Deuteronomo 32:1-52

32  “Tamverani kumwamba inu, ndiloleni ndilankhule.Ndipo dziko lapansi limve mawu a pakamwa panga.+   Malangizo anga adzagwa ngati mvula,+Mawu anga adzatsika ngati mame,+Ngati mvula yowaza pa udzu,+Ngatinso mvula yamphamvu pazomera.+   Pakuti ndidzalengeza dzina la Yehova.+Vomerezani ukulu wa Mulungu wathu!+   Iye ndi Thanthwe, ndipo ntchito yake ndi yangwiro,+Njira zake zonse ndi zolungama.+Mulungu wokhulupirika,+ amene sachita chosalungama.+Iye ndi wolungama ndi wowongoka.+   Iwo achita okha zinthu zowawonongetsa,+Si ana ake, chilemacho n’chawo.+Iwo ndiwo m’badwo wopotoka maganizo ndi wokhotakhota!+   Kodi mukupitiriza kuchitira Yehova mwa njira imeneyi,+Anthu opusa ndi opanda nzeru inu?+Kodi iye si Atate wanu amene anakulengani,+Amene anakupangani ndi kukuchititsani kukhazikika?+   Kumbukirani masiku akale,+Ganizirani zaka za mibadwomibadwo ya m’mbuyomu.Funsa bambo ako ndipo akuuza,+Amuna achikulire pakati panu, ndipo akufotokozera.+   Pamene Wam’mwambamwamba anapereka cholowa kwa mitundu,+Pamene analekanitsa ana a Adamu,+Anaika malire a anthu+Poganizira chiwerengero cha ana a Isiraeli.+   Pakuti gawo la Yehova ndilo anthu ake.+Yakobo ndiye gawo la cholowa chake.+ 10  Anam’peza m’dziko lachipululu,+M’chipululu chopanda kanthu, molira zilombo zakutchire.+Pamenepo anayamba kum’zungulira,+ kum’samalira,+Kum’teteza monga mwana wa diso lake.+ 11  Monga mmene chiwombankhanga chimagwedezera mwamphamvu chisa chake,Mmene chimaulukira pamwamba pa ana ake,+Mmene chimatambasulira mapiko ake, ndi kutenga anawo,N’kuwanyamula pamapiko ake,+ 12  Yehova yekha anapitiriza kumutsogolera,+Ndipo panalibe mulungu wachilendo kuwonjezera pa iye.+ 13  Anapitiriza kumuyendetsa pamapiri a dziko lapansi,+Moti anadya zokolola za m’minda.+Anapitirizanso kumudyetsa uchi wochokera m’thanthwe,+Ndi mafuta ochokera m’mwala wa nsangalabwi.+ 14  Anamudyetsanso mafuta a mkaka wa ng’ombe ndi mkaka wa nkhosa,+Pamodzi ndi mafuta a nkhosa.Anamudyetsa nkhosa zamphongo za ku Basana, mbuzi zamphongo,+Pamodzi ndi tirigu wabwino koposa ngati mafuta okuta impso.+Ndipo anali kumwa magazi a mphesa monga vinyo.+ 15  Yesuruni*+ atayamba kunenepa, anayamba kupanduka.+Iwe wanenepa, wakulupala, wakhuta mopitirira muyezo.+Pamenepo iye anasiya Mulungu amene anam’panga,+Ndi kunyoza Thanthwe+ la chipulumutso chake. 16  Anayamba kuputa nsanje+ yake ndi milungu yachilendo.+Anapitiriza kumukhumudwitsa ndi zinthu zonyansa.+ 17  Iwo anali kupereka nsembe kwa ziwanda, osati kwa Mulungu.+Anapereka nsembe kwa milungu imene sanaidziwe,+Milungu yatsopano yongobwera kumene,+Imene makolo anu akale sanaidziwe. 18  Munaiwala Thanthwe limene linakuberekani,+Ndipo munayamba kuiwala Mulungu amene anachititsa kuti mukhalepo kudzera mwa zowawa za pobereka.+ 19  Yehova ataona zimenezi anayamba kuwanyoza,+Chifukwa chakuti ana ake aamuna ndi aakaziwo anam’sautsa. 20  Choncho iye anati, ‘Ndiwabisire nkhope yanga,+Ndione kuti ziwathera bwanji.Pakuti iwo ndi m’badwo wokonda zoipa,+Ana osakhulupirika.+ 21  Iwo andichititsa nsanje ndi milungu yachabe.+Andisautsa ndi mafano awo opanda pake.+Ndipo ine ndidzawachititsa nsanje ndi anthu achabe,+Ndidzawakhumudwitsa ndi mtundu wopusa.+ 22  Pakuti pa kukwiya kwanga moto wayaka,+Ndipo udzayaka mpaka kukafika ku Manda,* malo a pansi penipeni.+Udzanyeketsa dziko lapansi ndi zipatso zake,+Ndi kuyatsa maziko a mapiri.+ 23  Ndidzawonjezera masoka awo,+Mivi yanga ndidzaithera pa iwo.+ 24  Adzalefuka ndi njala+ ndi kuwonongeka ndi matenda otentha thupi koopsa,+Ndi chiwonongeko chowawa.+Ndidzawatumizira zilombo za mano ataliatali,+Pamodzi ndi njoka zapoizoni za m’fumbi.+ 25  Kunja lupanga lidzawasandutsa anamfedwa,+Ndipo mkati mwa nyumba, mantha adzawasandutsa anamfedwa.+Zimenezi zidzawaphera anyamata ndi anamwali,+Mwana woyamwa pamodzi ndi munthu wa imvi.+ 26  Ndikananena kuti: “Ndidzawabalalitsa,+Ndidzachititsa anthu kuti asatchule n’komwe za iwo,”+ 27  Ngati ndikanati sindikuopa kusautsidwa ndi mdani,+Kuti adani awo angamve molakwa,+Kutinso anganene kuti: “Dzanja lathu lapambana,+Ndipo si Yehova amene wachita zonsezi.”+ 28  Pakuti iwo ndi mtundu wopanda nzeru,+Ndipo ndi osazindikira.+ 29  Akanakhala anzeru,+ akanaganizira mozama zimenezi.+Akanalingalira kuti ziwathera bwanji.+ 30  Kodi munthu mmodzi angathamangitse bwanji anthu 1,000,Kapena anthu awiri angapitikitse bwanji anthu 10,000?+ N’zosatheka, pokhapokha Thanthwe lawo litawagulitsa,+Komanso ngati Yehova atawapereka. 31  Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu,+Ndipo adani athu angavomereze zimenezi.+ 32  Mtengo wawo wa mpesa ndi wochokera ku mtengo wa mpesa wa ku Sodomu,Ndi kuminda ya m’mapiri a ku Gomora.+ Zipatso zawo za mphesa ndi zakupha,Ndipo ndi zowawa.+ 33  Vinyo wawo ndi poizoni wa njoka zikuluzikulu,Ndiponso ndi poizoni wakupha wa mamba.+ 34  Kodi sindinasunge zimenezi,Ndi kuziikira chidindo m’nkhokwe yanga?+ 35  Kubwezera ndi kwanga, chilangonso ndi changa.+Pa nthawi yoikidwiratu phazi lawo lidzaterereka poyenda,+Pakuti tsiku la tsoka lawo layandikira,+Ndipo zowagwera zikufika mofulumira.’+ 36  Pakuti Yehova adzaweruza anthu ake,+Ndipo adzamva chisoni chifukwa cha atumiki ake,+Chifukwa adzaona kuti thandizo lawachokera.Adzaona kuti pangokhala munthu wonyozeka ndi wopanda pake. 37  Pamenepo iye adzati, ‘Ili kuti milungu yawo,+Thanthwe limene anathawirako,+ 38  Milungu imene inali kudya mafuta a nsembe zawo,+Ndi kumwa vinyo wa nsembe zawo zachakumwa?+Ibwere kudzakuthandizani.+Ikhaletu malo anu obisalamo.+ 39  Onani tsopano kuti ndine Mulungu,+Ndipo palibe milungu ina pamodzi ndi ine.+Ndimapha ndiponso ndimapereka moyo.+Ndavulaza koopsa,+ ndipo ine ndidzachiritsa,+Palibe aliyense wonditsomphola m’dzanja langa.+ 40  Ndikukweza dzanja langa kumwamba polumbira,+Ndipo ndikunena kuti: “Pali ine, Mulungu wamoyo wosatha,”+ 41  Ndikanoladi lupanga langa lonyezimira,+Dzanja langa likagwira chiweruzo,+Ndidzalipsira adani anga,+Ndipo ndidzabwezera chilango kwa odana nane kwambiri.+ 42  Ndidzaledzeretsa mivi yanga ndi magazi,+Magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa.Ndipo lupanga langa lidzadya nyama,+Pamodzi ndi mitu ya atsogoleri a adani.’+ 43  Kondwerani, mitundu inu, pamodzi ndi anthu ake,+Pakuti adzabwezera magazi a atumiki ake,+Ndipo adzabwezera chilango kwa adani ake,+Nadzaphimba machimo a dziko la anthu ake.” 44  Pamenepo Mose anabwera ndi kulankhula mawu onse a nyimbo iyi m’makutu mwa anthu onse,+ iye pamodzi ndi Hoseya* mwana wa Nuni.+ 45  Mose atamaliza kulankhula mawu onsewa kwa Aisiraeli onse, 46  anapitiriza kuwauza kuti: “Ganizirani mofatsa mawu onse amene ndikulankhula mokuchenjezani lero,+ ndipo muuze ana anu kuti aonetsetse kuti akuchita zimene mawu onse a chilamulo ichi akunena.+ 47  Pakuti amenewa si mawu opanda pake kwa inu,+ chifukwa mawu amenewa ndiwo moyo wanu.+ Mwa kutsatira mawu amenewa mudzatalikitsa masiku anu panthaka imene mukupita kukaitenga kukhala yanu, mutawoloka Yorodano.”+ 48  Yehova anapitiriza kulankhula ndi Mose pa tsiku lomweli kuti: 49  “Kwera m’phiri ili la Abarimu,+ phiri la Nebo,+ limene lili m’dziko la Mowabu, moyang’anana ndi Yeriko, ndipo uone dziko la Kanani limene ndikupereka kwa ana a Isiraeli kuti likhale lawo.+ 50  Pamenepo ukafera m’phiri limene ukukwera ndi kugona ndi makolo ako,+ monga mmene Aroni m’bale wako anafera m’phiri la Hora+ ndi kugona ndi makolo ake. 51  Izi zili choncho chifukwa anthu inu munachita mosakhulupirika kwa ine+ pakati pa ana a Isiraeli, kumadzi a pa Meriba+ ku Kadesi, m’chipululu cha Zini. Ndiponso chifukwa chakuti anthu inu simunandilemekeze pakati pa ana a Isiraeli.+ 52  Pakuti udzaona dzikolo uli patali, koma sudzalowa m’dziko limene ndikupereka kwa ana a Isiraeli.”+

Mawu a M'munsi

Kutanthauza “Wolungama.” Limeneli ndi dzina laulemu la Isiraeli.
Onani Zakumapeto 5.
Dzina lakale la Yoswa.