Luka 20:1-47

20  Tsiku lina pamene anali kuphunzitsa anthu m’kachisi ndi kulengeza uthenga wabwino, panafika ansembe aakulu, alembi pamodzi ndi akulu.+  Iwo anamufunsa kuti: “Tiuzeni, kodi muli ndi ulamuliro wochitira zinthu zimenezi? Kapena ndani amene anakupatsani ulamuliro umenewu?”+  Poyankha Yesu anawauza kuti: “Inenso ndikufunsani funso limodzi, ndipo mundiyankhe:+  Kodi ubatizo wa Yohane unali wochokera kumwamba kapena kwa anthu?”+  Pamenepo iwo anayamba kukambirana okhaokha kuti: “Tikanena kuti, ‘Unachokera kumwamba,’ iye anena kuti, ‘Nanga n’chifukwa chiyani simunamukhulupirire?’+  Koma tikanena kuti, ‘Unachokera kwa anthu,’ anthu onsewa atiponya miyala,+ chifukwa iwo akukhulupirira ndi mtima wonse kuti Yohane+ anali mneneri.”+  Choncho anayankha kuti sakudziwa kumene unachokera.  Pamenepo Yesu anawauza kuti: “Inenso sindikuuzani ulamuliro umene ndimachitira zimenezi.”+  Ndiyeno iye anayamba kuuza anthuwo fanizo ili: “Munthu wina analima munda wa mpesa,+ ndipo anasiya mundawo m’manja mwa alimi n’kupita kudziko lina kumene anakhalako nthawi yaitali ndithu.+ 10  Koma nyengo ya zipatso itakwana anatumiza kapolo+ wake kwa alimiwo,+ kuti akamupatseko zina mwa zipatso za m’munda wa mpesawo.+ Komano alimiwo anamumenya ndi kumubweza chimanjamanja.+ 11  Koma iye anawatumiziranso kapolo wina. Ameneyonso anamumenya ndi kumuchitira chipongwe, ndipo anamubweza chimanjamanja.+ 12  Anatumizanso wachitatu.+ Uyunso anamuvulaza ndi kumuponya kunja. 13  Zitatero mwini munda wa mpesa uja anati, ‘Ndichite chiyani tsopano? Chabwino, nditumiza mwana wanga wokondedwa.+ Mwana wanga yekhayu ayenera kuti akamulemekeza ndithu.’ 14  Alimiwo atamuona anayamba kukambirana kuti, ‘Eya, uyu ndiye wolandira cholowa. Tiyeni timuphe kuti cholowacho chikhale chathu.’+ 15  Atatero anamutulutsa+ m’munda wa mpesawo ndi kumupha.+ Pamenepa, kodi mwini munda wa mpesa uja adzachita chiyani kwa alimiwo?+ 16  Adzabwera ndi kupha alimiwo ndipo munda wa mpesawo adzaupereka kwa ena.”+ Atamva zimenezi iwo anati: “Ayi zisatero ndithu!” 17  Koma iye anawayang’ana ndi kunena kuti: “Pajatu malemba amati, ‘Mwala umene omanga nyumba anaukana,+ umenewu wakhala mwala wapakona wofunika kwambiri.’+ Kodi mawu amenewa amatanthauza chiyani? 18  Aliyense wogwera pamwala umenewo adzaphwanyika.+ Ndipo aliyense amene mwalawo udzamugwere,+ udzam’pereratu.”+ 19  Tsopano alembi ndi ansembe aakulu aja, pozindikira kuti iye anali kunena za iwo mufanizolo, anayesetsa kupeza mpata kuti amugwire ola lomwelo, koma anaopa anthu.+ 20  Ndiyeno ataonetsetsa zochita zake, anatuma aganyu mwachinsinsi kuti akadzionetse ngati olungama, n’cholinga choti akamukole+ m’mawu ake, kuti akamupereke ku boma ndi kwa bwanamkubwa.+ 21  Choncho iwo anamufunsa kuti: “Mphunzitsi, tikudziwa kuti mumanena ndi kuphunzitsa molondola ndipo mulibe tsankho, koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu mogwirizana ndi choonadi.+ 22  Kodi n’kololeka kuti ife tizipereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi?”+ 23  Koma Yesu anazindikira ndale zawo ndipo anawauza kuti:+ 24  “Ndionetseni khobidi la dinari. Kodi nkhope ndi mawu ali pamenepo n’zandani?” Iwo anayankha kuti: “Ndi za Kaisara.”+ 25  Iye anawauza kuti: “Chotero perekani zinthu za Kaisara kwa Kaisara,+ koma za Mulungu kwa Mulungu.”+ 26  Pamenepo iwo analephera kumutapa m’kamwa pa zimene ananenazi pamaso pa anthu, mwakuti pothedwa nzeru ndi yankho lake, anangokhala chete kusowa chonena.+ 27  Koma Asaduki ena, amene amanena kuti kulibe kuuka kwa akufa anafika+ ndi kuyamba kumufunsa, 28  kuti: “Mphunzitsi, Mose+ anatilembera kuti, ‘Ngati munthu wamwalira n’kusiya mkazi amene sanabereke naye ana, m’bale wake+ atenge mkazi wamasiyeyo ndi kuberekera m’bale wake uja ana mwa mkaziyo.’+ 29  Ndiyeno panali amuna 7 apachibale. Woyamba anatenga mkazi, koma anamwalira wopanda mwana.+ 30  Wachiwirinso chimodzimodzi. 31  Kenako wachitatu anamutenga. Zinachitika chimodzimodzi kwa amuna onse 7 aja: onse anamwalira osasiya ana.+ 32  Pa mapeto pake mkazi uja nayenso anamwalira.+ 33  Kodi pamenepa, pouka kwa akufa, mkazi ameneyu adzakhala wa ndani popeza onse 7 anamukwatira?”+ 34  Yesu anawayankha kuti: “Ana a m’nthawi* ino amakwatira+ ndi kukwatiwa. 35  Koma amene ayesedwa oyenerera+ kudzapeza moyo pa nthawi* imeneyo+ ndi kudzaukitsidwa kwa akufa+ sadzakwatira kapena kukwatiwa. 36  Ndiponso iwo sadzafanso,+ chifukwa adzakhala ngati angelo. Iwo adzakhalanso ana a Mulungu mwa kukhala ana a kuuka kwa akufa.+ 37  Koma zakuti akufa amaukitsidwa ngakhalenso Mose anafotokoza m’nkhani ya chitsamba cha minga.+ M’nkhani imeneyo iye ananena kuti Yehova ndi ‘Mulungu wa Abulahamu, Mulungu wa Isaki ndi Mulungu wa Yakobo.’+ 38  Iye ndi Mulungu wa anthu amoyo, osati akufa, pakuti kwa iye onsewa ndi amoyo.”+ 39  Poyankha ena mwa alembiwo anati: “Mphunzitsi, mwanena bwino.” 40  Ananena zimenezi chifukwa sanathenso kulimba mtima kuti amufunse funso lina ngakhale limodzi. 41  Ndiyeno iye anawafunsa kuti: “N’chifukwa chiyani amanena kuti Khristu ndi mwana wa Davide?+ 42  Pakuti Davide mwiniyo ananena m’buku la Masalimo kuti, ‘Yehova anauza Ambuye wanga kuti: “Khala kudzanja langa lamanja 43  kufikira nditaika adani ako monga chopondapo mapazi ako.”’+ 44  Chotero Davide anamutcha ‘Ambuye.’ Nanga akukhala bwanji mwana wake?” 45  Kenako, anthu onse akumvetsera, iye anauza ophunzirawo kuti:+ 46  “Chenjerani ndi alembi. Iwo amakonda kuyendayenda atavala mikanjo. Amakonda kupatsidwa moni m’misika ndi kukhala m’mipando yakutsogolo m’masunagoge. Amakondanso malo olemekezeka kwambiri pa chakudya chamadzulo.+ 47  Iwo ndi amene amadyerera nyumba za akazi amasiye,+ ndipo mwachiphamaso amapereka mapemphero ataliatali. Anthu amenewa adzalandira chiweruzo champhamvu.”+

Mawu a M'munsi

Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.