Miyambo 11:1-31

11  Sikelo yachinyengo imam’nyansa Yehova,+ koma mwala woyezera, wolemera mokwanira, umam’sangalatsa.  Kodi kudzikweza kwafika? Ndiye kuti manyazinso afika.+ Koma nzeru zimakhala ndi anthu odzichepetsa.+  Mtima wosagawanika wa anthu owongoka ndi umene umawatsogolera,+ koma kupotoza zinthu kwa anthu ochita zachinyengo kudzawawononga.+  Zinthu zamtengo wapatali zidzakhala zopanda phindu pa tsiku la mkwiyo woopsa,+ koma chilungamo n’chimene chidzapulumutse munthu ku imfa.+  Kulungama kwa munthu wopanda cholakwa n’kumene kudzawongole njira yake,+ koma woipa adzagwera m’zoipa zakezo.+  Kulungama kwa anthu owongoka mtima n’kumene kudzawapulumutse,+ koma anthu ochita zinthu mwachinyengo adzagwidwa ndi zolakalaka zawo.+  Munthu woipa akafa, chiyembekezo chake chimawonongeka,+ ndipo zimene anali kuyembekezera kuchokera ku mphamvu zake sizichitika.+  Wolungama ndi amene amapulumutsidwa ku zowawa,+ ndipo woipa amalowa m’malo mwake.+  Wopanduka amawononga mnzake ndi pakamwa pake,+ koma anthu olungama amapulumutsidwa chifukwa chodziwa zinthu.+ 10  Mudzi umakondwera chifukwa cha makhalidwe abwino a anthu olungama,+ koma anthu oipa akawonongeka pamakhala mfuu yachisangalalo.+ 11  Mudzi umakwezedwa chifukwa cha madalitso a anthu olungama,+ koma umagwetsedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oipa.+ 12  Munthu wopanda nzeru mumtima mwake amanyoza mnzake,+ koma munthu wozindikira bwino ndi amene amakhala chete.+ 13  Amene amayendayenda n’kumanenera ena zoipa+ amaulula zinsinsi za anzake,+ koma wokhulupirika* amabisa nkhani.+ 14  Pakakhala popanda malangizo anzeru, anthu amagwa.+ Koma pakakhala aphungu ochuluka anthu amapulumuka.+ 15  Munthu amene walonjeza kuti adzapereka ngongole ya mlendo iye akadzalephera kubweza,+ zinthu sizidzamuyendera bwino. Koma wodana ndi kugwirana chanza pochita mgwirizano sakhala ndi nkhawa. 16  Mkazi wachikoka amapeza ulemu.+ Koma anthu ochitira nkhanza anzawo amapeza chuma. 17  Munthu wosonyeza kukoma mtima kosatha amapindulitsa moyo wake,+ koma munthu wankhanza amachititsa kuti thupi lake linyanyalidwe.+ 18  Munthu woipa amapeza malipiro achinyengo,+ koma wofesa chilungamo amapeza malipiro enieni.+ 19  Munthu wosasunthika pachilungamo adzapeza moyo,+ koma munthu wofunafuna zoipa adzafa.+ 20  Anthu a mtima wopotoka amam’nyansa Yehova,+ koma anthu opanda cholakwa m’njira yawo amam’sangalatsa.+ 21  Ngakhale dzanja ligwirane ndi dzanja linzake, munthu woipa sadzapewa chilango,+ koma ana a anthu olungama adzapulumuka ndithu.+ 22  Monga momwe chimakhalira chipini* chagolide pamphuno ya nkhumba, ndi mmenenso amakhalira mkazi wokongola koma wosaganiza bwino.+ 23  Zolakalaka za anthu olungama, ndithu n’zabwino.+ Chiyembekezo cha oipa chimabweretsa mkwiyo woopsa.+ 24  Pali amene amapatsa mowolowa manja, komabe zinthu zake zimawonjezeka.+ Palinso amene safuna kupatsa ena zinthu zoyenera kuwapatsa, koma amangokhala wosowa.+ 25  Munthu wopatsa mowolowa manja adzalandira mphoto,+ ndipo wothirira ena mosaumira nayenso adzathiriridwa mosaumira.+ 26  Wokana kugulitsa mbewu zake kwa anthu, anthuwo adzam’temberera. Koma wolola kuzigulitsa adzalandira madalitso.+ 27  Wofunafuna kuchitira ena zabwino, amafunafuna kuvomerezedwa ndi Mulungu.*+ Koma wofunafuna kuchita zoipa, zoipazo zidzam’bwerera.+ 28  Wodalira chuma chake adzagwa,+ koma anthu olungama adzasangalala ngati masamba a zomera.+ 29  Aliyense wochititsa nyumba yake kunyanyalidwa+ adzagwira mphepo,+ ndipo munthu wopusa adzakhala wantchito wa munthu wa mtima wanzeru. 30  Zipatso za munthu wolungama ndizo mtengo wa moyo,+ ndipo munthu wopulumutsa miyoyo ndi wanzeru.+ 31  Wolungamatu adzalandira mphoto yake padziko lapansi.+ Ndiye kuli bwanji woipa ndi wochimwa?+

Mawu a M'munsi

Mawu ake enieni, “wa mzimu wokhulupirika.”
“Chipini” ndi kachitsulo kapena kamtengo kokongoletsera kamene amakaika pabowo limene amaboola pamphuno.
Zingatanthauzenso kuvomerezedwa ndi anthu.