Ezekieli 15:1-8

15  Yehova anapitiriza kulankhula nane kuti:  “Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wa mpesa+ umasiyana bwanji ndi mitengo ina yonse? Kodi kamtengo kophuka pambali pa mtengowo pakati pa mitengo ya m’nkhalango kamasiyana bwanji ndi mitengo ina?  Kodi anthu amadula nthambi yake kuti ikhale mtengo wogwiritsira ntchito inayake? Kapena kodi amatengapo kamtengo koti akhome pakhoma kuti azikolowekapo ziwiya zosiyanasiyana?  Mtengowotu umangoikidwa pamoto basi kuti ukhale nkhuni.+ Motowo umanyeketsa kutsinde ndi kunsonga kwake. Pakati pa mtengowo pamapsanso.+ Choncho kodi mtengowo ungagwire ntchito ina iliyonse?  Mtengowo ukakhala wathunthu saugwiritsa ntchito iliyonse. Ndiye kuli bwanji ukapsa ndi moto n’kunyeka? Kodi ungagwirenso ntchito iliyonse?”+  “Chotero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti, ‘Mofanana ndi mtengo wa mpesa umene uli pakati pa nkhalango, umene ndaupereka kuti uzikhala nkhuni pamoto, ndaperekanso anthu okhala mu Yerusalemu.+  Anthuwo ndawayang’ana mokwiya.+ Iwo achoka pamoto, koma motowo uwanyeketsa.+ Anthu inu mudzadziwa kuti ine ndine Yehova, ndikadzawayang’ana mokwiya.’”+  “‘Dziko lawo ndidzalisandutsa bwinja lokhalokha+ chifukwa chakuti iwo achita zosakhulupirika,’+ watero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.”

Mawu a M'munsi