Ekisodo 37:1-29

37  Tsopano Bezaleli+ anapanga Likasa+ la mtengo wa mthethe, mikono iwiri ndi hafu m’litali, mkono umodzi ndi hafu m’lifupi, ndi mkono umodzi ndi hafu msinkhu wake.+  Kenako analikuta ndi golide woyenga bwino mkati ndi kunja komwe, ndipo anapanga mkombero wagolide kuzungulira Likasalo.+  Ndiyeno analipangira mphete zinayi zagolide zoika pamwamba pa miyendo yake inayi. Mphete ziwiri zinali mbali imodzi, ndipo mphete zina ziwiri zinali mbali inayo.+  Anapanganso mitengo yonyamulira ya mtengo wa mthethe ndipo anaikuta ndi golide.+  Mitengo yonyamulirayo anailowetsa m’mphete zam’mbali mwa Likasa zija kuti azinyamulira Likasalo.+  Kenako anapanga chivundikiro+ chagolide woyenga bwino, mikono iwiri ndi hafu m’litali, ndi mkono umodzi ndi hafu m’lifupi.+  Anapanganso akerubi awiri agolide. Anali osula ndipo anawapanga kumapeto onse awiri a chivundikirocho.+  Kerubi mmodzi anali kumbali imodzi ya chivundikirocho ndipo kerubi wina kumbali inayo. Akerubiwo anawapanga kumbali zonse ziwiri za chivundikirocho.+  Mapiko a akerubiwo anali okweza m’mwamba ndi otambasula.+ Iwo anaphimba chivundikirocho ndi mapiko awo, ndipo anakhala moyang’anizana, koma nkhope zawo zinayang’ana pachivundikirocho.+ 10  Ndiyeno anapanga tebulo la mtengo wa mthethe,+ mikono iwiri m’litali, mkono umodzi m’lifupi ndi mkono umodzi ndi hafu msinkhu wake.+ 11  Analikuta ndi golide woyenga bwino, ndipo anapanga mkombero wagolide kuzungulira tebulo lonselo.+ 12  Analipangiranso felemu, muyezo wake chikhatho* chimodzi m’lifupi mwake. Felemuli linazungulira tebulo lonse ndipo anapanga mkombero wagolide pafelemulo.+ 13  Kuwonjezera pamenepo, analipangira mphete zinayi zagolide ndi kuziika m’makona ake anayi, mmene munali miyendo yake inayi.+ 14  Mphetezo zinali pafupi ndi felemu lija kuti muzilowa mitengo yonyamulira tebulolo.+ 15  Ndiyeno anapanga mitengo yonyamulira ya mtengo wa mthethe ndi kuikuta ndi golide. Mitengo imeneyi inali yonyamulira tebulolo.+ 16  Atatero anapanga ziwiya za patebulolo, mbale zake, zikho zake, mitsuko yake ndi mbale zake zolowa zoti azithirira nsembe zachakumwa. Anazipanga ndi golide woyenga bwino.+ 17  Kenako anapanga choikapo nyale+ chagolide woyenga bwino. Chimenechi chinali chosula. Choikapo nyalechi chinali ndi nthambi m’mbali mwake, ndiponso chinali ndi masamba ofunga duwa, mfundo ndi maluwa.+ 18  Choikapo nyalechi chinali ndi nthambi 6. Kumbali ina kunatuluka nthambi zitatu, ndipo kumbali inayo kunatulukanso nthambi zitatu.+ 19  Pamalo atatu a nthambi za mbali imodzi, panali masamba ofunga duwa opangidwa ngati maluwa a mtengo wa amondi, ndipo masambawo anatsatizana ndi mfundo ndi maluwa. Pamalo atatu a nthambi za mbali inayo, panalinso masamba ofunga duwa opangidwa ngati maluwa a mtengo wa amondi, ndipo masambawo anatsatizana ndi mfundo ndi maluwa. Nthambi 6 zotuluka m’choikapo nyalecho zinali zotero.+ 20  Ndipo pamalo anayi a choikapo nyalecho panali masamba ofunga duwa opangidwa ngati maluwa a mtengo wa amondi, ndipo masambawo anatsatizana ndi mfundo ndi maluwa.+ 21  Mfundo imodzi inali pansi pa nthambi zake ziwiri, mfundo ina inalinso pansi pa nthambi zake ziwiri, ndipo mfundo inanso inali pansi pa nthambi zinanso ziwiri. Zinali choncho ndi nthambi 6 zotuluka m’choikapo nyale.+ 22  Choikapo nyalecho chinali ndi mfundo ndi nthambi. Chonsechi chinali chiwiya chimodzi chosula, chagolide woyenga bwino.+ 23  Ndiyeno anachipangira nyale 7, zopanira zake zozimitsira nyale ndi mbale zake zoikamo phulusa la zingwe za nyale. Zonsezi zinali zagolide woyenga bwino.+ 24  Choikapo nyalecho pamodzi ndi ziwiya zake zonsezi anazipanga pogwiritsa ntchito golide woyenga bwino wolemera talente limodzi.* 25  Kenako anapanga guwa lansembe zofukiza+ la matabwa a mthethe.+ M’litali mwake linali mkono umodzi, m’lifupi mwake mkono umodzi. Mbali zake zonse zinayi zinali zofanana, ndipo msinkhu wake unali mikono iwiri. Guwalo linali ndi nyanga pamwamba pake.+ 26  Ndiyeno analikuta ndi golide woyenga bwino pamwamba pake ndi m’mbali mwake kuzungulira guwalo, komanso nyanga zake. Analipangira mkombero wagolide wozungulira guwa lonselo.+ 27  Kumbali ziwiri za guwalo anapangako mphete zagolide, ziwiri kumbali iyi ndi zinanso ziwiri kumbali inayo. Anazipanga m’munsi mwa mkombero kuti muzilowa mitengo yonyamulira guwalo.+ 28  Anapanganso mitengo yonyamulira ya mtengo wa mthethe ndipo anaikuta ndi golide.+ 29  Kuwonjezera pamenepo, anapanganso mafuta ogwiritsa ntchito pa kudzoza kopatulika,+ ndi mafuta onunkhira+ osakaniza mwaluso.

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa Eks 25:25.
“Talente limodzi” linali kulemera makilogalamu pafupifupi 34.2.