Luka 11:1-54

11  Tsopano Yesu anali kupemphera pamalo enaake. Atatsiriza, mmodzi wa ophunzira ake anamuuza kuti: “Ambuye, tiphunzitseni kupemphera,+ ngati mmene Yohane anaphunzitsira ophunzira ake.”+  Pamenepo iye anawauza kuti: “Mukamapemphera+ muzinena kuti, ‘Atate, dzina lanu liyeretsedwe.+ Ufumu wanu ubwere.+  Mutipatse chakudya+ chathu chalero malinga ndi chakudya chofunika pa tsikuli.  Ndipo mutikhululukire machimo athu,+ pakuti nafenso timakhululukira aliyense amene amatilakwira.*+ Komanso musatilowetse m’mayesero.’”+  Kenako anawauza kuti: “Ndani wa inu amene ali ndi bwenzi lake kumene angapite pakati pa usiku kukam’pempha kuti, ‘Bwanawe, ndibwerekeko mitanda itatu ya mkate,  chifukwa mnzanga wangofika kumene kuchokera ku ulendo ndipo ndilibe chomupatsa’?  Ndiyeno ali m’nyumbayo n’kuyankha kuti, ‘Usandivutitse ine.+ Takhoma kale chitseko, ndipo ine ndi ana anga tagona kale. Sindingadzukenso kuti ndikupatse kanthu.’  Ndithu ndikukuuzani, Adzadzuka ndi kum’patsa zonse zimene akufuna, osati chifukwa chakuti ndi bwenzi lake, koma chifukwa cha kukakamira kwake.+  Choncho ndikukuuzani, Pemphanibe,+ ndipo adzakupatsani. Pitirizani kufunafuna,+ ndipo mudzapeza. Gogodanibe, ndipo adzakutsegulirani. 10  Pakuti aliyense wopempha amalandira,+ aliyense wofunafuna amapeza, ndipo aliyense wogogoda adzam’tsegulira. 11  Kodi kapena pakati panu alipo bambo amene mwana wake+ atam’pempha nsomba, angam’patse njoka m’malo mwa nsomba? 12  Kapena atam’pempha dzira iye angam’patse chinkhanira? 13  Choncho ngati inu, ngakhale kuti ndinu oipa, mumadziwa kupatsa ana anu+ mphatso zabwino, kuli bwanji Atate wakumwamba! Ndithudi iye adzapereka mowolowa manja mzimu woyera+ kwa amene akum’pempha.” 14  Nthawi inayake anali kutulutsa chiwanda cholepheretsa munthu kulankhula.+ Chiwandacho chitatuluka, munthu wosalankhulayo analankhula, ndipo khamu la anthu linadabwa kwambiri. 15  Koma ena mwa iwo anati: “Ameneyu amatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebule* wolamulira wa ziwanda.”+ 16  Koma ena pofuna kumuyesa, anayamba kumupempha kuti awasonyeze chizindikiro+ chochokera kumwamba. 17  Podziwa maganizo awo,+ iye anawauza kuti: “Ufumu uliwonse wogawanika umatha, ndipo nyumba yogawanika imagwa.+ 18  Choncho ngati Satana wagawanika, ufumu wake ungalimbe bwanji?+ Chifukwa inu mukuti ndikutulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebule. 19  Ngati ndikutulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebule, kodi otsatira anu+ akuzitulutsa ndi chiyani? Pa chifukwa chimenechi iwo adzakuweruzani. 20  Koma ngati ziwandazo ndikuzitulutsa ndi chala cha Mulungu,+ ndiye kuti ufumu wa Mulungu wakufikiranidi modzidzimutsa.+ 21  Munthu wamphamvu,+ wokhala ndi zida zokwanira, akamalondera nyumba yake, chuma chake chimatetezeka. 22  Koma wina wamphamvu kuposa iyeyu+ akabwera n’kumugonjetsa,+ amamulanda zida zake zonse zimene amadalira, ndipo katundu amene wamulanda, amamugawa kwa ena. 23  Amene sali kumbali yanga akutsutsana ndi ine, ndipo amene sasonkhanitsa anthu pamodzi ndi ine amawabalalitsa.+ 24  “Mzimu wonyansa ukatuluka mwa munthu, umadutsa m’malo ouma kufunafuna malo okhala, koma akapanda kupezeka, umanena kuti, ‘Ndibwerera m’nyumba yanga mmene ndinatuluka muja.’+ 25  Tsopano ukafikamo umapeza muli mosesa bwino komanso mokongola. 26  Kenako umapita kukatenga mizimu ina 7+ yoipa kwambiri kuposa umenewu, ndipo ikalowa mkatimo, imakhala mmenemo. Potsirizira pake zochita za munthu ameneyu zimakhala zoipa kwambiri kuposa poyamba paja.”+ 27  Pamene anali kunena mawu amenewa, mayi wina m’khamu la anthulo anafuula n’kumuuza kuti: “Ndi wodala mayi+ amene mimba yake inanyamula inu ndiponso amene munayamwa mabere ake!” 28  Koma iye anati: “Ayi, m’malomwake, Odala ndi amene akumva mawu a Mulungu ndi kuwasunga!”+ 29  Pamene anthu osonkhana pamodzi anali kuchulukirachulukira, iye anayamba kunena kuti: “M’badwo uwu ndi m’badwo woipa, ukufuna chizindikiro.+ Koma sudzapatsidwa chizindikiro chilichonse kupatulapo chizindikiro cha Yona chokha.+ 30  Monga momwe Yona+ anakhalira chizindikiro kwa anthu a ku Nineve, Mwana wa munthu adzakhalanso chizindikiro ku m’badwo uwu. 31  Mfumukazi+ ya kum’mwera adzaiimiritsa pa chiweruzo limodzi ndi anthu a m’badwo uwu, ndipo idzawatsutsa. Chifukwa mfumukazi imeneyi inabwera kuchokera kumalekezero a dziko lapansi kudzamva nzeru za Solomo. Koma tsopano wina woposa+ Solomo ali pano. 32  Anthu a ku Nineve adzaimirira pa chiweruzo limodzi ndi m’badwo uwu ndipo adzautsutsa. Chifukwa iwo analapa atamva ulaliki wa Yona.+ Koma tsopano wina woposa+ Yona ali pano. 33  Munthu akayatsa nyale saiika m’chipinda cha pansi kapena kuivundikira ndi dengu, koma amaiika pachoikapo nyale,+ kuti onse olowa aone kuwala. 34  Nyale ya thupi ndi diso lako. Ngati diso lako lili lolunjika pa chinthu chimodzi, thupi lako lonse limawala kwambiri.+ Koma ngati lili loipa, thupi lako limachita mdima. 35  Chotero khala tcheru. Mwina kuwala kumene kuli mwa iwe ndiko mdima.+ 36  Choncho ngati thupi lako lonse lili lowala kwambiri, popanda mbali ina yamdima, thupi lonse lidzawala kwambiri+ ngati mmene nyale imachitira pokuunikira ndi kuwala kwake.” 37  Atalankhula zimenezi, Mfarisi wina anam’pempha kuti akadye naye.+ Choncho iye anapitadi kukadya chakudya. 38  Koma Mfarisiyo anadabwa kuona kuti anayamba kudya chakudyacho asanasambe.+ 39  Choncho Ambuye anamuuza kuti: “Inu Afarisi mumayeretsa kunja kwa kapu ndi mbale, koma mkati+ mwanu mwadzaza maganizo ofuna kulanda zinthu za anthu ndi kuchita zinthu zoipa.+ 40  Anthu opanda nzeru inu! Amene anapanga kunja+ anapanganso mkati, si choncho kodi? 41  Koma inu, perekani zimene zili mkati monga mphatso zachifundo,+ mukatero zina zonse zokhudza inuyo zidzakhala zoyera. 42  Tsoka inu Afarisi, chifukwa mumapereka chakhumi+ cha timbewu ta minti ndi ta luwe, ndi cha mbewu zakudimba zamtundu uliwonse. Koma mumanyalanyaza chilungamo ndi chikondi cha Mulungu! Unalidi udindo wanu kuchita zinthu zimenezi, koma simunayenera kusiya zinazo.+ 43  Tsoka inu Afarisi, chifukwa mumakonda mipando yakutsogolo m’masunagoge ndi kupatsidwa moni m’misika!+ 44  Tsoka inu, chifukwa muli ngati manda achikumbutso osaonekera, moti anthu amayenda pamwamba pake koma osadziwa!”+ 45  Poyankha wina wodziwa+ Chilamulo anamuuza kuti: “Mphunzitsi, izi mukunenazi mukunyoza ndi ife tomwe.” 46  Pamenepo iye anati: “Tsoka inunso odziwa Chilamulo, chifukwa mumasenzetsa anthu katundu wovuta kunyamula, koma inuyo simukhudza katunduyo ngakhale ndi chala chokha!+ 47  “Tsoka inu, chifukwa mumamanga manda achikumbutso a aneneri, komatu makolo anu ndi amene anawapha!+ 48  Mosakayikira, ndinu mboni pa zimene makolo anu anachita. Ndipo mukugwirizana+ nawonso, chifukwa iwo anapha+ aneneri, pamene inu mukumanga manda awo. 49  Pa nkhani imeneyi, nzeru+ ya Mulungu inanenanso kuti, ‘Ndidzawatumizira aneneri ndi atumwi, koma iwo adzapha ndi kuzunza ena mwa iwo. 50  N’chifukwa chake m’badwo uwu udzafunsidwa za magazi a aneneri,+ okhetsedwa kuchokera pamene dziko linakhazikika.+ 51  Kuyambira magazi a Abele+ mpaka magazi a Zekariya,+ amene anaphedwa pakati pa guwa lansembe ndi nyumba yopatulika.’+ Inde, ndikukuuzani, m’badwo uwu udzafunsidwa za magazi amenewo. 52  “Tsoka inu odziwa Chilamulo, chifukwa munalanda anthu kiyi yowathandiza kudziwa zinthu.+ Inuyo simunalowemo, ndipo ofuna kulowamo munawatsekereza!”+ 53  Choncho atachoka kumeneko, alembi ndi Afarisi anayamba kumuunjirira koopsa ndi kum’panikiza ndi mafunso okhudza zinthu zina. 54  Anali kuyembekezera+ kumva mawu oti amutape nawo m’kamwa.+

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa Mt 6:12.
“Belezebule” ndi dzina lina la Satana.