Machitidwe 16:1-40

16  Choncho Paulo anafika ku Debe ndiponso ku Lusitara.+ Kumeneko kunali wophunzira wina dzina lake Timoteyo,+ mwana wa mayi wachiyuda wokhulupirira, koma bambo ake anali Mgiriki.  Abale a ku Lusitara ndi ku Ikoniyo anamuchitira umboni wabwino.  Paulo anaonetsa kuti akufuna kumutenga pa ulendo wake. Chotero anamutenga ndi kum’dula+ chifukwa cha Ayuda amene anali kumeneko, pakuti onse anali kudziwa kuti bambo ake ndi Mgiriki.  Popitiriza ulendo wawo m’mizinda, anali kupatsa okhulupirira a kumeneko malamulo oyenera kuwatsatira, malinga ndi zimene atumwi ndi akulu ku Yerusalemu anagamula.+  Choncho mipingo inapitiriza kulimba m’chikhulupiriro+ ndipo chiwerengero chinapitiriza kuwonjezeka tsiku ndi tsiku.  Kenako iwo anapita ku Fulugiya ndiponso m’dziko la Galatiya,+ chifukwa mzimu woyera unawaletsa kulankhula mawu opatulika m’chigawo cha Asia.  Atafika ku Musiya anayesetsa kuti apite ku Bituniya,+ koma mzimu wa Yesu sunawalole.  Choncho analambalala Musiya ndi kukafika ku Torowa.+  Ndiyeno usiku Paulo anaona masomphenya.+ Munthu wina wa ku Makedoniya anaimirira ndi kumupempha kuti: “Wolokerani ku Makedoniya kuno mudzatithandize.” 10  Atangoona masomphenya amenewo, tinaganiza zopita ku Makedoniya.+ Tinali otsimikiza kuti Mulungu watiitana kuti tikalengeze uthenga wabwino kwa anthu akumeneko. 11  Chotero tinanyamuka ulendo wa panyanja kuchokera ku Torowa. Tinayenda molunjika mpaka ku Samatirake, koma tsiku lotsatira tinafika ku Neapoli. 12  Titachoka kumeneko tinafika ku Filipi,+ mzinda umene uli pansi pa ulamuliro wa Roma, umenenso ndi likulu la chigawo cha Makedoniya.+ Tinakhala mumzinda umenewu kwa masiku ndithu. 13  Tsiku la sabata tinatuluka pachipata n’kupita m’mbali mwa mtsinje, kumene tinali kuganiza kuti kuli malo opempherera. Ndiyeno tinakhala pansi ndi kuyamba kulankhula ndi amayi amene anali atasonkhana kumeneko. 14  Pamenepo panali mayi wina dzina lake Lidiya ndipo anali wolambira Mulungu. Iyeyu anali wochokera kumzinda wa Tiyatira+ ndipo anali wogulitsa nsalu ndi zovala zofiirira. Pamene anali kumvetsera, Yehova anatsegula kwambiri mtima wake+ kuti atchere khutu ku zimene Paulo anali kunena. 15  Tsopano iye ndi a m’banja lake atabatizidwa,+ anachonderera kuti: “Abale ngati inu mwaona kuti ndine wokhulupirika kwa Yehova, tiyeni mukalowe m’nyumba yanga ndi kukhala mmenemo.”+ Moti anatiumiriza ndithu kupita kwawo.+ 16  Ndiyeno pamene tinali kupita kumalo opempherera, tinakumana ndi mtsikana wina wantchito wogwidwa ndi mzimu,+ chiwanda cholosera zam’tsogolo.+ Iye anali kupezera mabwana ake phindu lochuluka+ mwa kumachita zoloserazo. 17  Mtsikana ameneyu anali kumangotsatira Paulo ndi ife n’kumafuula kuti:+ “Anthu awa ndi akapolo a Mulungu Wam’mwambamwamba, ndipo akulengeza njira ya chipulumutso kwa inu.” 18  Iye anakhala akuchita zimenezi kwa masiku ambiri. Potsirizira pake Paulo anatopa nazo+ ndipo anatembenuka n’kuuza mzimuwo kuti: “Ndikukulamula m’dzina la Yesu Khristu kuti utuluke mwa mtsikanayu.”+ Nthawi yomweyo mzimuwo unatuluka.+ 19  Koma mabwana ake aja ataona kuti chiyembekezo chawo chopeza phindu chatha,+ anagwira Paulo ndi Sila ndi kuwakokera mumsika, kubwalo la olamulira.+ 20  Atafika nawo kwa akuluakulu a boma, ananena kuti: “Anthu awa akusokoneza kwambiri+ mzinda wathu, chikhalirecho iwowa ndi Ayuda. 21  Ndipo akufalitsa miyambo+ imene kwa ife ndi yosaloleka kuitsatira kapena kuichita, popeza ndife Aroma.” 22  Pamenepo khamu la anthu linanyamuka pamodzi ndi kuukira atumwiwo. Ndipo akuluakulu a boma aja, anavula atumwiwo malaya awo akunja mochita kuwang’ambira ndi kulamula kuti awakwapule ndi zikoti.+ 23  Atawakwapula zikoti zambiri,+ anawaponya m’ndende ndi kulamula woyang’anira ndende kuti awasunge mosamala kwambiri.+ 24  Popeza kuti anamulamula zimenezi, iye anawaponya m’chipinda chamkati cha ndendeyo+ ndi kumanga mapazi awo m’matangadza.+ 25  Koma chapakati pa usiku,+ Paulo ndi Sila anali kupemphera ndi kutamanda Mulungu poimba nyimbo,+ ndipo akaidi ena anali kuwamva. 26  Mwadzidzidzi panachitika chivomezi champhamvu, mpaka maziko a ndendeyo anagwedezeka. Nthawi yomweyo zitseko zonse zinatseguka, ndipo onse maunyolo awo anamasuka.+ 27  Woyang’anira ndende uja atadzuka ku tulo take ndi kuona kuti zitseko za ndende n’zotseguka, anasolola lupanga lake kuti adziphe,+ poganiza kuti akaidiwo athawa.+ 28  Pomwepo Paulo anafuula mokweza kuti: “Usadzivulaze,+ tonse tilipo!” 29  Pamenepo anapempha kuti amupatse nyale ndipo analumphira mkatimo. Akunjenjemera ndi mantha, anagwada+ pamaso pa Paulo ndi Sila. 30  Kenako anawatulutsa kunja n’kunena kuti: “Mabwana inu, ndichite chiyani+ kuti ndipulumuke?” 31  Iwo anati: “Khulupirira mwa Ambuye Yesu ndipo udzapulumuka,+ limodzi ndi a m’nyumba yako.”+ 32  Ndipo analankhula mawu a Yehova kwa iye pamodzi ndi onse a m’nyumba yake.+ 33  Mu ola lomwelo la usiku, anawatenga ndi kuwatsuka zilonda zawo. Ndipo onse, iye ndi a m’banja lake, anabatizidwa+ mosataya nthawi. 34  Kenako anapita nawo kunyumba kwake ndi kuwaikira chakudya patebulo. Ndipo iye limodzi ndi onse a m’banja lake, anakondwera kwambiri chifukwa anakhulupirira Mulungu. 35  M’mawa mwake, akuluakulu a boma+ anatumiza asilikali kukanena kuti: “Amuna amenewo amasuleni.” 36  Choncho woyang’anira ndende uja anauza Paulo uthengawo, kuti: “Akuluakulu a boma atumiza anthu kudzanena kuti awirinu mumasulidwe. Choncho tulukani tsopano, ndipo mupite mu mtendere.” 37  Koma Paulo anawauza kuti: “Iwo atikwapula pamaso pa anthu ndi kutiponya m’ndende popanda kuzenga mlandu wathu, chikhalirecho ndife Aroma.+ Kodi tsopano akutitulutsa mseri? Ayi, zimenezo sizitheka! Abwere eniakewo adzatitulutse okha.” 38  Choncho asilikaliwo anauza akuluakulu a boma aja mawu amenewa. Pamenepo akuluakulu a bomawo anachita mantha atamva kuti anthuwo ndi Aroma.+ 39  Chotero anabwera ndi kuwachonderera, ndipo atawatulutsa anawapempha kuti achoke mumzindawo. 40  Koma iwo anatuluka m’ndendemo n’kupita kunyumba kwa Lidiya. Ataona abale, anawalimbikitsa+ kenako ananyamuka n’kumapita.

Mawu a M'munsi