Deuteronomo 20:1-20

20  “Mukapita kunkhondo kukamenyana ndi adani anu, musachite nawo mantha mukaona kuti ali ndi mahatchi ndi magaleta ankhondo,+ ndiponso mukaona kuti adani anuwo ndi ochuluka kwambiri kuposa inu. Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani m’dziko la Iguputo ali ndi inu.+  Mukayandikira kuti mumenyane nawo, wansembe azifika pafupi nanu ndi kulankhula ndi anthu+  kuti, ‘Mverani Aisiraeli inu. Lero mukuyandikira adani anu kuti mumenyane nawo. Mitima yanu isachite mantha.+ Musaope ndipo musathawe mwamantha kapena kunjenjemera chifukwa cha iwo,+  chifukwa Yehova Mulungu wanu akuyenda limodzi nanu kuti akumenyereni nkhondo ndi kukupulumutsani kwa adani anu.’+  “Atsogoleri+ nawonso azilankhula ndi anthuwo kuti, ‘Kodi pali amene wamanga nyumba yatsopano koma sanaitsegulire? Achoke ndi kubwerera kunyumba yakeyo, kuopera kuti angafe pankhondo, ndipo munthu wina angatsegulire nyumbayo.+  Kodi pali amene walima munda wa mpesa koma sanayambe kukolola zipatso zake? Achoke ndi kubwerera kunyumba yake, kuopera kuti angafe pankhondo ndipo munthu wina angakolole za m’munda wakewo.+  Kodi pali amene analonjeza mkazi kuti adzamukwatira ndipo sanamutenge? Achoke ndi kubwerera kunyumba yake,+ kuopera kuti angafe pankhondo ndipo mwamuna wina angatenge mkaziyo.’  Ndiyeno atsogoleri apitirize kulankhula ndi anthuwo kuti, ‘Kodi pali wamantha ndi wosalimba mtima?+ Achoke ndi kubwerera kunyumba yake, kuti angachititse mantha mitima ya abale ake ngati mmene wachitira mtima wake.’+  Atsogoleriwo akamaliza kulankhula ndi anthu, azisankha akulu a magulu ankhondo oti akhale patsogolo pa anthuwo. 10  “Mukayandikira mzinda kuti mumenyane nawo, muzilengeza kumzindawo mfundo za mtendere.+ 11  Ndiyeno ngati mzindawo wakupatsani yankho la mtendere ndipo akutsegulirani zipata zake, pamenepo anthu onse opezeka mmenemo azikhala anu kuti azikugwirirani ntchito yaukapolo. Iwo azikutumikirani.+ 12  Koma ngati mzindawo sukukhazikitsa mtendere ndi inu,+ ndipo ukuchita nanu nkhondo, moti inuyo mwauzungulira, 13  Yehova Mulungu wanu adzaupereka ndithu m’manja mwanu, ndipo zikatero muzipha mwamuna aliyense ndi lupanga.+ 14  Koma musaphe akazi, ana aang’ono,+ ziweto+ ndi chilichonse chopezeka mumzindawo. Muzifunkha+ zinthu zonse za mumzindawo ndipo muzidya zimene mwafunkha kwa adani anu amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.+ 15  “Muzichita zimenezi ndi mizinda yonse yakutali kwambiri ndi inu imene siili pakati pa mizinda ya mitundu iyi. 16  Mizinda yokhayi ya anthu awa a mitundu ina imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani monga cholowa, ndi imene simuyenera kusiyamo chilichonse chopuma chili chamoyo,+ 17  chifukwa muyenera kuwawononga ndithu. Mukawononge Ahiti, Aamori, Akanani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi,+ monga mmene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani. 18  Mukawawononge kuti asakakuphunzitseni kuchita zinthu zawo zonse zonyansa zimene achitira milungu yawo, kuti mungachimwire Yehova Mulungu wanu.+ 19  “Mukazungulira mzinda kwa masiku ambiri mwa kumenyana nawo kuti muulande, musawononge mitengo yake mwa kuisamulira nkhwangwa. Muyenera kudya zipatso za mitengoyo, chotero simuyenera kuidula.+ Kodi mtengo wa m’munda ndi munthu kuti muwuukire? 20  Mungathe kuwononga mtengo wokhawo umene mukuudziwa kuti subereka zipatso zakudya. Mtengo woterowo mungaudule ndi kumangira mpanda wozungulira+ mzinda wa adani umene ukuchita nanu nkhondo, kufikira mzindawo utagwa.

Mawu a M'munsi