Chivumbulutso 5:1-14

5  Kenako, ndinaona mpukutu wolembedwa mkati ndi kunja komwe,+ uli m’dzanja lamanja la Iye wokhala pampando wachifumu.+ Unali womatidwa+ mwamphamvu ndi zidindo 7 zomatira.  Ndipo ndinaona mngelo wamphamvu akulengeza ndi mawu okweza kuti: “Ndani ali woyenera kumatula zidindo zimene amatira mpukutuwu ndi kuutsegula?”  Koma sipanapezeke ndi mmodzi yemwe, kaya kumwamba, padziko lapansi, kapena pansi pa nthaka, wotha kutsegula mpukutuwo kapena kuyang’anamo ndi kuuwerenga.  Choncho ine ndinalira kwambiri chifukwa sipanapezeke wina aliyense woyenera kutsegula mpukutuwo, kapena kuyang’anamo ndi kuuwerenga.+  Koma mmodzi wa akulu aja anandiuza kuti: “Tonthola. Taona! Mkango wa fuko la Yuda,+ muzu+ wa Davide,+ anapambana pa nkhondo+ moti iye ndiye woyenera kumatula zidindo 7 zimene amatira mpukutuwo ndi kuutsegula.”  Kenako ndinaona mwana wa nkhosa+ wooneka ngati wophedwa,+ ataimirira pafupi ndi mpando wachifumu+ uja ndi zamoyo zinayi, ndi pakati pa akulu aja.+ Iye anali ndi nyanga 7, ndi maso 7. Maso amenewo akuimira mizimu 7 ya Mulungu,+ imene yatumizidwa m’dziko lonse lapansi.  Iye anapita, ndipo nthawi yomweyo anatenga mpukutu umene unali kudzanja lamanja la Iye wokhala pampando wachifumu.+  Atatenga mpukutuwo, zamoyo zinayi ndi akulu 24 aja+ anagwada ndi kuwerama pamaso pa Mwanawankhosa. Aliyense wa iwo anali ndi zeze woimbira+ ndi mbale yagolide yodzaza ndi zofukiza. Zofukizazo+ zikuimira mapemphero+ a oyera.  Iwo anali kuimba nyimbo yatsopano,+ yakuti: “Inu ndinu woyenera kutenga mpukutuwo ndi kumatula zidindo zake zomatira, chifukwa munaphedwa, ndipo ndi magazi anu,+ munagula+ anthu kuti atumikire Mulungu.+ Anthu ochokera mu fuko lililonse, chinenero chilichonse, mtundu uliwonse, ndi dziko lililonse. 10  Ndipo munawasandutsa mafumu+ ndi ansembe+ a Mulungu wathu,+ moti adzakhala mafumu+ olamulira dziko lapansi.” 11  Kenako, ndinaona ndi kumva mawu a angelo ambiri atazungulira mpando wachifumu limodzi ndi zamoyo zija ndi akulu aja. Chiwerengero chawo chinali miyanda kuchulukitsa ndi miyanda*+ ndiponso masauzande kuchulukitsa ndi masauzande.+ 12  Iwo anali kunena mofuula kuti: “Mwanawankhosa amene anaphedwa+ ndiye woyenera kulandira mphamvu, chuma, nzeru, nyonga, ulemu, ulemerero, ndi madalitso.”+ 13  Ndipo cholengedwa chilichonse chakumwamba, padziko lapansi,+ pansi pa nthaka, panyanja, ndi zinthu zonse za mmenemo, ndinazimva zikunena kuti: “Iye wokhala pampando wachifumu,+ ndi Mwanawankhosa,+ atamandidwe ndiponso alandire ulemu,+ ulemerero,+ ndi mphamvu, kwamuyaya.” 14  Ndiyeno zamoyo zinayi zija zinati: “Ame!” Ndipo akulu aja+ anagwada n’kuwerama ndi kulambira.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “10,000 kuchulukitsa ndi ma 10,000.”