Deuteronomo 34:1-12

34  Ndiyeno Mose anachoka m’chipululu cha Mowabu kupita m’phiri la Nebo,+ pamwamba pa Pisiga,+ moyang’anana ndi Yeriko.+ Pamenepo Yehova anayamba kumuonetsa dziko lonse, kuchokera ku Giliyadi mpaka ku Dani.+  Anamuonetsanso dziko lonse la Nafitali, dziko la Efuraimu ndi la Manase, dziko lonse la Yuda mpaka kunyanja ya kumadzulo.+  Anamuonetsa Negebu+ ndi Chigawo*+ cha Yorodano, chigwa cha ku Yeriko, mzinda wa mitengo ya kanjedza,+ mpaka ku Zowari.+  Ndiyeno Yehova anamuuza kuti: “Dziko lija ndinalumbira kwa Abulahamu, Isaki ndi Yakobo kuti, ‘Ndidzalipereka kwa mbewu yako’+ ndi limeneli. Ndakuonetsa kuti ulione ndi maso ako chifukwa sudzawoloka kukalowa m’dzikolo.”+  Kenako Mose mtumiki wa Yehova+ anafera pamenepo m’dziko la Mowabu, mogwirizana ndi zimene Yehova analamula.+  Iye anamuika m’manda m’chigwa, m’dziko la Mowabu moyang’anana ndi Beti-peori,+ ndipo palibe amene akudziwa manda ake kufikira lero.+  Mose anamwalira ali ndi zaka 120.+ Diso lake silinachite mdima+ ndipo anali adakali ndi mphamvu.+  Ana a Isiraeli analira Mose m’chipululu cha Mowabu masiku 30.+ Ndiyeno masiku onse olira maliro a Mose anatha.  Yoswa mwana wa Nuni anali wodzazidwa ndi mzimu wa nzeru,+ pakuti Mose anaika manja ake pa iye.+ Choncho ana a Isiraeli anayamba kumumvera ndipo iwo anayamba kuchita monga momwe Yehova analamulira Mose.+ 10  Koma mu Isiraeli simunakhalebe mneneri aliyense wofanana ndi Mose,+ amene Yehova anali kumudziwa pamasom’pamaso,+ 11  amene anachita zizindikiro ndi zozizwitsa zonse zimene Yehova anam’tuma kukachita m’dziko la Iguputo kwa Farao, kwa atumiki ake onse ndi m’dziko lake lonse.+ 12  Simunakhalebe mneneri amene anachita zinthu zazikulu ndi zoopsa ndi dzanja lake lamphamvu, ngati zimene Mose anachita pamaso pa Aisiraeli onse.+

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa Ge 13:10.