ ndipo adzam’bwezera zimene anachitazo.+ 18  Langa mwana wako padakali chiyembekezo,+ ndipo usalakelake imfa yake.+ 19  Wamkwiyo waukulu ayenera kulipitsidwa,+ chifukwa ukam’pulumutsa, uzichita zimenezi kawirikawiri.+ 20  Mvera uphungu+ ndipo utsatire malangizo* kuti udzakhale wanzeru m’tsogolo.+ 21  Mumtima mwa munthu mumakhala zolinga zambiri,+ koma zolinga za Yehova n’zimene zidzakwaniritsidwe.+ 22  Chinthu chosiririka mwa munthu wochokera kufumbi ndicho kukoma mtima kwake kosatha,+ ndipo munthu wosauka ali bwino kuposa munthu wonama.+ 23  Kuopa Yehova kumapezetsa moyo.+ Munthu amagona mosatekeseka+ ndipo zoipa sizim’gwera.+ 24  Munthu waulesi amapisa dzanja lake m’mbale yodyera,+ koma n’kulephera kulibweretsa pakamwa.+ 25  Menya wonyoza+ kuti wosadziwa zinthu achenjere.+ Ndipo womvetsa zinthu uyenera kum’dzudzula kuti adziwe zinthu zowonjezereka.+ 26  Wochitira zoipa bambo ake ndiponso wothamangitsa mayi ake,+ ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.+ 27  Mwana wanga ukasiya kumvera malangizo, ndiye kuti wapatuka pa mawu okudziwitsa zinthu.+ 28  Mboni yopanda pake imanyoza chilungamo,+ ndipo pakamwa pa anthu oipa pamameza zinthu zopweteka ena.+ 29  Zilango anazikhazikitsira anthu onyoza,+ ndipo zikwapu anazisungira msana wa anthu opusa.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti “tsindwi.”
Onani mawu a m’munsi pa Miy 1:2.