Aroma 11:1-36

11  Ndiye ndifunse kuti, kodi Mulungu anakana anthu ake?+ Ayi ndithu! Paja inenso ndine Mwisiraeli,+ wa mbewu ya Abulahamu, wa fuko la Benjamini.+  Mulungu sanakane anthu ake amene anali oyambirira kuwavomereza.+ Kodi ndithu simukudziwa kuti Lemba limati chiyani za Eliya, pamene anali kuchonderera Mulungu motsutsa Aisiraeli?+ Limati:  “Yehova, iwo apha aneneri anu, agumula maguwa anu ansembe, moti ine ndatsala ndekhandekha. Tsopano akufunafuna moyo wanga.”+  Koma kodi mawu a Mulungu+ anati chiyani kwa iyeyo? Anati: “Ndadzisungira anthu 7,000, amene sanagwadire Baala.”+  Chotero, pa nthawi ino alipo ena ochepa+ amene anasankhidwa+ mwa kukoma mtima kwakukulu.  Ndiyetu ngati anasankhidwa mwa kukoma mtima kwakukulu,+ sanasankhidwe chifukwa cha ntchito zawo ayi.+ Zitati zitero, kukoma mtima kumeneko sikungakhalenso kukoma mtima kwakukulu.+  Ndiye zili bwanji pamenepa? Chimene Aisiraeli akuchifunitsitsa sanachipeze,+ koma anthu osankhidwa+ ndi amene anachipeza. Enawo anaumitsa mitima yawo+  monga mmene Malemba amanenera kuti: “Mulungu wawapatsa mzimu wa tulo tatikulu,+ maso osaona ndi makutu osatha kumva, kufikira lero.”+  Ndiponso Davide anati: “Tebulo lawo likhale msampha, mbuna, chopunthwitsa ndi chilango kwa iwo.+ 10  Maso awo achite mdima kuti asaone, ndipo weramitsani msana wawo nthawi zonse.”+ 11  Ndiyeno ndifunse, Kodi anapunthwa mpaka kugweratu?+ Ayi! Koma chifukwa cha kulakwa kwawo+ pali chipulumutso kwa anthu a mitundu ina,+ kuti olakwawo achite nsanje.+ 12  Chotero ngati kulakwa kwawo kukutanthauza chuma ku dziko, ndipo kuchepa kwawo kukutanthauza chuma kwa anthu a mitundu ina,+ bwanji nanga za chiwerengero chawo chokwanira?+ Chidzatanthauzatu zazikulu kuposa pamenepo! 13  Tsopano ndikulankhula kwa inu ochokera m’mitundu ina. Malinga n’kuti ndine mtumwi+ weniweni wotumidwa kwa mitundu ina,+ ndimalemekeza+ utumiki wanga,+ 14  kuti mwina ndingapangitse anthu a mtundu wanga kuchita nsanje ndi kupulumutsapo+ ena a iwo.+ 15  Chifukwa ngati dziko layanjidwa ndi Mulungu chifukwa chakuti iwo anatayidwa,+ ndiye kuti akadzalandiridwa+ zidzatanthauza moyo kuchokera ku imfa. 16  Ndiponso, ngati mbali ya mtanda imene yadyedwa monga chipatso choyambirira+ ili yoyera, ndiye kuti mtanda wonse ndi woyeranso. Ngati muzu uli woyera,+ ndiye kuti nthambi nazonso ndi zoyera. 17  Ngati nthambi zina zinadulidwa, koma iwe ngakhale kuti ndiwe nthambi ya mtengo wa maolivi wam’tchire, unalumikizidwa pakati pa nthambi zotsala+ ndipo unayamba kugawana nawo muzu wamafuta+ wa mtengo wa maoliviwo,+ 18  usakondwere monyoza nthambi zimene zinadulidwazo. Koma ngati ukunyoza nthambizo,+ kumbukira kuti si iwe amene ukuchirikiza muzu,+ koma muzu ndi umene ukuchirikiza iweyo.+ 19  Komatu tsopano unganene kuti: “Nthambi zina zinadulidwa+ kuti alumikizepo ine.”+ 20  N’zoonadi! Iwo anadulidwa chifukwa chakuti analibe chikhulupiriro,+ koma iweyo waimirira chifukwa cha chikhulupiriro.+ Taya maganizo odzikuzawo,+ koma khala ndi mantha.+ 21  Pakuti ngati Mulungu sanalekerere nthambi zachilengedwe, sadzakulekereranso iweyo.+ 22  Choncho taona kukoma mtima+ komanso kusalekerera+ kwa Mulungu. Amene anagwa anaona kusalekerera+ kwake, koma iweyo ukuona kukoma mtima kwa Mulungu, malinga ngati ukukhalabe+ m’kukoma mtima kwake. Apo ayi, iwenso udzadulidwa.+ 23  Iwonso ngati angayambe kukhala ndi chikhulupiriro, adzalumikizidwa kumtengowo,+ pakuti Mulungu akhoza kuwalumikizanso. 24  Ngati iweyo unadulidwa kumtengo wa maolivi umene mwachilengedwe umamera m’tchire, ndipo mosemphana ndi chilengedwe, unalumikizidwa+ kumtengo wa maolivi wolimidwa, kodi si kwapafupi kulumikiza nthambi izi kumtengo wawo umene zinadulidwako?+ 25  Pakuti sindikufuna kuti mukhale osadziwa abale za chinsinsi chopatulika+ chimenechi, kuopera kuti mungadzione ngati ochenjera. Chinsinsi chopatulikacho n’chakuti ena mu Isiraeli aumitsa mitima yawo+ mpaka chiwerengero chonse+ cha anthu ochokera m’mitundu ina chitakwanira.+ 26  Mwa njira imeneyi, Aisiraeli onse+ adzapulumuka. Izi zikugwirizana ndi zimene Malemba amanena kuti: “Wolanditsa adzachokera m’Ziyoni+ ndi kuchotsera Yakobo zochita zonse zosalemekeza Mulungu.+ 27  Limeneli lidzakhala pangano langa ndi iwo,+ pamene ndidzawachotsera machimo awo.”+ 28  Zoonadi, pa nkhani ya uthenga wabwino iwo ndi adani a Mulungu, ndipo zimenezi zapindulitsa inu.+ Koma kunena za kusankha kwa Mulungu, iwo ndi okondedwa ake chifukwa cha makolo awo oyambirira.+ 29  Mulungu sadzadandaula+ chifukwa cha mphatso zake ndiponso chifukwa chakuti anawaitana. 30  Pakuti monga mmene inuyo munalili osamvera+ Mulungu koma tsopano mwasonyezedwa chifundo+ chifukwa cha kusamvera kwawo,+ 31  iwowa tsopano akhala osamvera, zimene zapangitsa kuti inuyo musonyezedwe chifundo,+ kuti iwonso tsopano asonyezedwe chifundo. 32  Popeza Mulungu walola onse kuti akhale akaidi a kusamvera,+ kuti onsewo awasonyeze chifundo.+ 33  Ndithudi, madalitso amene Mulungu amapereka ndi ochuluka kwambiri.+ Nzeru+ zake n’zozama, ndiponso iye ndi wodziwa zinthu kwambiri.+ Ziweruzo zake ndi zosasanthulika,+ ndipo ndani angatulukire njira zake? 34  Pakuti “ndani akudziwa maganizo a Yehova,+ kapena ndani angakhale phungu wake?”+ 35  Kapenanso, “Ndani anayamba kumupatsa kanthu, kuti amubwezere?”+ 36  Chifukwa zinthu zonse zimachokera kwa iye ndipo iye ndi amene anazipanga ndiponso ndi zake.+ Ulemerero ukhale wake kwamuyaya.+ Ame.

Mawu a M'munsi