Ekisodo 34:1-35

34  Pamenepo Yehova anauza Mose kuti: “Sema miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija,+ ndipo ine ndidzalemba pamiyala yosemayo mawu amene anali pamiyala yoyamba ija,+ imene iwe unaswa.+  Ndipo ukonzeke kuti mawa m’mawa ukakwere m’phiri la Sinai ndi kukakhala pafupi ndi ine kumeneko, pamwamba pa phirilo.+  Koma usakwere m’phirimo ndi wina aliyense, ndipo musapezeke wina aliyense mmenemo.+ Kuwonjezera apo, nkhosa kapena ng’ombe zisadye m’tsinde mwa phirilo.”+  Chotero Mose anasemadi miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija, ndipo anadzuka m’mamawa ndi kukwera m’phiri la Sinai, atanyamula miyala iwiriyo m’manja mwake, monga momwe Yehova anam’lamulira.  Pamenepo Yehova anatsika+ mumtambo ndi kuimirira pafupi ndi Mose, n’kulengeza dzina lake lakuti Yehova.+  Ndipo Yehova anadutsa pamaso pa Mose akulengeza kuti: “Yehova, Yehova, Mulungu wachifundo+ ndi wachisomo,+ wosakwiya msanga+ ndiponso wodzaza ndi kukoma mtima kosatha+ ndi choonadi.+  Wosungira mibadwo masauzande kukoma mtima kosatha,+ wokhululukira zolakwa ndi machimo,+ koma wosalekerera konse wolakwa osam’langa.+ Wolanga ana, zidzukulu, ndi ana a zidzukuluzo chifukwa cha zolakwa za abambo awo.”+  Nthawi yomweyo, Mose anagwada n’kuweramira pansi.+  Kenako iye anati: “Tsopano ngati mwandikomera mtima, inu Yehova, chonde, Yehova ayende nafe pakati pathu,+ chifukwa anthuwa ndi ouma khosi,+ ndipo mutikhululukire zolakwa zathu ndi machimo athu,+ ndi kutitenga kukhala chuma chanu.”+ 10  Poyankha Mulungu anati: “Tsopano ndichita nanu pangano ili: Ndidzachita zinthu zodabwitsa pamaso pa anthu ako onse, zinthu zimene sizinachitikepo padziko lonse lapansi kapena m’mitundu yonse.+ Ndipo anthu onse okuzungulirani adzaonadi ntchito za Yehova, chifukwa ndidzachita nanu chinthu chochititsa mantha.+ 11  “Koma inu sungani zimene ndikukulamulani lero.+ Inetu ndikuthamangitsa pamaso panu Aamori, Akanani, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.+ 12  Samalani kuti musachite pangano ndi anthu a m’dziko limene mukupitako+ kuopera kuti ungakhale msampha pakati panu.+ 13  Koma maguwa awo ansembe mukawagwetse, zipilala zawo zopatulika mukaziphwanye ndipo mizati yawo yopatulika mukaidule.+ 14  Pakuti simuyenera kugwadira mulungu wina,+ chifukwa Yehova, amene dzina lake ndi Nsanje, alidi Mulungu wansanje.*+ 15  Samalani, kuopera kuti mungachite pangano ndi anthu okhala m’dzikomo, pakuti iwo adzachita chiwerewere ndi milungu yawo+ ndi kupereka nsembe kwa milungu yawo.+ Chifukwa mukachita nawo pangano, mosakayikira wina adzakuitanani kunyumba kwake ndipo nanunso mudzadya nsembe yakeyo.+ 16  Kenako mudzatenga ena mwa ana awo aakazi kuti akhale akazi a ana anu aamuna,+ ndipo ana awo aakazi adzachita chiwerewere ndi milungu yawo, n’kuchititsa ana anu aamuna kuchita chiwerewere ndi milungu yawo.+ 17  “Musadzipangire milungu ya mafano opangidwa ndi chitsulo chosungunula.+ 18  “Muzisunga chikondwerero cha mkate wosafufumitsa.+ Monga momwe ndinakulamulirani, muzidya mkate wosafufumitsa masiku 7 m’mwezi wa Abibu*+ pa nthawi yoikidwiratu, chifukwa munatuluka mu Iguputo m’mwezi wa Abibu. 19  “Mwana aliyense woyamba kubadwa ndi wanga,+ ngakhalenso mwana woyamba kubadwa wa ziweto zanu zonse, ng’ombe ndi nkhosa.+ 20  Mwana woyamba kubadwa wa bulu muzimuwombola ndi nkhosa.+ Koma ngati simungamuwombole, muzimupha mwa kum’thyola khosi. Ndipo aliyense woyamba kubadwa mwa ana anu aamuna muzimuwombola.+ Palibe amene ayenera kuonekera kwa ine ali chimanjamanja.+ 21  “Muzigwira ntchito zanu kwa masiku 6, koma pa tsiku la 7 muzisunga sabata.+ M’nyengo yolima ndi m’nyengo yokolola muzisunga sabata.+ 22  “Muzichita chikondwerero cha masabata ndi tirigu woyamba kucha pa nyengo yokolola tiriguyo.+ Muzichitanso chikondwerero cha zokolola kumapeto kwa chaka.+ 23  “Katatu pa chaka, mwamuna aliyense pakati panu azionekera+ kwa Ambuye woona, Yehova, Mulungu wa Isiraeli. 24  Pakuti ndidzathamangitsira mitunduyo kutali ndi inu,+ ndipo ndidzakuza dera lanu.+ Palibe aliyense adzasirira dziko lanu pamene mwachoka kukaona nkhope ya Yehova Mulungu wanu katatu pa chaka.+ 25  “Popereka magazi a nsembe yanga musawapereke limodzi ndi chilichonse chofufumitsa.+ Ndipo nsembe ya chikondwerero cha pasika isamagone mpaka m’mawa.+ 26  “Zipatso zoyamba kucha zabwino koposa+ za m’munda mwanu muzibwera nazo kunyumba ya Yehova Mulungu wanu.+ “Musawiritse mwana wa mbuzi mumkaka wa mayi wake.”+ 27  Pamenepo Yehova anauza Mose kuti: “Dzilembere mawuwa+ chifukwa ine ndikuchita pangano ndi iwe ndi Isiraeli mogwirizana ndi mawu amenewa.”+ 28  Choncho Mose anakhalabe m’phirimo ndi Yehova masiku 40, usana ndi usiku. Iye sanadye mkate kapena kumwa madzi.+ Ndipo Mulungu analemba mawu a pangano, Mawu Khumi,* pamiyala yosemayo.+ 29  Ndiyeno Mose anatsika m’phiri la Sinai atanyamula miyala iwiri ija ya Umboni m’manja mwake,+ koma iye sanadziwe kuti nkhope yake inali kuwala chifukwa anali atalankhula ndi Mulungu.+ 30  Aroni ndi ana onse a Isiraeli ataona Mose, anaona kuti nkhope yake ikuwala, ndipo anaopa kumuyandikira.+ 31  Pamenepo Mose anawaitana. Chotero Aroni ndi atsogoleri onse a khamu la Isiraeli anabwerera kwa iye, ndipo Mose anayamba kulankhula nawo. 32  Kenako ana onse a Isiraeli anamuyandikira, ndipo iye anayamba kuwauza malamulo onse amene Yehova anam’patsa paphiri la Sinai.+ 33  Mose akatha kulankhula nawo anali kuika chophimba pankhope yake.+ 34  Koma Mose akamalowa kukaonekera kwa Yehova kuti akalankhule naye, anali kuchotsa chophimbacho mpaka atatulukamo.+ Kenako anali kupita kwa ana a Isiraeli ndi kuwauza zimene walamulidwa.+ 35  Ndipo ana a Isiraeli anali kuona kuti nkhope ya Mose ikuwala.+ Choncho Mose anali kuphimbanso nkhope yake mpaka atabwerera kukalankhula ndi Mulungu.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti “Mulungu wofuna kuti anthu azidzipereka kwa iye yekha.”
Onani Zakumapeto 13.
Mawu akuti “Mawu Khumi” akutanthauza mawu khumi olamula, zinthu khumi zoyenera kuchita, kapena Malamulo Khumi.