Luka 18:1-43

18  Ndiyeno Yesu anawauza fanizo pofuna kuwasonyeza kufunika koti azipemphera nthawi zonse, osaleka.+  Iye anati: “Mumzinda winawake munali woweruza wina amene anali wosaopa Mulungu ndiponso wosasamala za munthu.  Koma mumzindawo munali mkazi wina wamasiye ndipo anali kupitapita+ kwa woweruza uja kukamupempha kuti, ‘Ndiweruzireni mlandu wanga ndi munthu amene akutsutsana nane, kuti pachitike chilungamo.’  Kwa kanthawi ndithu woweruzayo sankafuna, koma pambuyo pake ananena mumtima mwake kuti, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kusamala za munthu,  ndionetsetsa kuti chilungamo chachitika kwa mkazi wamasiyeyu. Ndichita zimenezi kuti asapitirize kumangobwera ndi kundisautsa kwambiri,+ chifukwa mkazi ameneyu akundivutitsa+ mosalekeza.’”  Kenako Ambuye anati: “Mwamvatu zimene woweruzayo ananena ngakhale kuti anali wosalungama!  Ndithu, ngakhale kuti Mulungu amalezera mtima+ osankhidwa ake, kodi sadzaonetsetsa kuti chilungamo+ chachitika kwa iwo, amene amafuulira kwa iye usana ndi usiku?  Ndithu ndikukuuzani, Iye adzaonetsetsa kuti chilungamo chachitika kwa iwo mwamsanga.+ Koma, Mwana wa munthu akadzafika, kodi adzapezadi chikhulupiriro padziko lapansi?”  Yesu ananenanso fanizo lotsatirali kwa ena odzidalira, odziona ngati olungama+ amenenso amaona ena onse ngati opanda pake.+ Iye anati: 10  “Anthu awiri anapita m’kachisi kukapemphera. Mmodzi anali Mfarisi, winayo anali wokhometsa msonkho. 11  Mfarisi uja anaimirira+ ndi kuyamba kupemphera+ mumtima mwake. Iye anati, ‘Mulungu wanga, ndikukuyamikani chifukwa ine sindili ngati anthu enawa ayi. Iwo ndi olanda, osalungama ndi achigololo. Sindilinso ngati wokhometsa msonkho uyu.+ 12  Ine ndimasala kudya kawiri pa mlungu ndipo ndimapereka chakhumi pa zinthu zonse zimene ndimapeza.’+ 13  Koma wokhometsa msonkho uja, ataima chapatali ndithu, sanafune ngakhale kukweza maso ake kumwamba. Anali kungodziguguda pachifuwa+ ndi kunena kuti, ‘Mulungu wanga, ndikomereni mtima munthu wochimwa ine.’+ 14  Ndithu ndikukuuzani, Munthu ameneyu anapita kwawo ataonedwa kukhala wolungama kwambiri+ kusiyana ndi wina uja, chifukwa aliyense wodzikweza adzam’nyazitsa, koma wodzichepetsa adzamukweza.”+ 15  Pamenepo anthu anayamba kumubweretsera ana kuti awakhudze ndi manja ake, koma ophunzirawo ataona zimenezo anayamba kuwakalipira.+ 16  Komabe Yesu anaitana anawo. Iye anati: “Alekeni anawo abwere kwa ine, musawaletse ayi. Pakuti ufumu wa Mulungu ndi wa anthu amene ali ngati ana amenewa.+ 17  Ndithu ndikukuuzani, Aliyense wosalandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamng’ono sadzalowa n’komwe mu ufumuwo.”+ 18  Tsopano wolamulira wina anamufunsa kuti: “Mphunzitsi Wabwino, ndizichita chiyani kuti ndikapeze moyo wosatha?”+ 19  Yesu anamufunsa kuti: “N’chifukwa chiyani ukunditchula kuti wabwino? Palibe wabwino, koma Mulungu yekha.+ 20  Iwe umadziwa malamulo+ akuti, ‘Usachite chigololo,+ Usaphe munthu,*+ Usabe,+ Usapereke umboni wonama+ ndiponso lakuti, Uzilemekeza bambo ako ndi mayi ako.’”+ 21  Pamenepo iye anati: “Zonsezi ndakhala ndikuzitsatira kuyambira ndili wamng’ono.”+ 22  Atamva zimenezo, Yesu anamuuza kuti: “Pali chinthu chimodzi chimene chikusowekabe mwa iwe: Kagulitse zinthu zonse zimene uli nazo n’kugawa ndalamazo kwa anthu osauka. Ukatero udzakhala ndi chuma kumwamba, ndiyeno ubwere udzakhale wotsatira wanga.”+ 23  Iye atamva zimenezi, anamva chisoni kwambiri, chifukwa anali wolemera kwabasi.+ 24  Yesu anamuyang’ana n’kunena kuti: “Zidzakhalatu zovuta kwambiri kuti anthu a ndalama adzalowe mu ufumu wa Mulungu!+ 25  Kunena zoona, n’chapafupi kuti ngamila ilowe padiso la singano kusiyana n’kuti munthu wolemera alowe mu ufumu wa Mulungu.”+ 26  Amene anamva zimenezi anati: “Ndiye angapulumuke ndani?” 27  Iye anawauza kuti: “Zinthu zosatheka ndi anthu n’zotheka ndi Mulungu.”+ 28  Koma Petulo ananena kuti: “Taonani! Ife tasiya zinthu zathu ndi kukutsatirani.”+ 29  Yesu anawauza kuti: “Ndithu ndikukuuzani, Palibe amene wasiya nyumba, mkazi, abale, makolo kapena ana, chifukwa cha ufumu wa Mulungu+ 30  amene sadzapeza zochuluka kwambiri kuposa zimenezi m’nthawi ino, ndipo m’nthawi* ikubwerayo moyo wosatha.”+ 31  Kenako anatengera pambali ophunzira 12 aja ndi kuwauza kuti: “Tamverani! Tsopano tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zinalembedwa ndi aneneri,+ zokhudza Mwana wa munthu zikakwaniritsidwa.+ 32  Mwachitsanzo, akamupereka kwa anthu a mitundu ina ndipo akamuseka,+ kum’chitira chipongwe+ ndi kumulavulira.+ 33  Akakamaliza kumukwapula+ akamupha,+ koma tsiku lachitatu iye adzauka.”+ 34  Koma iwo sanamvetse tanthauzo la chilichonse cha zimenezi. Mawu amenewa anabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe zimene zinanenedwazo.+ 35  Tsopano pamene anali kuyandikira ku Yeriko, munthu wina wakhungu anakhala pansi m’mphepete mwa msewu n’kumapemphapempha.+ 36  Atamva khamu la anthu likudutsa chapomwepo, anafunsa chimene chinali kuchitika. 37  Iwo anamuuza kuti: “Yesu Mnazareti akudutsa!”+ 38  Atamva zimenezo anafuula kuti: “Yesu, Mwana wa Davide, ndichitireni chifundo!”+ 39  Ndiyeno amene anali patsogolo anayamba kumudzudzula mwamphamvu kuti akhale chete. Koma m’pamenenso iye anafuula kwambiri kuti: “Mwana wa Davide, ndichitireni chifundo.”+ 40  Choncho Yesu anaima ndi kulamula kuti munthuyo apite naye kwa iye.+ Atafika pafupi, Yesu anamufunsa kuti: 41  “Ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?”+ Iye anayankha kuti: “Ambuye, ndithandizeni kuti ndiyambe kuona.”+ 42  Choncho Yesu anamuuza kuti: “Yamba kuona, chikhulupiriro chako chakuchiritsa.”+ 43  Nthawi yomweyo anayamba kuona,+ ndipo anayamba kumutsatira akulemekeza Mulungu.+ Komanso anthu onse, ataona zimenezi, anatamanda Mulungu.

Mawu a M'munsi

Kupha uku ndi kupha munthu mwachiwembu osati mwalamulo.
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.