Aroma 1:1-32
1 Ndine Paulo kapolo+ wa Yesu Khristu, woitanidwa+ kuti ndikhale mtumwi,+ ndiponso wosankhidwa kuti ndilalikire uthenga wabwino wa Mulungu.+
2 Uthenga umenewu anaulonjeza kalekale kudzera mwa aneneri+ ake m’Malemba oyera.
3 Uthengawo umanena za Mwana wake, amene anatuluka m’mbewu ya Davide+ monga munthu,+
4 koma amene Mulungu mwa mphamvu+ yake anam’lengeza kukhala Mwana wake+ mwa mzimu woyera+ pomuukitsa kwa akufa.+ Ameneyu ndi Yesu Khristu Ambuye wathu.
5 Kudzera mwa iyeyu, tinalandira kukoma mtima+ kwakukulu ndiponso ndinasankhidwa kukhala mtumwi+ kuti mitundu yonse ikhale yomvera mwa chikhulupiriro+ chifukwa cha dzina lake.
6 Pakati pa mitundu imeneyo palinso inuyo amene munaitanidwa kuti mukhale ake a Yesu Khristu.
7 Ndikulembera inu nonse amene muli ku Roma monga okondedwa a Mulungu, oitanidwa+ kukhala oyera:+
Kukoma mtima kwakukulu ndi mtendere+ wochokera kwa Mulungu Atate wathu ndi Ambuye wathu Yesu Khristu+ zikhale ndi inu.
8 Choyamba, ndikuyamika+ Mulungu wanga kudzera mwa Yesu Khristu chifukwa cha nonsenu, pakuti chikhulupiriro chanu chikusimbidwa+ m’dziko lonse.
9 Mulungu, amene ndikumuchitira utumiki wopatulika ndi moyo wanga wonse polalikira uthenga wabwino wonena za Mwana wake, ndiye mboni yanga+ ya mmene ndimakutchulirani m’mapemphero anga nthawi zonse.+
10 Ndimamupempha kuti ngati n’kotheka mwa chifuniro+ chake, ulendo uno wokha ndibwere kwanuko.
11 Popeza ndikulakalaka kukuonani+ kuti ndikugawireni mphatso+ inayake yauzimu kuti mukhale olimba,
12 kapena kuti tidzalimbikitsane+ mwa chikhulupiriro, chanu ndi changa.+
13 Koma sindikufuna kuti mukhale osadziwa abale,+ kuti nthawi zambiri ndinkafuna kubwera kwanuko,+ koma pakhala zondilepheretsa mpaka pano. Ndikufuna kuti ndidzapeze zipatso+ pakati pa inu monganso ndinachitira pakati pa mitundu ina yonse.
14 Ineyo ndili ndi ngongole kwa Agiriki, kwa anthu amene si Agiriki, kwa anthu anzeru+ ndi kwa opusa.
15 Chotero ndikufunitsitsa kudzalengeza uthenga wabwino+ kwa inunso kumeneko ku Roma.+
16 Pakuti sindichita nawo manyazi+ uthenga wabwino. Kunena zoona, uthengawo ndi mphamvu+ ya chipulumutso imene Mulungu amaipereka kwa aliyense amene ali ndi chikhulupiriro,+ choyamba kwa Myuda+ kenako kwa Mgiriki.+
17 Mu uthenga wabwinowu, chilungamo+ cha Mulungu chimaululidwa chifukwa cha chikhulupiriro cha munthu.+ Zikatero, chikhulupiriro cha munthuyo chimalimbanso monga mmene Malemba amanenera kuti: “Koma wolungama adzakhala ndi moyo mwa chikhulupiriro chake.”+
18 Mkwiyo wa Mulungu+ ukusonyezedwa kuchokera kumwamba pa anthu onse osaopa Mulungu ndi ochita zosalungama+ amene akupondereza choonadi+ m’njira yosalungama.+
19 Chifukwa chake n’chakuti, zimene anthu angathe kudziwa ponena za Mulungu zikuonekera pakati pawo,+ popeza Mulungu anazisonyeza kwa iwo.+
20 Chilengedwere dziko kupita m’tsogolo,+ makhalidwe a Mulungu osaoneka+ ndi maso akuonekera bwino. Makhalidwe a Mulungu amenewa, ngakhalenso mphamvu zake zosatha+ ndiponso Umulungu+ wake, zikuonekera m’zinthu zimene anapanga+ moti anthuwo alibenso chifukwa chomveka chosakhulupirira kuti kuli Mulungu.+
21 Chifukwa chakuti, ngakhale anam’dziwa Mulungu, iwo sanam’patse ulemerero monga Mulungu kapena kumuyamikira.+ M’malomwake anayamba kulingalira zinthu zopanda pake+ ndipo mtima wawo wopusawo unachita mdima.+
22 Ngakhale anali kunena motsimikiza kuti ndi anzeru, iwo anakhala opusa+
23 ndipo anasandutsa ulemerero+ wa Mulungu amene sawonongeka kukhala ngati chifaniziro+ cha munthu, mbalame, zolengedwa za miyendo inayi ndi zokwawa,+ zonsezo zimene zimawonongeka.
24 Chotero malinga ndi zilakolako za m’mitima mwawo, Mulungu anawasiya kuti achite zonyansa,+ kuti matupi awo+ achitidwe chipongwe.+
25 Anateronso kwa anthu amene anasinthanitsa choonadi+ cha Mulungu ndi bodza+ polambira chilengedwe ndi kuchichitira utumiki wopatulika m’malo mochita zimenezo kwa Iye amene anazilenga, amene ndi wotamandika kosatha. Ame.
26 Ndiye chifukwa chake Mulungu anawasiya kuti atsatire zilakolako zamanyazi za kugonana,+ popeza akazi pakati pawo anasiya njira yachibadwa ya matupi awo n’kumachita zosemphana ndi chibadwa.+
27 Amunanso chimodzimodzi. Iwo anasiya njira yachibadwa yofuna akazi+ n’kumatenthetsana okhaokha mwachiwawa m’chilakolako choipa, amuna ndi amuna anzawo,+ kuchitirana zonyansa+ ndi kulandiriratu mphoto+ yoyenerera kulakwa kwawo.+
28 Ndiponso monga mmene iwo sanafunire kumudziwa Mulungu molondola,+ iye anawasiya ndi maganizo awo oipa,+ kuti azichita zinthu zosayenerazo,+
29 popeza anadzazidwa ndi zosalungama+ zonse, kuipa+ konse, kusirira konse kwa nsanje,+ ndi uchimo+ wonse. Mtima wawo unadzala kaduka,+ umbanda,+ ndewu,+ chinyengo+ ndi njiru.+ Anakonda manong’onong’o+
30 ndi miseche.+ Anakhala odana ndi Mulungu, achipongwe,+ odzikweza,+ odzimva,+ oyambitsa zoipa,+ osamvera makolo,+
31 osazindikira,+ osasunga mapangano,+ opanda chikondi chachibadwa+ ndiponso opanda chifundo.+
32 Amenewa ngakhale kuti amalidziwa bwino lamulo lolungama la Mulungu,+ lakuti amene amachita zinthu zimenezi n’ngoyenera imfa,+ iwo amapitiriza kuzichita. Kuwonjezera apo, amagwirizananso+ ndi anthu amene amachita zimenezo.