Ekisodo 22:1-31

22  “Munthu akaba ng’ombe kapena nkhosa, n’kuipha kapena kuigulitsa, azilipira ng’ombe zisanu pa ng’ombe imodzi imene waba, ndi nkhosa zinayi pa nkhosa imodzi imene waba.+  (“Wakuba+ akapezeka akuthyola nyumba kuti abe+ ndipo akakanthidwa n’kufa, amene wamuphayo alibe mlandu wa magazi.+  Ngati dzuwa linali litatuluka, amene wamuphayo ali ndi mlandu wa magazi.) “Wakuba azilipira ndithu. Ngati alibe kalikonse, pamenepo azigulitsidwa kuti alipire zinthu zimene anabazo.+  Ngati zimene anabazo zapezeka ndi iyeyo zili zamoyo, kaya ndi ng’ombe, bulu kapena nkhosa, azilipira zowirikiza kawiri.  “Munthu akalekerera ziweto zake kukadya m’munda wa mpesa kapena wa mbewu zina, kapena watumiza nyama zake zonyamula katundu kukadya m’munda wa munthu wina, azilipira+ popereka zokolola zabwino koposa za m’munda wake wa mpesa kapena za m’munda wake wa mbewu zina.  “Moto ukabuka n’kugwirira zomera zaminga, ndipo wafalikira m’munda n’kutentha mitolo yambewu, mbewu zosadula kapena munda wonse,+ amene anayatsa motowo azilipira ndithu chifukwa cha zotenthedwazo.  “Munthu akapatsa mnzake ndalama kapena katundu wina kuti amusungire,+ zinthuzo n’kubedwa m’nyumba ya mnzakeyo, wakubayo akapezeka azilipira zowirikiza kawiri.+  Ngati wakubayo sanapezeke, azibweretsa mwininyumbayo pafupi ndi Mulungu woona*+ pofuna kuona ngati iyeyo sanatenge katundu wa mnzakeyo.  Koma pa milandu iliyonse+ yokhudza ng’ombe, bulu, nkhosa, chovala, kapena chilichonse chimene chinasowa chimene angachiloze kuti, ‘Ichi n’changa!’ awiri onsewo mlandu wawo uzifika pamaso pa Mulungu woona.+ Amene Mulungu adzamuweruze kuti ndiye woipa, azilipira mnzake zowirikiza kawiri.+ 10  “Munthu akapatsa mnzake bulu, ng’ombe, nkhosa kapena chiweto chilichonse kuti amusungire, ndipo chafa, chalumala kapena chabedwa popanda woona zimene zachitika, 11  iye alumbire+ kwa mnzake pamaso pa Yehova kuti si iye amene wachita zimenezo pa katundu wa mnzake.+ Mwini wa katunduyo azivomereza lumbirolo ndipo mnzakeyo asalipire. 12  Koma ngati anachita kum’bera,* azilipira kwa mwini wa katunduyo.+ 13  Ngati nyamayo inaphedwa ndi chilombo,+ azibweretsa nyama yakufayo monga umboni.+ Asalipire pa nyama iliyonse yophedwa ndi chilombo. 14  “Koma ngati munthu wabwereka chiweto kwa mnzake+ ndipo chalumala kapena chafa mwiniwake palibe, wobwerekayo azilipira ndithu.+ 15  Ngati mwiniwake alipo, wobwerekayo asalipire. Ngati anafunika kupereka ndalama kuti abwereke, adzangopereka ndalama yobwerekera chiwetocho. 16  “Mwamuna akanyengerera namwali wosalonjezedwa kukwatiwa n’kugona naye,+ azim’tenga ndithu kukhala mkazi wake atapereka chiwongo.*+ 17  Bambo a namwaliyo akakaniratu kum’patsa mwana wawo, iye aziperekabe chiwongo chimene amaperekera namwali.+ 18  “Mkazi wamatsenga musam’lole kukhala ndi moyo.+ 19  “Aliyense wogonana ndi nyama aziphedwa ndithu.+ 20  “Wopereka nsembe kwa milungu ina osati kwa Yehova yekha aziphedwa ndithu.+ 21  “Musachitire nkhanza mlendo wokhala pakati panu kapena kum’pondereza,+ chifukwa anthu inu munalinso alendo m’dziko la Iguputo.+ 22  “Anthu inu musazunze mkazi wamasiye kapena mwana wamasiye* aliyense.+ 23  Mukamuzunza ngakhale pang’ono, iye n’kundilirira, ndidzamva ndithu kulira kwake.+ 24  Pamenepo mkwiyo wanga udzakuyakirani,+ ndipo ndidzakuphani ndithu ndi lupanga, kuti akazi anu akhale akazi amasiye ndiponso ana anu akhale ana amasiye.+ 25  “Ukabwereketsa ndalama kwa anthu anga, kwa munthu wovutika amene ali pafupi ndi iwe,+ usakhale ngati munthu wopereka ngongole yakatapira* kwa iye. Usafunepo chiwongoladzanja.+ 26  “Mnzako ukamulanda chovala chake monga chikole,+ uzim’bwezera dzuwa likamalowa. 27  Pakuti chofunda chake n’chomwecho.+ Imeneyo ndi nsalu yake yakunja. Adzafunda chiyani pogona? Ndiyeno akandilirira, ine ndidzamumvera ndithu, chifukwa ndine wachifundo.+ 28  “Usatemberere Mulungu+ kapena kutemberera mtsogoleri amene ali pakati pa anthu ako.+ 29  “Popereka zokolola zako zambirizo komanso zotuluka moponderamo mphesa ndi moyengeramo mafuta zochulukazo, usapereke monyinyirika.+ Mwana wako wamwamuna woyamba kubadwa uzim’pereka kwa ine.+ 30  Zimene uzichita ndi mwana woyamba kubadwa wa ng’ombe ndi wa nkhosa yako ndi izi:+ Azikhala ndi mayi wake masiku 7.+ Pa tsiku la 8 uzim’pereka kwa ine. 31  “Inuyo muzikhala anthu oyera pamaso panga+ ndipo musadye nyama imene yaphedwa ndi chilombo kuthengo.+ Imeneyo muziponyera agalu.+

Mawu a M'munsi

Kutanthauza kuti, kupita naye kwa oweruza oimira Mulungu woona.
Mwina chifukwa cha kusasamala kapena chifukwa cha zochitika zina zimene akanatha kuzipewa.
“Chiwongo” ndi ndalama zimene mwamuna amalipira pokwatira. Ena amati “chimalo.”
Mawu ake enieni, “mwana wamwamuna wopanda bambo.”
“Ngongole yakatapira” ndi ngongole imene munthu pobweza amayenera kuwonjezerapo ndalama zina zochuluka. Ena amati “kalowa.”