Miyambo 16:1-33

16  Munthu ndiye amakonza maganizo mumtima mwake,+ koma kwa Yehova n’kumene kumachokera yankho la palilime lake.+  Njira zonse za munthu zimaoneka zoyera m’maganizo mwake,+ koma Yehova amafufuza zolinga zake.+  Pereka ntchito zako kwa Yehova,+ ndipo zolinga zako ndithu zidzakhazikika.+  Yehova anapanga chilichonse n’cholinga,+ ndipo ngakhale woipa anamusungira tsiku loipa.+  Yehova amanyansidwa ndi munthu aliyense wa mtima wonyada.+ Ngakhale anthu atagwirana manja, munthu sangapewe chilango.+  Cholakwa chimaphimbika ndi kukoma mtima kosatha ndiponso choonadi,+ ndipo chifukwa choopa Yehova munthu amapatuka pa choipa.+  Yehova akasangalala ndi njira za munthu,+ amachititsa ngakhale adani a munthuyo kukhala naye pa mtendere.+  Ndi bwino kukhala ndi zinthu zochepa mwachilungamo+ kuposa kukhala ndi zinthu zambiri koma mopanda chilungamo.+  Munthu angaganize za njira zake mumtima mwake,+ koma Yehova ndiye amawongolera mayendedwe ake.+ 10  Chigamulo chochokera kwa Mulungu chizikhala palilime la mfumu poweruza milandu.+ Pakamwa pake pazikhala pokhulupirika.+ 11  Muyezo wachilungamo ndiponso masikelo ndi za Yehova.+ Miyala yonse ya m’thumba loyezera kulemera kwa zinthu ndiyo ntchito zake.+ 12  Kuchita zinthu zoipa kumanyansa mafumu,+ chifukwa mpando wachifumu umakhazikika ndi chilungamo.+ 13  Milomo yolungama imasangalatsa mfumu yaikulu,+ ndipo mfumuyo imakonda munthu wolankhula zinthu zowongoka.+ 14  Mkwiyo wa mfumu umatanthauza amithenga a imfa,+ koma munthu wanzeru ndi amene amauziziritsa.+ 15  Nkhope ya mfumu ikawala, zimatanthauza moyo.+ Ndipo mafuno ake abwino ali ngati mtambo wa mvula yomalizira.+ 16  Kupeza nzeru n’kwabwino kwambiri kuposa kupeza golide.+ Ndipo ndi bwino kusankha kumvetsa zinthu kuposa siliva.+ 17  Kupewa zoipa ndiko njira ya anthu owongoka mtima.+ Munthu amene amateteza njira yake, amasunga moyo wake.+ 18  Kunyada kumafikitsa munthu ku chiwonongeko,+ ndipo mtima wodzikuza umachititsa munthu kupunthwa.+ 19  Kuli bwino kukhala wodzichepetsa limodzi ndi anthu ofatsa,+ kusiyana n’kugawana katundu wolanda ndi anthu odzikuza.+ 20  Munthu wosonyeza kuzindikira pa zinthu adzapeza zabwino,+ ndipo wodala ndi munthu amene amakhulupirira Yehova.+ 21  Munthu wanzeru mumtima mwake adzatchedwa wozindikira,+ ndipo munthu wolankhula zabwino amakopa ena ndi mawu a pakamwa pake.+ 22  Kuzindikira kumakhala ngati chitsime cha moyo kwa ozindikirawo,+ ndipo malangizo* a anthu opusa ndi uchitsiru.+ 23  Mtima wa munthu wanzeru umamuchititsa kuti asonyeze kuzindikira ndi pakamwa pake,+ ndipo umachititsa milomo yake kutulutsa mawu okopa.+ 24  Mawu okoma ali ngati chisa cha uchi.+ Amakhala okoma kwa munthu ndipo amachiritsa mafupa.+ 25  Pali njira yooneka ngati yowongoka kwa munthu,+ koma mapeto ake ndi imfa.+ 26  Munthu wakhama amadzigwirira yekha ntchito+ chifukwa chakuti pakamwa pake pamamukakamiza kwambiri.+ 27  Munthu wopanda pake amafukula zinthu zoipa,+ ndipo pakamwa pake pamakhala mawu okhala ngati makala amoto.+ 28  Kazitape amangokhalira kuyambitsa mikangano,+ ndipo wonenera anzake zoipa amalekanitsa mabwenzi apamtima.+ 29  Munthu wachiwawa amakopa mnzake,+ ndipo amam’chititsa kuti ayende m’njira yoipa.+ 30  Iye amatsinzinira ndi maso ake pokonza ziwembu.+ Amalumirira mano, ndipo amakwanitsadi kuchita chiwembu. 31  Imvi ndizo chisoti chachifumu cha ulemerero+ zikapezeka m’njira yachilungamo.+ 32  Munthu wosakwiya msanga ndi wabwino kuposa munthu wamphamvu,+ ndipo munthu wolamulira mtima wake amaposa munthu wogonjetsa mzinda.+ 33  Maere amaponyedwa pamwendo,+ koma zonse zimene maerewo amasonyeza zimachokera kwa Yehova.+

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa Miy 1:2.