Ekisodo 25:1-40

25  Ndiyeno Yehova anauza Mose kuti:+  “Uza ana a Isiraeli kuti apereke zopereka kwa ine. Anthu inu mulandire zopereka zanga kwa munthu aliyense amene mtima wake wamulimbikitsa.+  Zopereka zimene muyenera kulandira kwa iwo ndi izi: golide,+ siliva,+ mkuwa,+  ulusi wabuluu, ubweya wa nkhosa wonyika mu utoto wofiirira, ulusi wofiira kwambiri, nsalu zabwino kwambiri, ndi ubweya wa mbuzi.+  Mulandirenso kwa iwo zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira, zikopa za akatumbu,* matabwa a mthethe,+  mafuta a nyale,+ mafuta a basamu+ opangira mafuta odzozera,+ ndi zofukiza zonunkhira.+  Komanso mulandire miyala ya onekisi ndi miyala yozika pa efodi*+ ndi pachovala pachifuwa.+  Ndipo mundipangire malo opatulika, popeza ndiyenera kukhala pakati panu.+  Mukapange chihema chopatulika ndi ziwiya zake mogwirizana ndendende ndi zonse zimene ndikukusonyeza.+ 10  “Mundipangire Likasa la mtengo wa mthethe,+ mikono* iwiri ndi hafu m’litali, mkono umodzi ndi hafu m’lifupi, ndi mkono umodzi ndi hafu msinkhu wake. 11  Kenako ulikute ndi golide woyenga bwino.+ Mkati ndi kunja komwe ulikute ndi golide, ndipo upange mkombero wagolide kuzungulira Likasalo.+ 12  Ulipangire mphete zinayi zagolide ndi kuziika pamwamba pa miyendo yake inayi. Mphete ziwiri zikhale mbali imodzi, ndipo mphete zina ziwiri zikhale mbali inayo.+ 13  Upangenso mitengo yonyamulira ya mtengo wa mthethe ndi kuikuta ndi golide.+ 14  Ulowetse mitengo yonyamulirayo mumphete zija za m’mbali mwa Likasa kuti azinyamulira Likasalo. 15  Mitengo yonyamulirayo izikhala mumphete za Likasalo. Isachotsedwemo.+ 16  M’Likasamo uikemo umboni umene ndidzakupatsa.+ 17  “Kenako upange chivundikiro chagolide woyenga bwino, mikono iwiri ndi hafu m’litali, ndi mkono umodzi ndi hafu m’lifupi.+ 18  Upangenso akerubi awiri agolide. Akhale osula ndipo uwaike kumapeto onse awiri a chivundikirocho.+ 19  Uike kerubi mmodzi kumbali imodzi ya chivundikirocho ndi kerubi wina kumbali inayo.+ Akerubiwo uwaike kumbali zonse ziwiri za chivundikirocho. 20  Ndipo akweze mapiko awo m’mwamba ali otambasula, aphimbe chivundikirocho ndi mapiko awo, ndipo akhale moyang’anizana,+ koma nkhope zawo ziweramire pachivundikiro. 21  Chivundikirocho+ uchiike pamwamba pa Likasalo, ndipo m’Likasamo uikemo umboni umene ndidzakupatsa. 22  Ine ndidzaonekera kwa iwe pamenepo ndi kulankhula nawe kuchokera pamwamba pa chivundikiro,+ pakati pa akerubi awiriwo amene ali pamwamba pa likasa la umboni. Kuchokera pamenepo ndidzakulamula zonse zokhudza ana a Isiraeli.+ 23  “Ndiyeno upange tebulo+ la mtengo wa mthethe, mikono iwiri m’litali, mkono umodzi m’lifupi ndi mkono umodzi ndi hafu msinkhu wake. 24  Ulikute ndi golide woyenga bwino, ndipo upange mkombero wagolide kuzungulira tebulo lonselo.+ 25  Ulipangirenso felemu, muyezo wake chikhatho* chimodzi m’lifupi mwake. Felemuli lizungulire tebulo lonse ndipo upange mkombero wagolide pafelemulo.+ 26  Tebulolo ulipangire mphete zinayi zagolide ndi kuziika m’makona ake anayi mmene muli miyendo yake inayi.+ 27  Mphetezo zikhale pafupi ndi felemu lija kuti muzilowa mitengo yonyamulira tebulolo.+ 28  Upangenso mitengo yonyamulira ya mtengo wa mthethe ndi kuikuta ndi golide. Mitengo imeneyi azinyamulira tebulolo.+ 29  “Ndiyeno upange mbale zake, zikho, mitsuko ndi mbale zolowa zoti azithirira nsembe zachakumwa. Uzipange ndi golide woyenga bwino.+ 30  Ndipo patebulopo uziikapo mkate wachionetsero pamaso panga nthawi zonse.+ 31  “Kenako upange choikapo nyale chagolide woyenga bwino. Chimenechi chikhale chosula.+ Choikapo nyalecho chikhale ndi tsinde, nthambi, masamba ofunga duwa, mfundo ndi maluwa. 32  Choikapo nyalecho chikhale ndi nthambi 6, kumbali ina kutuluke nthambi zitatu, ndipo kumbali inayo kutulukenso nthambi zitatu.+ 33  Pamalo atatu a nthambi za mbali imodzi, pakhale masamba ofunga duwa opangidwa ngati maluwa a mtengo wa amondi, ndipo masambawo atsatizane ndi mfundo ndi maluwa. Pamalo atatu a nthambi za mbali inayo, pakhalenso masamba ofunga duwa opangidwa ngati maluwa a mtengo wa amondi, ndipo masambawo atsatizane ndi mfundo ndi maluwa.+ Nthambi 6 zotuluka m’choikapo nyalecho zikhale zotero. 34  Ndipo pamalo anayi a choikapo nyalecho pakhale masamba ofunga duwa opangidwa ngati maluwa a mtengo wa amondi, ndipo masambawo atsatizane ndi mfundo ndi maluwa.+ 35  Mfundo imodzi ikhale pansi pa nthambi zake ziwiri, mfundo ina ikhalenso pansi pa nthambi zake ziwiri, ndipo mfundo inanso ikhale pansi pa nthambi zinanso ziwiri. Zikhale choncho ndi nthambi 6 zotuluka m’choikapo nyale.+ 36  Choikapo nyalecho chikhale ndi mfundo ndi nthambi. Chonsechi chisulidwe monga chiwiya chimodzi, chagolide woyenga bwino.+ 37  Ndipo uchipangire nyale 7. Nyalezo ziziyatsidwa kuti ziziunikira patsogolo pake.+ 38  Zopanira zake zozimitsira nyale ndi mbale zake zoikamo phulusa la zingwe za nyale, zikhale zagolide woyenga bwino.+ 39  Choikapo nyalecho pamodzi ndi ziwiya zake zonsezi azipange pogwiritsa ntchito golide woyenga bwino wolemera talente limodzi.* 40  Uonetsetse kuti wazipanga motsatira chitsanzo chimene wasonyezedwa m’phiri.+

Mawu a M'munsi

Katumbu ndi nyama yaubweya ya m’madzi, ndipo katumbu amene akutchulidwa pano ndi mtundu waukulu wa akatumbu amene amapezeka m’nyanja zikuluzikulu.
Zikuoneka kuti chimenechi chinali chovala chofanana ndi epuloni, ndipo chinali ndi nsalu yakutsogolo ndi yakumbuyo. Onani Zakumapeto 14.
“Mkono umodzi” ndi wofanana ndi masentimita 44 ndi hafu.
“Chikhatho” chimenechi chinali muyezo wokwana masentimita 7.4.
“Talente limodzi” limalemera makilogalamu pafupifupi 34.2.