Aroma 14:1-23

14  Landirani munthu wokhala ndi zofooka m’chikhulupiriro+ chake, koma osagamula pa zoganiza za mumtima mwake.+  Wina ali ndi chikhulupiriro chakuti angadye china chilichonse,+ koma munthu wofooka amadya zamasamba.  Amene amadya, asanyoze amene sadya,+ ndipo wosadyayo asaweruze amene amadya, popeza ameneyo analandiridwa ndi Mulungu.  Ndiwe ndani kuti uweruze wantchito wapakhomo wa mnzako?+ Ndi udindo wa bwana wake kumuweruza kuti ndi wolakwa kapena wosalakwa.+ Komatu Yehova akhoza kumukomera mtima chifukwa angathe kumuthandiza.+  Wina amaona tsiku lina ngati loposa linzake,+ koma wina amaona tsiku lina mofanana ndi masiku ena onse.+ Choncho munthu aliyense akhale wotsimikiza ndi mtima wonse m’maganizo mwake.  Amene amasunga tsiku amalisungira kulemekeza Yehova. Amene amadya, amadya kuti alemekeze Yehova,+ chifukwa amayamika Mulungu.+ Amene sadya, sadya pofuna kulemekeza Yehova,+ chifukwa nayenso amayamika Mulungu.+  Kunena zoona, palibe aliyense wa ife amene amakhala ndi moyo kuti adzilemekeze yekha,+ ndipo palibe amene amafa kuti adzilemekeze yekha.  Pakuti tikakhala ndi moyo, timakhalira moyo Yehova,*+ ndipo tikafa, timafera Yehova.+ Chotero kaya tikhale ndi moyo kapena tife, ndife a Yehova.+  Ndiye chifukwa chake Khristu anafa n’kukhalanso ndi moyo,+ kuti akhale Ambuye wa akufa+ ndiponso wa amoyo.+ 10  Nanga n’chifukwa chiyani umaweruza m’bale wako?+ Kapenanso n’chifukwa chiyani umanyoza m’bale wako? Pakuti tonse tidzaimirira patsogolo pa mpando woweruzira milandu+ wa Mulungu. 11  Malembatu amati: “‘Pali ine Mulungu wamoyo,’ watero Yehova,+ ‘bondo lililonse lidzandigwadira ine, ndipo lilime lililonse lidzavomereza poyera kwa Mulungu.’”+ 12  Chotero aliyense wa ife adzayankha yekha kwa Mulungu.+ 13  Pa chifukwa chimenechi, tisamaweruzane,+ koma m’malomwake tsimikizani mtima+ kuti simuikira m’bale wanu+ chokhumudwitsa+ kapena chopunthwitsa. 14  Ndikudziwa ndipo ndikukhulupirira mwa Ambuye Yesu kuti palibe chakudya chodetsedwa mwa icho chokha.+ Koma ngati munthu akuona chinachake monga chodetsedwa, kwa iyeyo ndi chodetsedwa.+ 15  Chifukwa ngati m’bale wako akuvutika maganizo chifukwa cha chakudya, ndiye kuti simukuyendanso m’chikondi.+ Musawononge* munthu amene Khristu anamufera+ chifukwa cha zakudya zanu. 16  Choncho musalole kuti anthu akunenereni zoipa pa zabwino zimene mukuchita. 17  Pakuti ufumu wa Mulungu+ si kudya ndi kumwa ayi,+ koma chilungamo,+ mtendere+ ndi chimwemwe+ zobwera ndi mzimu woyera. 18  Chifukwa aliyense wotumikira Khristu motere ali wovomerezeka kwa Mulungu ndipo anthu amakondwera naye.+ 19  Choncho, tiyeni titsatire zinthu zobweretsa mtendere+ ndiponso zolimbikitsana.+ 20  Siyani kuwononga ntchito ya Mulungu chifukwa cha zakudya basi.+ Zoonadi, zinthu zonse ndi zoyera, koma munthu amene amadya ngakhale pamene akukhumudwitsa ena, amalakwa.+ 21  Ndi bwino kusadya nyama kapena kusamwa vinyo kapena kusachita kalikonse kamene kamakhumudwitsa m’bale wako.+ 22  Chikhulupiriro chimene uli nacho, khala nacho pakati pa iweyo ndi Mulungu.+ Wodala munthu amene sakudziika pa chiweruzo ndi zinthu zimene wasankha kuchita. 23  Koma ngati akudya ndipo akukayikira, ameneyo watsutsidwa kale,+ chifukwa sakudya mwa chikhulupiriro. Ndithu, chilichonse chochitidwa mosemphana ndi chikhulupiriro ndi tchimo.+

Mawu a M'munsi

Onani Zakumapeto 2.
Kutanthauza kuwononga chikhulupiriro kapena chiyembekezo cha moyo wosatha wa m’tsogolo.