Ekisodo 24:1-18

24  Choncho Mulungu anauza Mose kuti: “Kwera upite kwa Yehova, iweyo, Aroni, Nadabu, Abihu+ ndi akulu 70+ a Isiraeli, ndipo mugwade chapatali.  Mose yekha ayandikire kwa Yehova, koma enawo asayandikire. Anthu ena onse asakwere m’phiri.”+  Ndiyeno Mose anapita kwa anthu ndi kuwafotokozera mawu onse a Yehova ndi zigamulo zake zonse.+ Pamenepo anthu onse anayankhira pamodzi kuti: “Mawu onse amene Yehova wanena tidzachita.”+  Choncho Mose analemba mawu onse a Yehova.+ Ndiyeno anadzuka m’mawa kwambiri n’kumanga guwa lansembe ndi zipilala 12 zoimira mafuko 12 a Isiraeli, m’tsinde mwa phiri.+  Kenako anatuma anyamata a Isiraeli ndipo anyamatawo anapereka nsembe zopsereza komanso anapereka ng’ombe kuti zikhale nsembe zachiyanjano+ kwa Yehova.  Pamenepo Mose anatenga hafu ya magazi ndi kuwaika m’mbale zolowa,+ ndipo hafu inayo anawaza paguwa lansembe.+  Ndiyeno anatenga buku la pangano+ ndi kuwerengera anthuwo kuti amve.+ Zitatero anthuwo anati: “Zonse zimene Yehova wanena tidzachita zomwezo ndipo tidzamumvera.”+  Pamenepo Mose anatenga magaziwo ndi kuwaza anthuwo,+ ndipo anati: “Awa ndiwo magazi okhazikitsira pangano+ limene Yehova wapangana nanu mwa mawu onsewa.”  Choncho Mose, Aroni, Nadabu, Abihu ndi akulu 70 a Isiraeli anakwera m’phirimo, 10  ndipo anaona Mulungu wa Isiraeli.+ Pansi pa mapazi ake panali chinthu chooneka ngati miyala ya safiro yoyalidwa bwino, choyera ngati kumwamba.+ 11  Mulungu sanawononge atsogoleri amenewo a ana a Isiraeli,+ koma iwo anaona masomphenya a Mulungu woona+ ndipo anadya ndi kumwa.+ 12  Pamenepo Yehova anauza Mose kuti: “Kwera m’phiri muno ufike kwa ine ndi kukhala momwe muno, pakuti ndikufuna kukupatsa miyala yosema imene ndalembapo chilamulo kuti ndiphunzitse anthu.”+ 13  Choncho Mose ndi Yoswa mtumiki wake ananyamuka, ndipo Mose anakwera m’phiri la Mulungu woona.+ 14  Koma Mose anali atauza akuluwo kuti: “Tidikireni pompano mpaka titabwerako.+ Panotu muli ndi Aroni ndi Hura.+ Aliyense amene ali ndi mlandu wofuna kuweruzidwa afikire iwowa.”+ 15  Motero Mose anakwera m’phirimo, mtambo utakuta phirilo.+ 16  Ulemerero wa Yehova+ unakhalabe paphiri la Sinai,+ ndipo mtambowo unakutabe phirilo kwa masiku 6. Ndiyeno pa tsiku la 7, Mulungu anaitana Mose kuchokera mumtambowo.+ 17  Kwa ana a Isiraeli, ulemerero wa Yehova unali kuoneka ngati moto wolilima+ pamwamba pa phiri. 18  Kenako Mose analowa mumtambomo ndi kukwera m’phirimo.+ Mose anakhala mmenemo masiku 40, usana ndi usiku.+

Mawu a M'munsi