Aroma 9:1-33

9  Ndikunena zoona+ mwa Khristu, sindikunama ayi.+ Ine pamodzi ndi chikumbumtima changa tikuchitira umboni mwa mzimu woyera,  kuti ndili ndi chisoni chachikulu ndiponso mtima ukundipweteka nthawi zonse.+  Ndikanakonda kuti ineyo ndichotsedwe kwa Khristu monga wotembereredwa m’malo mwa abale anga,+ amene ali anthu a mtundu wanga.+  Amenewa ndi Aisiraeli,+ amene Mulungu anawatenga kukhala ana ake.+ Anawapatsanso ulemerero,+ mapangano,+ Chilamulo,+ utumiki wopatulika+ ndi malonjezo.+  Iwo ndi ana a makolo akale aja.+ Komanso Khristu monga munthu,+ anatuluka pakati pawo. Mulungu,+ amene ndiye wamkulu pa zinthu zonse, atamandike kwamuyaya. Ame.  Komabe, sizili ngati kuti mawu a Mulungu analephera.+ Pakuti si onse ochokera kwa Isiraeli amene alidi “Aisiraeli.”+  Ndiponso si onse amene ali ana chifukwa chongokhala mbewu ya Abulahamu.+ Koma Malemba amati, “Amene adzatchedwa ‘mbewu yako’ adzachokera mwa Isaki.”+  Izi zikutanthauza kuti, si ana akuthupi+ amene alidi ana a Mulungu,+ koma ana a lonjezo+ ndiwo amayesedwa mbewu.  Popeza lonjezo lija linati: “Ndidzabweranso nthawi ngati yomwe ino, ndipo Sara adzakhala ndi mwana wamwamuna.”+ 10  Lonjezolo silinaperekedwe pa nthawi imeneyo yokha ayi, koma linaperekedwanso kwa Rabeka pamene anali ndi pakati pa mapasa+ a Isaki kholo lathu lija. 11  Mapasawo asanabadwe ndiponso asanachite chilichonse chabwino kapena choipa,+ kuti cholinga cha Mulungu powasankha chikhalebe chodalira Iye amene amaitana,+ osati chodalira ntchito, 12  Rabeka anauzidwa kuti: “Wamkulu adzakhala kapolo wa wamng’ono.”+ 13  Monga mmene Malemba amanenera kuti: “Ndinakonda Yakobo, koma Esau ndinadana naye.”+ 14  Ndiye tinene kuti chiyani? Kodi Mulungu alibe chilungamo?+ Ayi si zimenezo! 15  Pakuti iye anauza Mose kuti: “Amene ndikufuna kumusonyeza chifundo, ndidzamusonyeza chifundo, ndipo ndidzamvera chisoni aliyense amene ndikufuna kumumvera chisoni.”+ 16  Chotero, sizidalira munthu wofunayo kapena amene akuthamanga, koma Mulungu,+ amene ali ndi chifundo.+ 17  Pakuti ponena za Farao, Lemba linati: “Ndakusiya ndi moyo kuti ndikusonyeze mphamvu zanga, ndi kuti dzina langa lilengezedwe padziko lonse lapansi.”+ 18  Chotero, iye amachitira chifundo munthu amene wafuna kumuchitira chifundo,+ koma amalola anthu ena kuti aumitse mitima yawo.+ 19  Mwina unganene kwa ine kuti: “N’chifukwa chiyani Mulungu akupezabe anthu zifukwa? Kodi ndani angatsutse chifuniro chake chimene chinanenedwa?”+ 20  Munthu iwe!+ Iweyo ndiwe ndani kuti uziyankhana ndi Mulungu?+ Kodi chinthu choumbidwa chinganene kwa munthu amene anachiumba kuti, “Unandipangiranji motere?”+ 21  Kodi simudziwa kuti woumba mbiya+ ali ndi ufulu woumba chiwiya china cholemekezeka, china chonyozeka kuchokera pa dongo limodzi?+ 22  Bwanji ngati Mulungu analekerera moleza mtima kwambiri ziwiya za mkwiyo zoyenera kuwonongedwa ngakhale kuti akufuna kuonetsa mkwiyo wake ndi mphamvu zake?+ 23  Ndiponso bwanji ngati anachita zimenezo kuti asonyeze kukula kwa ulemerero wake+ kwa ziwiya+ zachifundo, zomwe anazikonzeratu kuti zikhale zaulemerero,+ 24  zimene ndi ifeyo amene anatiitana osati kuchokera mwa Ayuda okha komanso mwa mitundu ina?+ 25  Zilinso monga mmene ananenera m’buku la Hoseya kuti: “Anthu amene si anthu anga+ ndidzawatcha ‘anthu anga,’ ndipo mkazi amene sanali wokondedwa ndidzamutcha ‘wokondedwa.’+ 26  Ndipo pamalo pamene anauzidwapo kuti, ‘Inu sindinu anthu anga,’ pamalo omwewo adzatchedwa ‘ana a Mulungu wamoyo.’”+ 27  Komanso, Yesaya analankhula mofuula zokhudza Isiraeli kuti: “Ngakhale kuti ana a Isiraeli adzakhala ochuluka ngati mchenga wa m’nyanja,+ ndi ochepa okha amene adzapulumuke.+ 28  Pakuti Yehova adzazenga milandu padziko lapansi, ndi kuimaliza yonse mwachangu.”+ 29  Ndiponso, monga Yesaya ananeneratu kuti: “Yehova wa makamu+ akanapanda kutisiyira mbewu, tikanakhala ngati Sodomu, ndipo tikanafanana ndi Gomora.”+ 30  Ndiye tinene kuti chiyani? Tinene kuti, ngakhale kuti anthu a mitundu ina sanatsatire chilungamo, iwo anapeza chilungamo+ chimene chimapezeka chifukwa cha chikhulupiriro.+ 31  Koma ngakhale kuti Aisiraeli anali kutsatira lamulo la chilungamo, sanalipeze lamulolo.+ 32  Chifukwa chiyani? Chifukwa chakuti iwo sanalitsatire mwa chikhulupiriro, koma malinga ndi kuganiza kwawo, analitsatira mwa ntchito.+ Iwo anakhumudwa “pamwala wokhumudwitsa”+ 33  monga mmene Malemba amanenera kuti: “Inetu ndikuika mwala+ wopunthwitsa ndiponso mwala wokhumudwitsa+ m’Ziyoni, koma munthu wokhulupirira mwalawo sadzakhumudwa.”+

Mawu a M'munsi